< Zekariya 9 >

1 Mawu a Yehova odzudzula dziko la Hadiraki ndi mzinda wa Damasiko pakuti maso a anthu ndiponso mafuko onse a Israeli ali pa Yehova—
Nkɔmhyɛ: Awurade asɛm tia Hadrak asase na ɛbɛka Damasko efisɛ, nnipa ne Israel mmusuakuw nyinaa ani wɔ Awurade so.
2 ndiponso mzinda wa Hamati, umene ukuchita malire ndi dzikoli, komanso pa Turo ndi Sidoni, ngakhale kuti iwo ndi anzeru kwambiri.
Na ɛbɛka Hamat a ɔne no bɔ hye, ɛbɛka Tiro ne Sidon, ɛwɔ mu sɛ wɔyɛ anyansafo.
3 Ndipo Turo anadzimangira linga; wadziwunjikira siliva ngati fumbi, ndi golide ngati zinyalala za mʼmisewu.
Tiro asi abandennen ama ne ho; waboa dwetɛ ano te sɛ mfutuma, ne sikakɔkɔɔ ano te sɛ dɔte a ɛwɔ mmɔnten so.
4 Taonani Ambuye adzamulanda chuma chakecho ndi kuwononga mphamvu zake mʼnyanja, ndipo adzapserera ndi moto.
Nanso Awurade begye nʼahode nyinaa na wasɛe ne tumi a ɔwɔ wɔ po so, na wɔde ogya bɛhyew no dwerɛbee.
5 Mzinda wa Asikeloni udzaona zimenezi, nʼkuchita mantha; Gaza adzanjenjemera ndi ululu, chimodzimodzinso Ekroni, chifukwa chiyembekezo chake chidzatheratu. Mfumu ya ku Gaza idzaphedwa ndipo Asikeloni adzakhala opanda anthu.
Askelon behu na wasuro Gasa de ɔyaw bebubu ne mu, na Ekron nso saa ara, efisɛ nʼanidaso bɛsa. Gasa bɛhwere ne hene na wobegyaw Askelon ofituw.
6 Mu Asidodi mudzakhala mlendo, ndipo ndidzathetsa kunyada kwa Afilisti.
Ananafo bɛtena Asdod, na metwa Filistifo ahantan agu.
7 Ndidzachotsa nyama ya magazi mʼkamwa mwawo, chakudya choletsedwa mʼmano mwawo. Amene atsala adzakhala anthu a Mulungu wathu, adzasanduka atsogoleri mu Yuda, ndipo Ekroni adzakhala ngati Ayebusi.
Meyi mogya afi wɔn ano, akyiwade nnuan nso meyi afi wɔn ano. Nkae no bɛyɛ yɛn Nyankopɔn de; wɔbɛyɛ Yuda ntuanofo, na Ekron bɛyɛ sɛ Yebusifo.
8 Koma Ine ndidzalondera Nyumba yanga ndi kuyiteteza kwa ankhondo osakaza. Palibenso mdani amene adzagonjetse anthu anga, pakuti tsopano ndikuwayangʼanira.
Nanso mɛbɔ me Fi ho ban wɔ wɔn a wɔtetɛw bɔ korɔn ho. Ɔhyɛsoni biara ntumi mfa me nkurɔfo so bio, efisɛ afei merewɛn.
9 Sangalala kwambiri, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni! Fuwula, mwana wamkazi wa Yerusalemu! Taona, mfumu yako ikubwera kwa iwe, yolungama ndi yogonjetsa adani, yodzichepetsa ndi yokwera pa bulu, pa mwana wamphongo wa bulu.
Di ahurusi, Ɔbabea Sion! Teɛ mu, Ɔbabea Yerusalem! Hwɛ, wo hene reba wo nkyɛn. Ɔteɛ na ɔwɔ nkwagye, odwo, na ɔte afurum so, afurum ba so na ɔte.
10 Ndidzachotsa magaleta ankhondo ku Efereimu ndi akavalo ankhondo ku Yerusalemu, ndipo uta wankhondo udzathyoka. Mfumuyo idzabweretsa mtendere pakati pa mitundu ya anthu. Ulamuliro wake udzayambira ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina, ndipo kuchokera ku Mtsinje (Yufurate) mpaka ku malekezero a dziko lapansi.
Megye nteaseɛnam afi Efraim ne akofo apɔnkɔ afi Yerusalem, na akodi tadua no wobebubu mu. Ɔbɛpae mu aka asomdwoe nsɛm akyerɛ aman no. Nʼahenni befi po akɔka po; ebefi Asubɔnten no akɔpem nsase ano.
11 Tsono kunena za iwe, chifukwa cha magazi a pangano lako ndi Ine, ndidzamasula amʼndende ako, ndidzawatulutsa mʼdzenje lopanda madzi.
Na wo de, esiane me ne wo mogya apam no nti, meyi wo nneduafo afi amoa a nsu nni mu mu.
12 Bwererani ku malo anu otetezedwa, inu amʼndende achiyembekezo; ngakhale tsopano ndikulengeza kuti ndidzakubwezerani zabwino mowirikiza.
Monsan nkɔ mʼaban mu, nneduafo a mowɔ anidaso; mprempren mpo merebɔ mo nkae sɛ mɛhyɛ mo anan mu mmɔho.
13 Ndidzakoka Yuda monga ndimakokera uta wanga, ndipo Efereimu ndiye muvi wake. Ndidzadzutsa ana ako iwe Ziyoni, kulimbana ndi ana ako iwe Grisi, ndipo ndidzakusandutsa iwe lupanga la munthu wankhondo.
Mɛkom Yuda sɛnea mikuntun me tadua na mede Efraim bɛhyɛ mu. Mɛkanyan wo mmabarima, Sion, atia wo Hela mmabarima, na mɛyɛ wo sɛ ɔkofo afoa.
14 Pamenepo Yehova adzaonekera kwa anthu ake; mivi yake idzangʼanima ngati chingʼaningʼani. Ambuye Yehova adzaliza lipenga; ndipo adzayenda mu mkuntho wochokera kummwera,
Afei Awurade bɛda ne ho adi wɔ wɔn so; nʼagyan betwa yerɛw te sɛ anyinam. Otumfo Awurade bɛhyɛn torobɛnto no; ɔbɛbɔ nsra wɔ atɔe fam ahum mu,
15 ndipo Yehova Wamphamvuzonse adzawateteza. Iwo adzawononga ndipo adzagonjetsa ndi miyala ya legeni. Adzamwa magazi ndi kubangula ngati amwa vinyo; magazi adzayenderera ngati a mʼmbale yowazira magazi pa ngodya za guwa lansembe.
Asafo Awurade bɛkata wɔn so. Wɔde ahwimmo bɛsɛe na wɔde adi nkonim. Wɔbɛnom na wɔabobɔ mu sɛnea wɔanom nsa; wɔbɛyɛ ma te sɛ kuruwa a wɔde pete afɔremuka ntwea so.
16 Tsiku limenelo Yehova Mulungu wawo adzawapulumutsa pakuti anthu ake ali ngati nkhosa. Adzanyezimira mʼdziko lake ngati miyala yokongola pa chipewa chaufumu.
Awurade wɔn Nyankopɔn, begye wɔn saa da no sɛ oguanhwɛfo gye ne nguan. Wobetwa yerɛw yerɛw wɔ nʼasase so, sɛ abohemaa a ɛbobɔ ahenkyɛw ho.
17 Taonani chikoka ndi kukongola kwawo! Tirigu adzasangalatsa anyamata, ndi vinyo watsopano anamwali.
Sɛnea wɔn ho betwa na wɔn ho ayɛ fɛ afa! Aduan bɛma mmerante anyin ahoɔden so na nsa foforo bɛma mmabaa anyin saa ara.

< Zekariya 9 >