< Zekariya 9 >

1 Mawu a Yehova odzudzula dziko la Hadiraki ndi mzinda wa Damasiko pakuti maso a anthu ndiponso mafuko onse a Israeli ali pa Yehova—
Sentence Parole de Yahweh contre le pays d’Hadrach; et à Damas sera son séjour, — car Yahweh a l’œil sur les hommes, et sur toutes les tribus d’Israël; —
2 ndiponso mzinda wa Hamati, umene ukuchita malire ndi dzikoli, komanso pa Turo ndi Sidoni, ngakhale kuti iwo ndi anzeru kwambiri.
et aussi à Hamath, voisine de Damas, à Tyr, ainsi qu’à Sidon, parce que leur sagesse est grande.
3 Ndipo Turo anadzimangira linga; wadziwunjikira siliva ngati fumbi, ndi golide ngati zinyalala za mʼmisewu.
Tyr s’est construit une citadelle, elle a amassé l’argent comme la poussière, et l’or comme la boue des rues.
4 Taonani Ambuye adzamulanda chuma chakecho ndi kuwononga mphamvu zake mʼnyanja, ndipo adzapserera ndi moto.
Voici que le Seigneur s’en emparera; il frappera sur mer sa puissance, et elle-même sera dévorée par le feu.
5 Mzinda wa Asikeloni udzaona zimenezi, nʼkuchita mantha; Gaza adzanjenjemera ndi ululu, chimodzimodzinso Ekroni, chifukwa chiyembekezo chake chidzatheratu. Mfumu ya ku Gaza idzaphedwa ndipo Asikeloni adzakhala opanda anthu.
Ascalon le verra et craindra; Gaza aussi, et elle se tordra de douleur; Accaron aussi, car son espérance est confondue. Il n’y aura plus de roi à Gaza, et Ascalon ne sera plus habitée.
6 Mu Asidodi mudzakhala mlendo, ndipo ndidzathetsa kunyada kwa Afilisti.
Un vil étranger s’installera à Azoth, et je détruirai l’orgueil des Philistins.
7 Ndidzachotsa nyama ya magazi mʼkamwa mwawo, chakudya choletsedwa mʼmano mwawo. Amene atsala adzakhala anthu a Mulungu wathu, adzasanduka atsogoleri mu Yuda, ndipo Ekroni adzakhala ngati Ayebusi.
J’ôterai son sang de sa bouche, et ses abominations d’entre ses dents; et lui aussi sera un reste pour notre Dieu; il sera comme un chefen Juda; et Accaron sera comme le Jébuséen.
8 Koma Ine ndidzalondera Nyumba yanga ndi kuyiteteza kwa ankhondo osakaza. Palibenso mdani amene adzagonjetse anthu anga, pakuti tsopano ndikuwayangʼanira.
Je camperai autour de ma maison pour la défendre; contre toute armée, tout allant et venant; et il ne passera plus chez eux d’oppresseur, car maintenant j’ai vu de mes yeux.
9 Sangalala kwambiri, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni! Fuwula, mwana wamkazi wa Yerusalemu! Taona, mfumu yako ikubwera kwa iwe, yolungama ndi yogonjetsa adani, yodzichepetsa ndi yokwera pa bulu, pa mwana wamphongo wa bulu.
Tressaille d’une grande joie, fille de Sion! Pousse des cris d’allégresse, fille de Jérusalem! Voici que ton Roi vient à toi; il est juste, lui, et protégé de Dieu; il est humble; monté sur un âne, et sur un poulain, petit d’une ânesse.
10 Ndidzachotsa magaleta ankhondo ku Efereimu ndi akavalo ankhondo ku Yerusalemu, ndipo uta wankhondo udzathyoka. Mfumuyo idzabweretsa mtendere pakati pa mitundu ya anthu. Ulamuliro wake udzayambira ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina, ndipo kuchokera ku Mtsinje (Yufurate) mpaka ku malekezero a dziko lapansi.
Je retrancherai d’Ephraïm les chars de guerre, et de Jérusalem les chevaux, et l’arc du combat sera détruit. Il parlera de paix aux nations; sa domination s’étendra d’une mer à l’autre, du fleuve jusqu’aux extrémités de la terre.
11 Tsono kunena za iwe, chifukwa cha magazi a pangano lako ndi Ine, ndidzamasula amʼndende ako, ndidzawatulutsa mʼdzenje lopanda madzi.
Pour toi aussi, à cause du sang de ton alliance, je retirerai tes captifs de la fosse sans eau.
12 Bwererani ku malo anu otetezedwa, inu amʼndende achiyembekezo; ngakhale tsopano ndikulengeza kuti ndidzakubwezerani zabwino mowirikiza.
Revenez au lieu fort, captifs d’espérance! Aujourd’hui encore je le déclare: je te rendrai au double.
13 Ndidzakoka Yuda monga ndimakokera uta wanga, ndipo Efereimu ndiye muvi wake. Ndidzadzutsa ana ako iwe Ziyoni, kulimbana ndi ana ako iwe Grisi, ndipo ndidzakusandutsa iwe lupanga la munthu wankhondo.
Car je bande pour moi Juda, et sur l’arc je place Ephraïm; j’exciterai tes fils, ô Sion, contre tes fils, ô Javan, et je ferai de toi comme une épée de vaillant.
14 Pamenepo Yehova adzaonekera kwa anthu ake; mivi yake idzangʼanima ngati chingʼaningʼani. Ambuye Yehova adzaliza lipenga; ndipo adzayenda mu mkuntho wochokera kummwera,
Yahweh apparaîtra au-dessus d’eux, sa flèche partira comme l’éclair; le Seigneur Yahweh sonnera de la trompette, et s’avancera dans les ouragans du midi.
15 ndipo Yehova Wamphamvuzonse adzawateteza. Iwo adzawononga ndipo adzagonjetsa ndi miyala ya legeni. Adzamwa magazi ndi kubangula ngati amwa vinyo; magazi adzayenderera ngati a mʼmbale yowazira magazi pa ngodya za guwa lansembe.
Yahweh des armées les protégera; Ils dévoreront, ils fouleront aux pieds les pierres de fronde; Ils boiront, ils se démèneront comme pris de vin, et ils seront remplis comme la coupe des sacrifices, comme les cornes de l’autel.
16 Tsiku limenelo Yehova Mulungu wawo adzawapulumutsa pakuti anthu ake ali ngati nkhosa. Adzanyezimira mʼdziko lake ngati miyala yokongola pa chipewa chaufumu.
Yahweh leur Dieu sera leur salut en ce jour-là, le salut du troupeau qui est son peuple; ils seront comme des pierres de diadème, qui brilleront dans son pays.
17 Taonani chikoka ndi kukongola kwawo! Tirigu adzasangalatsa anyamata, ndi vinyo watsopano anamwali.
Quelle prospérité, quelle beauté que la leur! Le froment fera croître les jeunes gens, et le vin nouveau les vierges.

< Zekariya 9 >