< Zekariya 9 >
1 Mawu a Yehova odzudzula dziko la Hadiraki ndi mzinda wa Damasiko pakuti maso a anthu ndiponso mafuko onse a Israeli ali pa Yehova—
The prophecy of the word of Jehovah is against the land of Hadrach, And upon Damascus shall it come down, For the eye of Jehovah is over man, And over all the tribes of Israel,
2 ndiponso mzinda wa Hamati, umene ukuchita malire ndi dzikoli, komanso pa Turo ndi Sidoni, ngakhale kuti iwo ndi anzeru kwambiri.
And against Hamath, which bordereth thereon, And Tyre and Sidon, though she be very wise.
3 Ndipo Turo anadzimangira linga; wadziwunjikira siliva ngati fumbi, ndi golide ngati zinyalala za mʼmisewu.
Though Tyre hath built her a fortress, And hath heaped up silver as dust, And fine gold as the mire of the streets,
4 Taonani Ambuye adzamulanda chuma chakecho ndi kuwononga mphamvu zake mʼnyanja, ndipo adzapserera ndi moto.
Behold, the Lord will cast her out, And will smite her power into the sea, And she shall be devoured by fire.
5 Mzinda wa Asikeloni udzaona zimenezi, nʼkuchita mantha; Gaza adzanjenjemera ndi ululu, chimodzimodzinso Ekroni, chifukwa chiyembekezo chake chidzatheratu. Mfumu ya ku Gaza idzaphedwa ndipo Asikeloni adzakhala opanda anthu.
Askelon shall see it and fear, Gaza also shall see and tremble, And Ekron, because her expectation shall be put to shame. The king shall perish from Gaza, And Askelon shall not be inhabited.
6 Mu Asidodi mudzakhala mlendo, ndipo ndidzathetsa kunyada kwa Afilisti.
And strangers shall dwell in Ashdod, And I will cut off the pride of the Philistines.
7 Ndidzachotsa nyama ya magazi mʼkamwa mwawo, chakudya choletsedwa mʼmano mwawo. Amene atsala adzakhala anthu a Mulungu wathu, adzasanduka atsogoleri mu Yuda, ndipo Ekroni adzakhala ngati Ayebusi.
And I will take away his blood out of his mouth, And his abominations from between his teeth; And even he shall be left for our God, And he shall be as a governor in Judah, And Ekron as a Jebusite.
8 Koma Ine ndidzalondera Nyumba yanga ndi kuyiteteza kwa ankhondo osakaza. Palibenso mdani amene adzagonjetse anthu anga, pakuti tsopano ndikuwayangʼanira.
And I will encamp about my house, as a garrison, Against him that passeth by and him that returneth, And no oppressor shall pass through them any more; For now have I seen with my own eyes.
9 Sangalala kwambiri, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni! Fuwula, mwana wamkazi wa Yerusalemu! Taona, mfumu yako ikubwera kwa iwe, yolungama ndi yogonjetsa adani, yodzichepetsa ndi yokwera pa bulu, pa mwana wamphongo wa bulu.
Rejoice greatly, daughter of Zion, Shout, daughter of Jerusalem! Behold, thy king cometh to thee; He is just and victorious, Mild, and riding upon an ass, Even upon a colt, the foal of an ass.
10 Ndidzachotsa magaleta ankhondo ku Efereimu ndi akavalo ankhondo ku Yerusalemu, ndipo uta wankhondo udzathyoka. Mfumuyo idzabweretsa mtendere pakati pa mitundu ya anthu. Ulamuliro wake udzayambira ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina, ndipo kuchokera ku Mtsinje (Yufurate) mpaka ku malekezero a dziko lapansi.
And I will cut off the chariot from Ephraim, And the horse from Jerusalem; And the battle-bow shall be cut off. And he shall speak peace to the nations; And his dominion shall be from sea to sea, And from the river to the ends of the earth.
11 Tsono kunena za iwe, chifukwa cha magazi a pangano lako ndi Ine, ndidzamasula amʼndende ako, ndidzawatulutsa mʼdzenje lopanda madzi.
As for thee also, on account of thy blood-sealed covenant, I will set thy prisoners free from the pit wherein is no water.
12 Bwererani ku malo anu otetezedwa, inu amʼndende achiyembekezo; ngakhale tsopano ndikulengeza kuti ndidzakubwezerani zabwino mowirikiza.
Return ye to the strong-hold, ye prisoners of hope! Even this day do I declare it: I will restore double unto thee.
13 Ndidzakoka Yuda monga ndimakokera uta wanga, ndipo Efereimu ndiye muvi wake. Ndidzadzutsa ana ako iwe Ziyoni, kulimbana ndi ana ako iwe Grisi, ndipo ndidzakusandutsa iwe lupanga la munthu wankhondo.
For I will bend Judah as a bow for myself; As a bow will I extend Ephraim to the utmost; And I will raise up thy sons, O Zion, Against thy sons, O Greece, And make thee as the sword of a mighty man.
14 Pamenepo Yehova adzaonekera kwa anthu ake; mivi yake idzangʼanima ngati chingʼaningʼani. Ambuye Yehova adzaliza lipenga; ndipo adzayenda mu mkuntho wochokera kummwera,
And Jehovah shall be seen over them. And his arrow shall go forth as lightning; And the Lord Jehovah shall blow the trumpet, And shall go forth with whirlwinds of the South.
15 ndipo Yehova Wamphamvuzonse adzawateteza. Iwo adzawononga ndipo adzagonjetsa ndi miyala ya legeni. Adzamwa magazi ndi kubangula ngati amwa vinyo; magazi adzayenderera ngati a mʼmbale yowazira magazi pa ngodya za guwa lansembe.
Jehovah of hosts shall defend them; And they shall devour, and trample under feet the sling-stones, And they shall drink, and shout as through wine, And they shall be filled like a bowl, like the corners of the altar.
16 Tsiku limenelo Yehova Mulungu wawo adzawapulumutsa pakuti anthu ake ali ngati nkhosa. Adzanyezimira mʼdziko lake ngati miyala yokongola pa chipewa chaufumu.
And Jehovah, their God, shall save them in that day; He will save his people as a flock; For they shall be as the stones of a crown, lifting themselves up in his land.
17 Taonani chikoka ndi kukongola kwawo! Tirigu adzasangalatsa anyamata, ndi vinyo watsopano anamwali.
How great shall be their prosperity, and how great their beauty! Corn shall make the young men thrive, and new wire the maidens.