< Zekariya 9 >
1 Mawu a Yehova odzudzula dziko la Hadiraki ndi mzinda wa Damasiko pakuti maso a anthu ndiponso mafuko onse a Israeli ali pa Yehova—
Herrens Ords Profeti er over Kadraks Land, og Damaskus er dets Hvilested — thi Herren har Øje med Mennesker og med alle Israels Stammer —
2 ndiponso mzinda wa Hamati, umene ukuchita malire ndi dzikoli, komanso pa Turo ndi Sidoni, ngakhale kuti iwo ndi anzeru kwambiri.
ogsaa Hamath, som grænser dertil, Tyrus og Zidon; thi den er saare viis.
3 Ndipo Turo anadzimangira linga; wadziwunjikira siliva ngati fumbi, ndi golide ngati zinyalala za mʼmisewu.
Og Tyrus byggede sig en Fæstning og sankede Sølv som Støv og Guld som Dynd paa Gaderne.
4 Taonani Ambuye adzamulanda chuma chakecho ndi kuwononga mphamvu zake mʼnyanja, ndipo adzapserera ndi moto.
Se, Herren, skal indtage den og slaa dens Magt paa Havet, og den selv skal fortæres af Ilden.
5 Mzinda wa Asikeloni udzaona zimenezi, nʼkuchita mantha; Gaza adzanjenjemera ndi ululu, chimodzimodzinso Ekroni, chifukwa chiyembekezo chake chidzatheratu. Mfumu ya ku Gaza idzaphedwa ndipo Asikeloni adzakhala opanda anthu.
Askalon skal se det og frygte, ligesaa Gaza, og den skal vorde saare bange, samt Ekron; thi dens Haab er blevet til Skamme; og Gaza skal miste sin Konge, og Askalon skal ikke bebos.
6 Mu Asidodi mudzakhala mlendo, ndipo ndidzathetsa kunyada kwa Afilisti.
Og der skal bo Horebørn i Asdod, og Jeg vil udrydde Filisternes Hovmod.
7 Ndidzachotsa nyama ya magazi mʼkamwa mwawo, chakudya choletsedwa mʼmano mwawo. Amene atsala adzakhala anthu a Mulungu wathu, adzasanduka atsogoleri mu Yuda, ndipo Ekroni adzakhala ngati Ayebusi.
Og jeg vil borttage hans Blod af hans Mund og hans Vederstyggeligheder fra hans Tænder, at ogsaa han skal blive tilbage for vor Gud; og han skal være som en Fyrste i Juda og Ekron som en Jebusiter.
8 Koma Ine ndidzalondera Nyumba yanga ndi kuyiteteza kwa ankhondo osakaza. Palibenso mdani amene adzagonjetse anthu anga, pakuti tsopano ndikuwayangʼanira.
Og jeg vil slaa Lejr for mit Hus imod Krigshær, at ingen drager derover frem eller tilbage, og at ingen, Undertrykker ydermere drager over dem; thi jeg har nu set til med mine Øjne.
9 Sangalala kwambiri, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni! Fuwula, mwana wamkazi wa Yerusalemu! Taona, mfumu yako ikubwera kwa iwe, yolungama ndi yogonjetsa adani, yodzichepetsa ndi yokwera pa bulu, pa mwana wamphongo wa bulu.
Fryd dig saare, Zions Datter! raab med Glæde, Jerusalems Datter! se, din Konge kommer til dig, han er retfærdig og frelst, fattig og ridende paa et Asen og paa et ungt Asen, Asenindens Føl
10 Ndidzachotsa magaleta ankhondo ku Efereimu ndi akavalo ankhondo ku Yerusalemu, ndipo uta wankhondo udzathyoka. Mfumuyo idzabweretsa mtendere pakati pa mitundu ya anthu. Ulamuliro wake udzayambira ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina, ndipo kuchokera ku Mtsinje (Yufurate) mpaka ku malekezero a dziko lapansi.
Og jeg vil udrydde Vogne af Efraim og Heste af Jerusalem, og Krigsbuen skal udryddes, og han skal tale til Hedningerne, saa der bliver Fred; og hans Herredømme skal være fra Hav til Hav og fra Floden indtil Jordens Ender.
11 Tsono kunena za iwe, chifukwa cha magazi a pangano lako ndi Ine, ndidzamasula amʼndende ako, ndidzawatulutsa mʼdzenje lopanda madzi.
Og du! for din Pagts Blods Skyld — dine bundne udlader jeg af en vandløs Hule.
12 Bwererani ku malo anu otetezedwa, inu amʼndende achiyembekezo; ngakhale tsopano ndikulengeza kuti ndidzakubwezerani zabwino mowirikiza.
Vender tilbage til Befæstningen, I bundne, som have Haab! endog i Dag forkynder jeg; Jeg vil gengælde dig dobbelt.
13 Ndidzakoka Yuda monga ndimakokera uta wanga, ndipo Efereimu ndiye muvi wake. Ndidzadzutsa ana ako iwe Ziyoni, kulimbana ndi ana ako iwe Grisi, ndipo ndidzakusandutsa iwe lupanga la munthu wankhondo.
Thi jeg spænder mig Juda, lægger Efraim paa Buen, og jeg vækker dine Sønner, Zion! imod dine Sønner, Grækenland! og jeg gør dig som, den vældiges Sværd.
14 Pamenepo Yehova adzaonekera kwa anthu ake; mivi yake idzangʼanima ngati chingʼaningʼani. Ambuye Yehova adzaliza lipenga; ndipo adzayenda mu mkuntho wochokera kummwera,
Og Herren vil lade sig se over dem, og hans Pil skal fare ud som Lynet; og den Herre, Herre skal støde i Basunen og gaa frem i Stormene af Syden.
15 ndipo Yehova Wamphamvuzonse adzawateteza. Iwo adzawononga ndipo adzagonjetsa ndi miyala ya legeni. Adzamwa magazi ndi kubangula ngati amwa vinyo; magazi adzayenderera ngati a mʼmbale yowazira magazi pa ngodya za guwa lansembe.
Den Herre Zebaoth skal beskærme dem, og de skulle æde, og de skulle nedtræde Slyngestene, og de skulle drikke, de skulle rase som af Vin, og de skulle fyldes som Offerskaalen som Alterets Hjørner.
16 Tsiku limenelo Yehova Mulungu wawo adzawapulumutsa pakuti anthu ake ali ngati nkhosa. Adzanyezimira mʼdziko lake ngati miyala yokongola pa chipewa chaufumu.
Og Herren deres Gud skal frelse dem paa den Dag som sit Folks Hjord; thi de ere Kronestene, der funkle over hans Land.
17 Taonani chikoka ndi kukongola kwawo! Tirigu adzasangalatsa anyamata, ndi vinyo watsopano anamwali.
Thi hvor stor skal dets Herlighed og hvor stor dets Skønhed være! Korn skal bringe unge Karle og Most unge Piger til at blomstre frem.