< Zekariya 9 >
1 Mawu a Yehova odzudzula dziko la Hadiraki ndi mzinda wa Damasiko pakuti maso a anthu ndiponso mafuko onse a Israeli ali pa Yehova—
Hadrak khohmuen neh a duemnah, Damasku ham BOEIPA kah olrhuh ol. Hlang neh Israel koca boeih kah a mik he, BOEIPA dongah ni a om.
2 ndiponso mzinda wa Hamati, umene ukuchita malire ndi dzikoli, komanso pa Turo ndi Sidoni, ngakhale kuti iwo ndi anzeru kwambiri.
A taengah rhi aka suem Khamath khaw, bahoeng aka cueih Tyre neh Sidon khaw om.
3 Ndipo Turo anadzimangira linga; wadziwunjikira siliva ngati fumbi, ndi golide ngati zinyalala za mʼmisewu.
Tyre loh amah hamla vongup a sak tih, cak te laipi bangla, sui khaw vongvoel kah tangnong bangla a hmoek.
4 Taonani Ambuye adzamulanda chuma chakecho ndi kuwononga mphamvu zake mʼnyanja, ndipo adzapserera ndi moto.
Ka Boeipa loh anih te a talh vetih, a caem khaw tuitunli la a ngawn pah ni he. Te phoeiah anih te, hmai loh a hlawp pawn ni.
5 Mzinda wa Asikeloni udzaona zimenezi, nʼkuchita mantha; Gaza adzanjenjemera ndi ululu, chimodzimodzinso Ekroni, chifukwa chiyembekezo chake chidzatheratu. Mfumu ya ku Gaza idzaphedwa ndipo Asikeloni adzakhala opanda anthu.
Ashkelon loh a hmuh vaengah a rhih vetih, Gaza khaw muep poi ni. Ekron khaw a uepnah ham yak ni. Gaza lamkah manghai milh vetih, Ashkelon khaw khosak tal ni.
6 Mu Asidodi mudzakhala mlendo, ndipo ndidzathetsa kunyada kwa Afilisti.
Ashdod ah halhca loh kho a sak vetih, Philisti kah hoemdamnah ka khoe ni.
7 Ndidzachotsa nyama ya magazi mʼkamwa mwawo, chakudya choletsedwa mʼmano mwawo. Amene atsala adzakhala anthu a Mulungu wathu, adzasanduka atsogoleri mu Yuda, ndipo Ekroni adzakhala ngati Ayebusi.
A ka lamkah a thii khaw, a no laklo lamkah a sarhingkoi khaw, ka khoe pah ni. Amah khaw mamih kah Pathen hamla sueng vetih, Judah ah khoboei la om ni. Te vaengah Ekron te Jebusi bangla om ni.
8 Koma Ine ndidzalondera Nyumba yanga ndi kuyiteteza kwa ankhondo osakaza. Palibenso mdani amene adzagonjetse anthu anga, pakuti tsopano ndikuwayangʼanira.
Ka im he, aka paan tih aka mael taeng lamloh, rhaltawt neh ka rhaeh thil ni. Ka mik neh ka hmuh coeng dongah, tueihno loh amih te paan voel mahpawh.
9 Sangalala kwambiri, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni! Fuwula, mwana wamkazi wa Yerusalemu! Taona, mfumu yako ikubwera kwa iwe, yolungama ndi yogonjetsa adani, yodzichepetsa ndi yokwera pa bulu, pa mwana wamphongo wa bulu.
Zion nu aw bahoeng omngaih laeh, Jerusalem nu aw yuhui laeh. Na manghai te na taengah a dueng la ha pai coeng ke. Amah loh mangdaeng te a khang. Te dongah laak so neh laaknu a ca laaktal dongah ngol.
10 Ndidzachotsa magaleta ankhondo ku Efereimu ndi akavalo ankhondo ku Yerusalemu, ndipo uta wankhondo udzathyoka. Mfumuyo idzabweretsa mtendere pakati pa mitundu ya anthu. Ulamuliro wake udzayambira ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina, ndipo kuchokera ku Mtsinje (Yufurate) mpaka ku malekezero a dziko lapansi.
Ephraim lamkah leng neh Jerusalem lamkah kah marhang khaw ka hnawt vetih, caemtloek lii khaw tlawt ni. Namtom taengah rhoepnah a thui vetih, a boeinah he tuitun lamloh tuitun duela, tuiva lamloh kho bawt duela a pha ni.
11 Tsono kunena za iwe, chifukwa cha magazi a pangano lako ndi Ine, ndidzamasula amʼndende ako, ndidzawatulutsa mʼdzenje lopanda madzi.
Nang khaw na paipi thii rhangneh na thongtla pataeng a khuiah tui aka om pawh tangrhom lamloh ka hlah ni.
12 Bwererani ku malo anu otetezedwa, inu amʼndende achiyembekezo; ngakhale tsopano ndikulengeza kuti ndidzakubwezerani zabwino mowirikiza.
Ngaiuepnah khuikah thongtla rhoek, lunghim taengla mael uh laeh, tahae khohnin ah pataeng a doek tih nang taengah rhaepnit la kan thuung ni.
13 Ndidzakoka Yuda monga ndimakokera uta wanga, ndipo Efereimu ndiye muvi wake. Ndidzadzutsa ana ako iwe Ziyoni, kulimbana ndi ana ako iwe Grisi, ndipo ndidzakusandutsa iwe lupanga la munthu wankhondo.
Judah te kamah hamla lii la ka phuk vetih, Ephraim khaw cung ni. Greek nang ca rhoek taengah Zion nang ca rhoek te kan haeng vetih, nang te hlangrhalh kah cunghang bangla kang khueh ni.
14 Pamenepo Yehova adzaonekera kwa anthu ake; mivi yake idzangʼanima ngati chingʼaningʼani. Ambuye Yehova adzaliza lipenga; ndipo adzayenda mu mkuntho wochokera kummwera,
BOEIPA he amih soah phoe vetih, a thaltang te rhaek bangla a khuen ni. Te vaengah ka Boeipa Yahovah loh tuki te a ueng vetih, tuithim hlipuei neh cet ni.
15 ndipo Yehova Wamphamvuzonse adzawateteza. Iwo adzawononga ndipo adzagonjetsa ndi miyala ya legeni. Adzamwa magazi ndi kubangula ngati amwa vinyo; magazi adzayenderera ngati a mʼmbale yowazira magazi pa ngodya za guwa lansembe.
Caempuei BOEIPA loh amih te a tungaep ni. Te vaengah a caak uh vetih, payai lung te a khoem uh ni. Misurtui vaengkah bangla, a ok vetih umya uh ni. Te phoeiah tah baelcak bangla, hmueihtuk rhungsut bangla hah uh ni.
16 Tsiku limenelo Yehova Mulungu wawo adzawapulumutsa pakuti anthu ake ali ngati nkhosa. Adzanyezimira mʼdziko lake ngati miyala yokongola pa chipewa chaufumu.
Te khohnin ah tah, amih te a Pathen BOEIPA loh, a pilnam tuping la, a khohmuen ah aka vang rhuisam lung la a khang ni.
17 Taonani chikoka ndi kukongola kwawo! Tirigu adzasangalatsa anyamata, ndi vinyo watsopano anamwali.
A kawnthen khaw bahoeng then, a sakthen khaw bahoeng then. Tongpang te cangpai neh, oila khaw misur thai neh thaihsu ni.