< Zekariya 8 >

1 Awa ndi mawu amene Yehova Wamphamvuzonse ananena.
Potem doszło [do mnie] słowo PANA zastępów mówiące:
2 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndikuchitira nsanje yayikulu Ziyoni. Mtima wanga ukupweteka chifukwa cha nsanje pa iyeyo.”
Tak mówi PAN zastępów: Byłem zazdrosny o Syjon w wielkiej gorliwości, byłem zazdrosny w wielkim gniewie.
3 Yehova akuti, “Ndidzabwerera ku Ziyoni ndi kukakhala ku Yerusalemu. Pamenepo Yerusalemu adzatchedwa Mzinda wa Choonadi ndipo phiri la Yehova Wamphamvuzonse lidzatchedwa Phiri Lopatulika.”
Tak mówi PAN: Wróciłem na Syjon i zamieszkam w Jerozolimie; a Jerozolima będzie nazwana Miastem Wiernym, a góra PANA zastępów – Górą Świętą.
4 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Abambo ndi amayi okalamba adzakhalanso mʼmisewu ya mu Yerusalemu, aliyense ali ndi ndodo mʼmanja mwake chifukwa cha kuchuluka kwa masiku ake.
Tak mówi PAN zastępów: Jeszcze siadać będą starcy i staruszki na ulicach Jerozolimy, każdy z nich z laską w ręku z powodu podeszłego wieku.
5 Ndipo misewu ya mu mzindamo idzadzaza ndi anyamata ndi atsikana akusewera.”
I ulice miasta będą pełne bawiących się na nich chłopców i dziewcząt.
6 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ngati zikuoneka kuti nʼzosatheka kwa anthu otsala pa nthawi ino, kodi zidzakhala zosathekanso kwa Ine?” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Tak mówi PAN zastępów: Jeśli w tych dniach wyda się to niemożliwe w oczach resztki tego ludu, czy będzie to też niemożliwe w moich oczach? – mówi PAN zastępów.
7 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani ndidzapulumutsa anthu anga kuchokera ku mayiko a kummawa ndi kumadzulo.
Tak mówi PAN zastępów: Oto wybawię swój lud z ziemi wschodniej i z ziemi zachodniej.
8 Ndidzawabweretsa kuti adzakhale mu Yerusalemu; adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo, wokhulupirika ndi wolungama pakati pawo.”
Sprowadzę go i zamieszka w Jerozolimie, i będzie moim ludem, a ja będę jego Bogiem, w prawdzie i sprawiedliwości.
9 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Inu amene tsopano mukumva mawu awa amene akuyankhula aneneri amene analipo pamene ankayika maziko a nyumba ya Yehova Wamphamvuzonse, ‘limbani mtima kuti mumange Nyumba ya Yehova.’
Tak mówi PAN zastępów: Niech się umocnią wasze ręce, wy, którzy słuchaliście w tych dniach słów z ust proroków, którzy byli w dniu, [kiedy] założono fundament domu PANA zastępów, aby świątynia została odbudowana.
10 Mpaka nthawi imeneyi panalibe munthu wolandira malipiro pa ntchito kapena ndalama zolipirira nyama zogwira ntchito. Panalibe munthu amene ankadzigwirira ntchito mwamtendere chifukwa choopa adani ake, pakuti Ine ndinkawayambanitsa.
Przed tymi dniami bowiem nie była wynagrodzona praca ludzka i praca bydląt. Dla wychodzących i wchodzących nie było pokoju z powodu wroga, bo ja podburzyłem wszystkich ludzi, jednych przeciwko drugim.
11 Koma tsopano sindidzachitira otsala mwa anthu awa zomwe ndinachita kale,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Lecz teraz nie uczynię z resztką tego ludu tak jak za dawnych dni, mówi PAN zastępów.
12 “Pakuti mbewu zidzamera bwino, mpesa udzabala zipatso zake, nthaka idzatulutsa zomera zake, ndi thambo lidzagwetsa mame. Ndidzapereka zonse kukhala cholowa cha otsala mwa anthu awa.
Ale siewy będą [rosły] w pokoju, winorośl wyda swój owoc, ziemia wyda swoje plony i niebiosa także spuszczą swoją rosę, a to wszystko dam resztce tego ludu w posiadanie.
13 Monga mwakhala muli chinthu chotembereredwa pakati pa mitundu ina ya anthu, inu Yuda ndi Israeli, choncho ndidzakupulumutsani, ndipo mudzakhala dalitso. Musachite mantha, koma limbani mtima.”
I stanie się, że jak byliście przekleństwem wśród pogan, domu Judy i domu Izraela, tak was wybawię i będziecie błogosławieństwem. Nie bójcie się i niech się umocnią wasze ręce.
14 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Monga ndinatsimikiza mtima kubweretsa choyipa pa inu, komanso osakuchitirani chisoni pamene makolo anu anandikwiyitsa,” akutero Yehova,
Tak bowiem mówi PAN zastępów: Jak postanowiłem ukarać was, gdy wasi ojcowie pobudzali mnie do gniewu, mówi PAN zastępów – i nie żałowałem tego;
15 “Choncho tsopano ndatsimikiza mtima kuchitiranso zabwino Yerusalemu ndi Yuda. Musachite mantha.
Tak znowu postanowiłem w tych dniach uczynić dobrze Jerozolimie i domowi Judy. Nie bójcie się.
16 Zinthu zoti muchite ndi izi: Muziwuzana zoona zokhazokha, muziweruza moona ndi mwachilungamo mʼmabwalo anu;
To [są] rzeczy, które będziecie czynić: Mówcie prawdę, każdy ze swoim bliźnim, wykonujcie sprawiedliwy i spokojny sąd w waszych bramach;
17 musamachitire mnzanu chiwembu, musamakonde kulumbira zonama. Zonsezi Ine ndimadana nazo,” akutero Yehova.
Nie obmyślajcie zła w sercach waszych, jeden przeciwko drugiemu, i nie lubujcie się w krzywoprzysięstwie, gdyż tego wszystkiego nienawidzę, mówi PAN.
18 Yehova Wamphamvuzonse anayankhulanso nane.
I doszło do mnie słowo PANA zastępów mówiące:
19 Ndipo ananena kuti, “Kusala zakudya kwa pa mwezi wachinayi, chisanu, chisanu ndi chiwiri ndi wakhumi, kudzakhala nthawi yachimwemwe, ya chisangalalo ndi nthawi ya madyerero chikondwerero kwa Yuda. Nʼchifukwa chake muzikonda choonadi ndi mtendere.”
Tak mówi PAN zastępów: Post w czwartym, piątym, siódmym i dziesiątym [miesiącu] zamienią się dla domu Judy w radość i wesele, i w rozkoszne święta. Miłujcie więc prawdę i pokój.
20 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu a mitundu yambiri ndi anthu okhala mʼmizinda yambiri adzabwerabe,
Tak mówi PAN zastępów: Jeszcze będą przychodzić narody i mieszkańcy wielu miast.
21 ndipo nzika za mzinda wina zidzapita ku mzinda wina, kukanena kuti, ‘Tiyeni mwamsanga tikapemphe madalitso kwa Yehova ndi kukapembedza Yehova Wamphamvuzonse. Inenso ndikupita kumeneko.’
Mieszkańcy jednego [miasta] pójdą do drugiego, mówiąc: Pójdźmy ochoczo przebłagać oblicze PANA i szukać PANA zastępów. Ja także pójdę.
22 Anthu ambiri ndiponso a ku mayiko amphamvu adzabwera ku Yerusalemu kudzapembedza Yehova Wamphamvuzonse ndi kudzapempha madalitso.”
A tak liczne ludy i potężne narody przybędą szukać PANA zastępów w Jerozolimie i przebłagać oblicze PANA.
23 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Masiku amenewo anthu khumi ochokera ku mitundu ya anthu a ziyankhulo zosiyana adzagwira mkanjo wa Myuda ndi kunena kuti, ‘Tipite nawo, chifukwa tamva kuti Mulungu ali nanu.’”
Tak mówi PAN zastępów: W tych dniach dziesięciu ludzi ze wszystkich języków narodów uchwyci się poły jednego Żyda, mówiąc: Pójdziemy z wami, bo usłyszeliśmy, [że] Bóg [jest] z wami.

< Zekariya 8 >