< Zekariya 8 >

1 Awa ndi mawu amene Yehova Wamphamvuzonse ananena.
Laselifika ilizwi leNkosi yamabandla lisithi:
2 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndikuchitira nsanje yayikulu Ziyoni. Mtima wanga ukupweteka chifukwa cha nsanje pa iyeyo.”
Itsho njalo iNkosi yamabandla: Ngilobukhwele ngeZiyoni ngobukhwele obukhulu, yebo, ngilobukhwele ngayo ngokuvutha okukhulu.
3 Yehova akuti, “Ndidzabwerera ku Ziyoni ndi kukakhala ku Yerusalemu. Pamenepo Yerusalemu adzatchedwa Mzinda wa Choonadi ndipo phiri la Yehova Wamphamvuzonse lidzatchedwa Phiri Lopatulika.”
Itsho njalo iNkosi: Ngibuyele eZiyoni, njalo ngizahlala phakathi kweJerusalema; njalo iJerusalema izakuthiwa ngumuzi weqiniso, lentaba yeNkosi yamabandla, intaba engcwele.
4 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Abambo ndi amayi okalamba adzakhalanso mʼmisewu ya mu Yerusalemu, aliyense ali ndi ndodo mʼmanja mwake chifukwa cha kuchuluka kwa masiku ake.
Itsho njalo iNkosi yamabandla: Kusezakuhlala amaxhegu lezalukazi ezitaladeni zeJerusalema, ngulowo lalowo elodondolo esandleni sakhe ngenxa yobunengi bezinsuku.
5 Ndipo misewu ya mu mzindamo idzadzaza ndi anyamata ndi atsikana akusewera.”
Lezitalada zomuzi zizagcwala abafana lamankazana bedlala ezitaladeni zawo.
6 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ngati zikuoneka kuti nʼzosatheka kwa anthu otsala pa nthawi ino, kodi zidzakhala zosathekanso kwa Ine?” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Itsho njalo iNkosi yamabandla: Uba kumangalisa emehlweni ensali yalababantu ngalezozinsuku, kungamangalisa lemehlweni ami yini? itsho iNkosi yamabandla.
7 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani ndidzapulumutsa anthu anga kuchokera ku mayiko a kummawa ndi kumadzulo.
Itsho njalo iNkosi yamabandla: Khangela, ngizasindisa abantu bami elizweni lempumalanga, lelizweni lokutshona kwelanga;
8 Ndidzawabweretsa kuti adzakhale mu Yerusalemu; adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo, wokhulupirika ndi wolungama pakati pawo.”
ngibalethe, bahlale phakathi kweJerusalema; njalo bazakuba ngabantu bami, lami ngibe nguNkulunkulu wabo, ngeqiniso langokulunga.
9 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Inu amene tsopano mukumva mawu awa amene akuyankhula aneneri amene analipo pamene ankayika maziko a nyumba ya Yehova Wamphamvuzonse, ‘limbani mtima kuti mumange Nyumba ya Yehova.’
Itsho njalo iNkosi yamabandla: Izandla zenu kaziqine, lina elizwayo ngalezinsuku amazwi la ngomlomo wabaprofethi, ababekhona mhla isisekelo sendlu yeNkosi yamabandla sibekwa, ukuze ithempeli lakhiwe.
10 Mpaka nthawi imeneyi panalibe munthu wolandira malipiro pa ntchito kapena ndalama zolipirira nyama zogwira ntchito. Panalibe munthu amene ankadzigwirira ntchito mwamtendere chifukwa choopa adani ake, pakuti Ine ndinkawayambanitsa.
Ngoba ngaphambi kwalezonsuku kwakungelaholo lomuntu, kwakungekho iholo lenyamazana; futhi kungekho ukuthula kulowo owayephuma kumbe owayengena ngenxa yenhlupheko; ngoba ngathuma wonke umuntu ngulowo emelene lomakhelwane wakhe.
11 Koma tsopano sindidzachitira otsala mwa anthu awa zomwe ndinachita kale,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Kodwa khathesi kangiyikuba kunsali yalababantu njengensukwini zakuqala, itsho iNkosi yamabandla.
12 “Pakuti mbewu zidzamera bwino, mpesa udzabala zipatso zake, nthaka idzatulutsa zomera zake, ndi thambo lidzagwetsa mame. Ndidzapereka zonse kukhala cholowa cha otsala mwa anthu awa.
Ngoba inhlanyelo izaphumelela, ivini lithele izithelo zalo, lomhlabathi uphe isivuno sawo, lamazulu aphe amazolo awo; njalo ngizakwenza insali yalababantu ukuthi idle ilifa lazo zonke lezizinto.
13 Monga mwakhala muli chinthu chotembereredwa pakati pa mitundu ina ya anthu, inu Yuda ndi Israeli, choncho ndidzakupulumutsani, ndipo mudzakhala dalitso. Musachite mantha, koma limbani mtima.”
Kuzakuthi-ke njengoba laliyisiqalekiso phakathi kwabezizwe, wena ndlu kaJuda, lawe ndlu kaIsrayeli, ngokunjalo ngizalisindisa, libe yisibusiso. Lingesabi, izandla zenu kaziqine.
14 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Monga ndinatsimikiza mtima kubweretsa choyipa pa inu, komanso osakuchitirani chisoni pamene makolo anu anandikwiyitsa,” akutero Yehova,
Ngoba itsho njalo iNkosi yamabandla: Njengoba nganginakane ukwenza okubi kini, lapho oyihlo bengithukuthelisa, itsho iNkosi yamabandla, njalo kangizisolanga;
15 “Choncho tsopano ndatsimikiza mtima kuchitiranso zabwino Yerusalemu ndi Yuda. Musachite mantha.
ngokunjalo ngibuye ngacabanga kulezinsuku ukwenza okuhle kuyo iJerusalema lakuyo indlu kaJuda; lingesabi.
16 Zinthu zoti muchite ndi izi: Muziwuzana zoona zokhazokha, muziweruza moona ndi mwachilungamo mʼmabwalo anu;
Lezi yizinto elizazenza: Khulumani iqiniso, ngulowo lalowo kumakhelwane wakhe; yehlulelani iqiniso lesahlulelo sokuthula emasangweni enu.
17 musamachitire mnzanu chiwembu, musamakonde kulumbira zonama. Zonsezi Ine ndimadana nazo,” akutero Yehova.
Lingacabangi ububi enhliziyweni yenu ngulowo lalowo emelene lomakhelwane; lingathandi isifungo samanga; ngoba zonke lezizinto yilezo engizizondayo, itsho iNkosi.
18 Yehova Wamphamvuzonse anayankhulanso nane.
Ilizwi leNkosi yamabandla laselifika kimi, lisithi:
19 Ndipo ananena kuti, “Kusala zakudya kwa pa mwezi wachinayi, chisanu, chisanu ndi chiwiri ndi wakhumi, kudzakhala nthawi yachimwemwe, ya chisangalalo ndi nthawi ya madyerero chikondwerero kwa Yuda. Nʼchifukwa chake muzikonda choonadi ndi mtendere.”
Itsho njalo iNkosi yamabandla: Ukuzila ukudla kwenyanga yesine, lokuzila ukudla kweyesihlanu, lokuzila ukudla kweyesikhombisa, lokuzila ukudla kweyetshumi, kuzakuba yintokozo, lokuthaba, lezikhathi ezimisiweyo zezinjabulo kuyo indlu yakoJuda. Ngakho thandani iqiniso lokuthula.
20 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu a mitundu yambiri ndi anthu okhala mʼmizinda yambiri adzabwerabe,
Itsho njalo iNkosi yamabandla: Kusezakwenzeka ukuthi kufike abantu labahlali bemizi eminengi.
21 ndipo nzika za mzinda wina zidzapita ku mzinda wina, kukanena kuti, ‘Tiyeni mwamsanga tikapemphe madalitso kwa Yehova ndi kukapembedza Yehova Wamphamvuzonse. Inenso ndikupita kumeneko.’
Labahlali bomunye umuzi bazakuya komunye, besithi: Kasihambeni ngokuphangisa ukuyancenga phambi kweNkosi, lokudinga iNkosi yamabandla; lami ngizahamba.
22 Anthu ambiri ndiponso a ku mayiko amphamvu adzabwera ku Yerusalemu kudzapembedza Yehova Wamphamvuzonse ndi kudzapempha madalitso.”
Yebo, kuzakuza abantu abanengi lezizwe ezilamandla ukuzadinga iNkosi yamabandla eJerusalema, lokuncenga phambi kweNkosi.
23 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Masiku amenewo anthu khumi ochokera ku mitundu ya anthu a ziyankhulo zosiyana adzagwira mkanjo wa Myuda ndi kunena kuti, ‘Tipite nawo, chifukwa tamva kuti Mulungu ali nanu.’”
Itsho njalo iNkosi yamabandla: Ngalezonsuku kuzakuthi abambe amadoda alitshumi ezindimini zonke zezizwe, yebo abambe umphetho wesembatho somuntu ongumJuda, athi: Sizahamba lani; ngoba sizwile ukuthi uNkulunkulu ulani.

< Zekariya 8 >