< Zekariya 8 >

1 Awa ndi mawu amene Yehova Wamphamvuzonse ananena.
Lafika njalo kimi ilizwi likaThixo uSomandla.
2 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndikuchitira nsanje yayikulu Ziyoni. Mtima wanga ukupweteka chifukwa cha nsanje pa iyeyo.”
Nanku okutshiwo nguThixo uSomandla: “Ngilobukhwele kabi ngeZiyoni; ngiyatsha ngobukhwele ngayo.”
3 Yehova akuti, “Ndidzabwerera ku Ziyoni ndi kukakhala ku Yerusalemu. Pamenepo Yerusalemu adzatchedwa Mzinda wa Choonadi ndipo phiri la Yehova Wamphamvuzonse lidzatchedwa Phiri Lopatulika.”
Nanku okutshiwo nguThixo: “Ngizabuyela eZiyoni ngihlale eJerusalema. Lapho-ke iJerusalema izathiwa nguMuzi weQiniso, lentaba kaThixo uSomandla izabizwa ngokuthi yiNtaba eNgcwele.”
4 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Abambo ndi amayi okalamba adzakhalanso mʼmisewu ya mu Yerusalemu, aliyense ali ndi ndodo mʼmanja mwake chifukwa cha kuchuluka kwa masiku ake.
Nanku okutshiwo nguThixo uSomandla, uthi: “Kuzakwenzakala njalo ukuthi amaxhegu lezalukazi bahlale nje ezitaladini zeJerusalema, ngulowo lodondolo lwakhe esandleni ngenxa yokuluphala.
5 Ndipo misewu ya mu mzindamo idzadzaza ndi anyamata ndi atsikana akusewera.”
Izitalada zedolobho zizaphithizela abafana lamantombazana bezidlalela khona.”
6 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ngati zikuoneka kuti nʼzosatheka kwa anthu otsala pa nthawi ino, kodi zidzakhala zosathekanso kwa Ine?” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Nanku okutshiwo nguThixo uSomandla, uthi: “Kungabonakala njengesimanga kwabayinsalela yalababantu ngalesosikhathi, kodwa kambe kungabonakala njengesimanga kimi na?” kutsho uThixo uSomandla.
7 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani ndidzapulumutsa anthu anga kuchokera ku mayiko a kummawa ndi kumadzulo.
Nanku okutshiwo nguThixo uSomandla, uthi: “Ngizabasindisa abantu bami emazweni asempumalanga lasemazweni asentshonalanga.
8 Ndidzawabweretsa kuti adzakhale mu Yerusalemu; adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo, wokhulupirika ndi wolungama pakati pawo.”
Ngizababuyisela bayehlala eJerusalema; bazakuba ngabantu bami, lami ngizathembeka njalo ngibe lokulunga kubo njengoNkulunkulu wabo.”
9 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Inu amene tsopano mukumva mawu awa amene akuyankhula aneneri amene analipo pamene ankayika maziko a nyumba ya Yehova Wamphamvuzonse, ‘limbani mtima kuti mumange Nyumba ya Yehova.’
Nanku okutshiwo nguThixo uSomandla, uthi: “Lina okwamanje eliwezwayo amazwi la akhulunywa ngabaphrofethi ababekhona kubekwa isisekelo sendlu kaThixo uSomandla, qinisani izandla zenu ukuze ithempeli lakhiwe.
10 Mpaka nthawi imeneyi panalibe munthu wolandira malipiro pa ntchito kapena ndalama zolipirira nyama zogwira ntchito. Panalibe munthu amene ankadzigwirira ntchito mwamtendere chifukwa choopa adani ake, pakuti Ine ndinkawayambanitsa.
Mandulo kwesikhathi leso kwakungekho imbadalo ngomsebenzi womuntu loba owenyamazana. Umuntu loba engubani wayengazihambeli loba azenzele okwakhe ekhululekile ngenxa yezitha, ngoba abantu ngasengibaxabanise labomakhelwane babo.
11 Koma tsopano sindidzachitira otsala mwa anthu awa zomwe ndinachita kale,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Kodwa khathesi kangisayikwenza kulaba abayinsalela njengalokho engakwenzayo endulo,” kutsho uThixo uSomandla.
12 “Pakuti mbewu zidzamera bwino, mpesa udzabala zipatso zake, nthaka idzatulutsa zomera zake, ndi thambo lidzagwetsa mame. Ndidzapereka zonse kukhala cholowa cha otsala mwa anthu awa.
“Inhlanyelo izakhula kuhle, ivini lizakhupha izithelo zalo, umhlabathi uzakhulisa amabele, lamazulu azakwehlisa amazolo awo. Zonke lezizinto ngizazinika njengelifa kwabayinsalela yalababantu.
13 Monga mwakhala muli chinthu chotembereredwa pakati pa mitundu ina ya anthu, inu Yuda ndi Israeli, choncho ndidzakupulumutsani, ndipo mudzakhala dalitso. Musachite mantha, koma limbani mtima.”
Njengoba beliyinto eqalekisiweyo phakathi kwezizwe, wena Juda lo-Israyeli, ngakho ngizalisindisa libe yisibusiso. Lingesabi, kodwa qinisani izandla zenu.”
14 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Monga ndinatsimikiza mtima kubweretsa choyipa pa inu, komanso osakuchitirani chisoni pamene makolo anu anandikwiyitsa,” akutero Yehova,
Nanku akutshoyo uThixo uSomandla, uthi: “Kanjengalokhu ngasengimisile ukwehlisela umonakalo phezu kwenu angaze ngatshengisa uzwelo lapho okhokho benu bangizondisa,” kutsho uThixo uSomandla,
15 “Choncho tsopano ndatsimikiza mtima kuchitiranso zabwino Yerusalemu ndi Yuda. Musachite mantha.
“yikho manje sengimisile ukwenza ubuhle njalo eJerusalema lakoJuda. Lingesabi.
16 Zinthu zoti muchite ndi izi: Muziwuzana zoona zokhazokha, muziweruza moona ndi mwachilungamo mʼmabwalo anu;
Nanzi izinto okumele lizenze: Khulumani iqiniso omunye komunye, njalo lehlulelane ngeqiniso langokuqonda emithethwandaba yenu;
17 musamachitire mnzanu chiwembu, musamakonde kulumbira zonama. Zonsezi Ine ndimadana nazo,” akutero Yehova.
lingakheli umakhelwane wenu amacebo amabi, njalo lingaze lathanda ukufunga ngokungamanga. Konke lokhu ngiyakuzonda,” kutsho uThixo.
18 Yehova Wamphamvuzonse anayankhulanso nane.
Ilizwi likaThixo uSomandla laphinda labuya kimi.
19 Ndipo ananena kuti, “Kusala zakudya kwa pa mwezi wachinayi, chisanu, chisanu ndi chiwiri ndi wakhumi, kudzakhala nthawi yachimwemwe, ya chisangalalo ndi nthawi ya madyerero chikondwerero kwa Yuda. Nʼchifukwa chake muzikonda choonadi ndi mtendere.”
Nanku akutshoyo uThixo uSomandla, uthi, “Amazilo awenyanga yesine, leyesihlanu, leyesikhombisa kanye leyetshumi azakuba yizikhathi zokuthokoza lokujabula, abe yimikhosi yokuthaba koJuda. Ngakho-ke thandani iqiniso lokuthula.”
20 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu a mitundu yambiri ndi anthu okhala mʼmizinda yambiri adzabwerabe,
Nanku akutshoyo uThixo uSomandla: “Abantu abanengi lezakhamizi zamadolobho amanengi basezakuza,
21 ndipo nzika za mzinda wina zidzapita ku mzinda wina, kukanena kuti, ‘Tiyeni mwamsanga tikapemphe madalitso kwa Yehova ndi kukapembedza Yehova Wamphamvuzonse. Inenso ndikupita kumeneko.’
njalo izakhamizi zedolobho leli zizakuya kwezakuleliyana zifike zithi, ‘Kasihambe khathesi lokhu siyoncenga uThixo, simfune uThixo uSomandla. Mina sengihamba.’
22 Anthu ambiri ndiponso a ku mayiko amphamvu adzabwera ku Yerusalemu kudzapembedza Yehova Wamphamvuzonse ndi kudzapempha madalitso.”
Kuzakuthi abantu abanengi lezizwe ezilamandla zizakuza eJerusalema ukuzafuna uThixo uSomandla bezocela kuye.”
23 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Masiku amenewo anthu khumi ochokera ku mitundu ya anthu a ziyankhulo zosiyana adzagwira mkanjo wa Myuda ndi kunena kuti, ‘Tipite nawo, chifukwa tamva kuti Mulungu ali nanu.’”
Nanku akutshoyo uThixo uSomandla, uthi: “Ngalezonsuku amadoda alitshumi aphuma kuzozonke izindimi lezizwe azagagadlela umphetho wengubo yomJuda oyedwa athi, ‘Wothi sihambe lawe ngoba sesizwile ukuthi uNkulunkulu ulani.’”

< Zekariya 8 >