< Zekariya 8 >

1 Awa ndi mawu amene Yehova Wamphamvuzonse ananena.
La parole de l'Éternel des armées me fut encore adressée en ces mots:
2 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndikuchitira nsanje yayikulu Ziyoni. Mtima wanga ukupweteka chifukwa cha nsanje pa iyeyo.”
Ainsi a dit l'Éternel des armées: Je suis jaloux pour Sion d'une grande jalousie; je suis jaloux pour elle avec une grande indignation.
3 Yehova akuti, “Ndidzabwerera ku Ziyoni ndi kukakhala ku Yerusalemu. Pamenepo Yerusalemu adzatchedwa Mzinda wa Choonadi ndipo phiri la Yehova Wamphamvuzonse lidzatchedwa Phiri Lopatulika.”
Ainsi a dit l'Éternel: Je reviens vers Sion; j'habiterai au milieu de Jérusalem; et Jérusalem sera appelée la ville fidèle, et la montagne de l'Éternel des armées, la montagne sainte.
4 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Abambo ndi amayi okalamba adzakhalanso mʼmisewu ya mu Yerusalemu, aliyense ali ndi ndodo mʼmanja mwake chifukwa cha kuchuluka kwa masiku ake.
Ainsi a dit l'Éternel des armées: Il y aura encore des vieillards et des femmes âgées, assis dans les places de Jérusalem, ayant chacun son bâton à la main, à cause du grand nombre de leurs jours.
5 Ndipo misewu ya mu mzindamo idzadzaza ndi anyamata ndi atsikana akusewera.”
Et les places de la ville seront remplies de jeunes garçons et de jeunes filles, qui se joueront dans ses places.
6 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ngati zikuoneka kuti nʼzosatheka kwa anthu otsala pa nthawi ino, kodi zidzakhala zosathekanso kwa Ine?” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Ainsi a dit l'Éternel des armées: Si cela semble difficile aux yeux du reste de ce peuple en ces jours-là, sera-ce pourtant difficile à mes yeux? dit l'Éternel des armées.
7 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani ndidzapulumutsa anthu anga kuchokera ku mayiko a kummawa ndi kumadzulo.
Ainsi a dit l'Éternel des armées: Voici, je vais sauver mon peuple du pays du Levant, et du pays du Couchant.
8 Ndidzawabweretsa kuti adzakhale mu Yerusalemu; adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo, wokhulupirika ndi wolungama pakati pawo.”
Je les ferai venir, et ils habiteront au milieu de Jérusalem; et ils seront mon peuple, et je serai leur Dieu, dans la vérité et dans la justice.
9 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Inu amene tsopano mukumva mawu awa amene akuyankhula aneneri amene analipo pamene ankayika maziko a nyumba ya Yehova Wamphamvuzonse, ‘limbani mtima kuti mumange Nyumba ya Yehova.’
Ainsi a dit l'Éternel des armées: Que vos mains se fortifient, ô vous qui entendez aujourd'hui ces paroles de la bouche des prophètes, au temps où la maison de l'Éternel des armées a été fondée et son temple rebâti.
10 Mpaka nthawi imeneyi panalibe munthu wolandira malipiro pa ntchito kapena ndalama zolipirira nyama zogwira ntchito. Panalibe munthu amene ankadzigwirira ntchito mwamtendere chifukwa choopa adani ake, pakuti Ine ndinkawayambanitsa.
Car, avant ce temps, il n'y avait point de salaire pour le travail de l'homme, ni de salaire pour le travail des bêtes; et pour ceux qui allaient et qui venaient, il n'y avait aucune paix à cause de l'ennemi, et je lançais tous les hommes les uns contre les autres.
11 Koma tsopano sindidzachitira otsala mwa anthu awa zomwe ndinachita kale,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Mais maintenant je ne serai pas pour le reste de ce peuple comme aux premiers jours, dit l'Éternel des armées.
12 “Pakuti mbewu zidzamera bwino, mpesa udzabala zipatso zake, nthaka idzatulutsa zomera zake, ndi thambo lidzagwetsa mame. Ndidzapereka zonse kukhala cholowa cha otsala mwa anthu awa.
Car la semence prospérera, la vigne rendra son fruit; la terre donnera son produit; les cieux donneront leur rosée, et je mettrai les restes de ce peuple en possession de toutes ces choses-là.
13 Monga mwakhala muli chinthu chotembereredwa pakati pa mitundu ina ya anthu, inu Yuda ndi Israeli, choncho ndidzakupulumutsani, ndipo mudzakhala dalitso. Musachite mantha, koma limbani mtima.”
Et comme vous avez été en malédiction parmi les nations, ô maison de Juda et maison d'Israël, ainsi je vous délivrerai, et vous serez en bénédiction. Ne craignez point, et que vos mains se fortifient!
14 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Monga ndinatsimikiza mtima kubweretsa choyipa pa inu, komanso osakuchitirani chisoni pamene makolo anu anandikwiyitsa,” akutero Yehova,
Car ainsi a dit l'Éternel des armées: Comme j'ai résolu de vous faire du mal, quand vos pères ont provoqué mon indignation, dit l'Éternel des armées, et que je ne m'en suis point repenti,
15 “Choncho tsopano ndatsimikiza mtima kuchitiranso zabwino Yerusalemu ndi Yuda. Musachite mantha.
Ainsi j'ai résolu au contraire, en ces jours-ci, de faire du bien à Jérusalem et à la maison de Juda. Ne craignez point!
16 Zinthu zoti muchite ndi izi: Muziwuzana zoona zokhazokha, muziweruza moona ndi mwachilungamo mʼmabwalo anu;
Voici les choses que vous devez faire: Dites la vérité, chacun à son prochain; rendez la justice dans vos portes, selon la vérité et pour la paix.
17 musamachitire mnzanu chiwembu, musamakonde kulumbira zonama. Zonsezi Ine ndimadana nazo,” akutero Yehova.
Et ne méditez point dans vos cœurs le mal l'un contre l'autre, et n'aimez point les faux serments, toutes ces choses que je hais, dit l'Éternel.
18 Yehova Wamphamvuzonse anayankhulanso nane.
La parole de l'Éternel des armées me fut adressée, en ces mots:
19 Ndipo ananena kuti, “Kusala zakudya kwa pa mwezi wachinayi, chisanu, chisanu ndi chiwiri ndi wakhumi, kudzakhala nthawi yachimwemwe, ya chisangalalo ndi nthawi ya madyerero chikondwerero kwa Yuda. Nʼchifukwa chake muzikonda choonadi ndi mtendere.”
Ainsi a dit l'Éternel des armées: Le jeûne du quatrième mois, le jeûne du cinquième, le jeûne du septième, et le jeûne du dixième mois deviendront pour la maison de Juda des jours de joie et d'allégresse, et des solennités heureuses. Mais aimez la vérité et la paix.
20 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu a mitundu yambiri ndi anthu okhala mʼmizinda yambiri adzabwerabe,
Ainsi a dit l'Éternel des armées: Il viendra encore des peuples et des habitants de plusieurs villes;
21 ndipo nzika za mzinda wina zidzapita ku mzinda wina, kukanena kuti, ‘Tiyeni mwamsanga tikapemphe madalitso kwa Yehova ndi kukapembedza Yehova Wamphamvuzonse. Inenso ndikupita kumeneko.’
Et les habitants de l'une iront à l'autre, et diront: Allons, allons supplier l'Éternel, et rechercher l'Éternel des armées! Je veux y aller, moi aussi!
22 Anthu ambiri ndiponso a ku mayiko amphamvu adzabwera ku Yerusalemu kudzapembedza Yehova Wamphamvuzonse ndi kudzapempha madalitso.”
Et plusieurs peuples et de puissantes nations viendront chercher l'Éternel des armées à Jérusalem, et y supplier l'Éternel.
23 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Masiku amenewo anthu khumi ochokera ku mitundu ya anthu a ziyankhulo zosiyana adzagwira mkanjo wa Myuda ndi kunena kuti, ‘Tipite nawo, chifukwa tamva kuti Mulungu ali nanu.’”
Ainsi a dit l'Éternel des armées: En ces jours-là, dix hommes de toutes les langues des nations saisiront le pan de la robe d'un Juif, et diront: Nous irons avec vous, car nous avons appris que Dieu est avec vous.

< Zekariya 8 >