< Zekariya 8 >
1 Awa ndi mawu amene Yehova Wamphamvuzonse ananena.
Et la parole du Seigneur, maître de toutes choses, me vint, disant:
2 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndikuchitira nsanje yayikulu Ziyoni. Mtima wanga ukupweteka chifukwa cha nsanje pa iyeyo.”
Voici ce que dit le Seigneur, maître de toutes choses: Je suis pris d'un grand zèle pour Jérusalem et pour Sion, et Je suis pris en même temps d'une grande colère.
3 Yehova akuti, “Ndidzabwerera ku Ziyoni ndi kukakhala ku Yerusalemu. Pamenepo Yerusalemu adzatchedwa Mzinda wa Choonadi ndipo phiri la Yehova Wamphamvuzonse lidzatchedwa Phiri Lopatulika.”
Voici ce que dit le Seigneur: Je reviendrai à Sion; Je résiderai au milieu de Jérusalem, et Jérusalem sera appelée la ville de vérité, et la montagne du Seigneur sera la montagne sainte.
4 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Abambo ndi amayi okalamba adzakhalanso mʼmisewu ya mu Yerusalemu, aliyense ali ndi ndodo mʼmanja mwake chifukwa cha kuchuluka kwa masiku ake.
Voici ce que dit le Seigneur tout-puissant: Des anciens et des anciennes s'assoiront encore dans les rues de Jérusalem, ayant chacun à la main un bâton de vieillesse, à cause de la plénitude de leurs jours.
5 Ndipo misewu ya mu mzindamo idzadzaza ndi anyamata ndi atsikana akusewera.”
Et les places de la ville seront remplies de jeunes garçons et de jeunes filles qui joueront dans ses rues.
6 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ngati zikuoneka kuti nʼzosatheka kwa anthu otsala pa nthawi ino, kodi zidzakhala zosathekanso kwa Ine?” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Voici ce que dit le Seigneur tout-puissant: Si en ces jours cela est impossible aux yeux de ceux qui sont restés de ce peuple, est-ce que cela sera impossible à Mes yeux? dit le Seigneur tout-puissant.
7 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani ndidzapulumutsa anthu anga kuchokera ku mayiko a kummawa ndi kumadzulo.
Voici ce que dit le Seigneur: Je sauverai Mon peuple des contrées de l'Orient et de celles de l'Occident;
8 Ndidzawabweretsa kuti adzakhale mu Yerusalemu; adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo, wokhulupirika ndi wolungama pakati pawo.”
et Je l'en ferai sortir, et Je le ramènerai au milieu de Jérusalem; et il sera Mon peuple, et Moi Je serai son Dieu de vérité et de justice.
9 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Inu amene tsopano mukumva mawu awa amene akuyankhula aneneri amene analipo pamene ankayika maziko a nyumba ya Yehova Wamphamvuzonse, ‘limbani mtima kuti mumange Nyumba ya Yehova.’
Voici ce que dit le Seigneur tout-puissant: Que vos mains soient fortes, ô vous qui entendez en ces jours les paroles de la bouche des prophètes, en ce jour où l'on a jeté les fondations de la maison du Seigneur tout-puissant, et où le temple a été relevé.
10 Mpaka nthawi imeneyi panalibe munthu wolandira malipiro pa ntchito kapena ndalama zolipirira nyama zogwira ntchito. Panalibe munthu amene ankadzigwirira ntchito mwamtendere chifukwa choopa adani ake, pakuti Ine ndinkawayambanitsa.
Car avant ces jours le salaire des hommes ne sera point lucratif, le travail des bêtes ne profitera point, et ceux qui sont entrés, ceux qui sont sortis, n'auront pas trouvé de paix, à cause de leurs afflictions. Et alors Je ferai marcher tous les hommes l'un contre l'autre.
11 Koma tsopano sindidzachitira otsala mwa anthu awa zomwe ndinachita kale,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Mais maintenant Je ne traiterai plus les restes de ce peuple comme aux jours d'autrefois, dit le Seigneur tout-puissant.
12 “Pakuti mbewu zidzamera bwino, mpesa udzabala zipatso zake, nthaka idzatulutsa zomera zake, ndi thambo lidzagwetsa mame. Ndidzapereka zonse kukhala cholowa cha otsala mwa anthu awa.
Je lui ferai connaître la paix. La vigne produira son fruit; la terre produira ses récoltes; le ciel donnera sa rosée, et au reste de Mon peuple Je laisserai toutes ces choses en héritage.
13 Monga mwakhala muli chinthu chotembereredwa pakati pa mitundu ina ya anthu, inu Yuda ndi Israeli, choncho ndidzakupulumutsani, ndipo mudzakhala dalitso. Musachite mantha, koma limbani mtima.”
Et voici ce qui arrivera: autant vous recevrez de malédictions chez les gentils, vous, maison d'Israël, autant Je mettrai de soins à vous sauver, et autant vous recevrez de bénédictions. Ayez bon courage, et fortifiez vos mains.
14 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Monga ndinatsimikiza mtima kubweretsa choyipa pa inu, komanso osakuchitirani chisoni pamene makolo anu anandikwiyitsa,” akutero Yehova,
Car voici ce que dit le Seigneur tout-puissant: De même que J'ai songé à vous affliger parce que vos pères avaient excité Mon courroux, dit le Seigneur tout-puissant,
15 “Choncho tsopano ndatsimikiza mtima kuchitiranso zabwino Yerusalemu ndi Yuda. Musachite mantha.
sans que Je M'en repente: de même Je suis disposé et Je songe, en ces jours, à combler de biens Jérusalem et la maison de Juda.
16 Zinthu zoti muchite ndi izi: Muziwuzana zoona zokhazokha, muziweruza moona ndi mwachilungamo mʼmabwalo anu;
Voici les choses que vous ferez: parlez selon la vérité à votre prochain; jugez devant vos portes selon la vérité, la justice et la paix.
17 musamachitire mnzanu chiwembu, musamakonde kulumbira zonama. Zonsezi Ine ndimadana nazo,” akutero Yehova.
Ne pensez pas à mal en vos discours contre votre prochain, et n'aimez pas le faux serment; car Je hais toutes ces choses, dit le Seigneur tout-puissant.
18 Yehova Wamphamvuzonse anayankhulanso nane.
Et la parole du Seigneur tout-puissant vint à moi, disant:
19 Ndipo ananena kuti, “Kusala zakudya kwa pa mwezi wachinayi, chisanu, chisanu ndi chiwiri ndi wakhumi, kudzakhala nthawi yachimwemwe, ya chisangalalo ndi nthawi ya madyerero chikondwerero kwa Yuda. Nʼchifukwa chake muzikonda choonadi ndi mtendere.”
Voici ce que dit le Seigneur tout-puissant: Le jeûne du quatrième mois, le jeûne du cinquième, le jeûne du septième, le jeûne du dixième, seront alors pour la maison de Juda un sujet de joie, d'allégresse et de bonnes fêtes; réjouissez-vous; aimez la vérité et la paix.
20 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu a mitundu yambiri ndi anthu okhala mʼmizinda yambiri adzabwerabe,
Voici ce que dit le Seigneur tout-puissant: Vous deviendrez encore un peuple nombreux, et vous habiterez beaucoup de villes.
21 ndipo nzika za mzinda wina zidzapita ku mzinda wina, kukanena kuti, ‘Tiyeni mwamsanga tikapemphe madalitso kwa Yehova ndi kukapembedza Yehova Wamphamvuzonse. Inenso ndikupita kumeneko.’
Et les habitants de cinq villes se réuniront en une seule, disant: Allons prier devant la face et sous les yeux du Seigneur tout-puissant; et Moi, J'irai à eux.
22 Anthu ambiri ndiponso a ku mayiko amphamvu adzabwera ku Yerusalemu kudzapembedza Yehova Wamphamvuzonse ndi kudzapempha madalitso.”
Et des peuples nombreux et des nations nombreuses viendront à Jérusalem chercher la face du Seigneur tout-puissant, et prier devant la face du Seigneur.
23 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Masiku amenewo anthu khumi ochokera ku mitundu ya anthu a ziyankhulo zosiyana adzagwira mkanjo wa Myuda ndi kunena kuti, ‘Tipite nawo, chifukwa tamva kuti Mulungu ali nanu.’”
Voici ce que dit le Seigneur tout-puissant: En ces jours, dix hommes de toutes les langues prendront par la frange de son manteau un homme de la Judée, disant: Nous irons avec toi, parce que nous avons ouï dire que Dieu est avec vous.