< Zekariya 8 >

1 Awa ndi mawu amene Yehova Wamphamvuzonse ananena.
Opět stalo se slovo Hospodina zástupů, řkoucí:
2 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndikuchitira nsanje yayikulu Ziyoni. Mtima wanga ukupweteka chifukwa cha nsanje pa iyeyo.”
Takto praví Hospodin zástupů: Horlil jsem pro Sion horlením velikým, nýbrž rozhněváním velikým horlil jsem pro něj.
3 Yehova akuti, “Ndidzabwerera ku Ziyoni ndi kukakhala ku Yerusalemu. Pamenepo Yerusalemu adzatchedwa Mzinda wa Choonadi ndipo phiri la Yehova Wamphamvuzonse lidzatchedwa Phiri Lopatulika.”
Takto praví Hospodin: Navrátil jsem se k Sionu, a bydlím u prostřed Jeruzaléma, aby sloul Jeruzalém městem věrným, a hora Hospodina zástupů horou svatosti.
4 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Abambo ndi amayi okalamba adzakhalanso mʼmisewu ya mu Yerusalemu, aliyense ali ndi ndodo mʼmanja mwake chifukwa cha kuchuluka kwa masiku ake.
Takto praví Hospodin zástupů: Ještěť sedati budou starci i baby na ulicích Jeruzalémských, maje každý z nich hůl v ruce své pro sešlost věku.
5 Ndipo misewu ya mu mzindamo idzadzaza ndi anyamata ndi atsikana akusewera.”
Ulice také města plné budou pacholat a děvčat, hrajících na ulicích jeho.
6 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ngati zikuoneka kuti nʼzosatheka kwa anthu otsala pa nthawi ino, kodi zidzakhala zosathekanso kwa Ine?” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Takto praví Hospodin zástupů: Zdali, že se to nepodobné zdá před očima ostatků lidu tohoto dnů těchto, také před očima mýma nepodobné bude? praví Hospodin zástupů.
7 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani ndidzapulumutsa anthu anga kuchokera ku mayiko a kummawa ndi kumadzulo.
Takto praví Hospodin zástupů: Aj, já vysvobozuji lid svůj z země východní, a z země na západ slunce,
8 Ndidzawabweretsa kuti adzakhale mu Yerusalemu; adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo, wokhulupirika ndi wolungama pakati pawo.”
A přivedu je zase. I budou bydliti u prostřed Jeruzaléma, a budou lidem mým, a já budu jejich Bohem v pravdě a v spravedlnosti.
9 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Inu amene tsopano mukumva mawu awa amene akuyankhula aneneri amene analipo pamene ankayika maziko a nyumba ya Yehova Wamphamvuzonse, ‘limbani mtima kuti mumange Nyumba ya Yehova.’
Takto praví Hospodin zástupů: Posilňtež se ruce vaše, kteříž jste slyšeli těchto dnů slova tato z úst proroků, od toho dne, v němž založen jest dům Hospodina zástupů, že má chrám dostaven býti.
10 Mpaka nthawi imeneyi panalibe munthu wolandira malipiro pa ntchito kapena ndalama zolipirira nyama zogwira ntchito. Panalibe munthu amene ankadzigwirira ntchito mwamtendere chifukwa choopa adani ake, pakuti Ine ndinkawayambanitsa.
Nebo před těmito dny práce lidská, ani práce hovádek se nenahražovala, nýbrž ani vycházejícímu ani vcházejícímu nebylo pokoje pro nepřítele, nebo já spustil jsem všecky lidi jedny s druhými.
11 Koma tsopano sindidzachitira otsala mwa anthu awa zomwe ndinachita kale,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Nyní pak, ne jako ve dnech těch předešlých, činím ostatkům lidu tohoto, praví Hospodin zástupů.
12 “Pakuti mbewu zidzamera bwino, mpesa udzabala zipatso zake, nthaka idzatulutsa zomera zake, ndi thambo lidzagwetsa mame. Ndidzapereka zonse kukhala cholowa cha otsala mwa anthu awa.
Ale rozsívání máte pokojné, vinný kmen vydává ovoce své, a země vydává úrodu svou, nebesa také dávají rosu svou, a to všecko dávám v dědictví ostatkům lidu tohoto.
13 Monga mwakhala muli chinthu chotembereredwa pakati pa mitundu ina ya anthu, inu Yuda ndi Israeli, choncho ndidzakupulumutsani, ndipo mudzakhala dalitso. Musachite mantha, koma limbani mtima.”
A tak stane se, že jakož jste byli zlořečením mezi pohany, ó dome Judský a dome Izraelský, tak zase vás chrániti budu, a budete požehnáním. Nebojtež se, posilňte se ruce vaše.
14 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Monga ndinatsimikiza mtima kubweretsa choyipa pa inu, komanso osakuchitirani chisoni pamene makolo anu anandikwiyitsa,” akutero Yehova,
Nebo takto praví Hospodin zástupů: Jakož jsem byl myslil zle učiniti vám, když mne hněvali otcové vaši, praví Hospodin zástupů, aniž jsem litoval:
15 “Choncho tsopano ndatsimikiza mtima kuchitiranso zabwino Yerusalemu ndi Yuda. Musachite mantha.
Tak obrátě se, myslím v těchto dnech dobře činiti Jeruzalému a domu Judskému. Nebojtež se.
16 Zinthu zoti muchite ndi izi: Muziwuzana zoona zokhazokha, muziweruza moona ndi mwachilungamo mʼmabwalo anu;
Tyto pak věci jsou, kteréž činiti budete: Mluvte pravdu každý s bližním svým, pravý a pokojný soud vynášejte v branách svých.
17 musamachitire mnzanu chiwembu, musamakonde kulumbira zonama. Zonsezi Ine ndimadana nazo,” akutero Yehova.
Aniž kdo bližnímu svému zlého obmýšlej v srdci svém, též přísahy falešné nemilujte; nebo všecko to jest, čehož nenávidím, praví Hospodin.
18 Yehova Wamphamvuzonse anayankhulanso nane.
I stalo se slovo Hospodina zástupů ke mně, řkoucí:
19 Ndipo ananena kuti, “Kusala zakudya kwa pa mwezi wachinayi, chisanu, chisanu ndi chiwiri ndi wakhumi, kudzakhala nthawi yachimwemwe, ya chisangalalo ndi nthawi ya madyerero chikondwerero kwa Yuda. Nʼchifukwa chake muzikonda choonadi ndi mtendere.”
Takto praví Hospodin zástupů: Půst čtvrtého měsíce, a půst pátého, a půst sedmého, a půst desátého obrátí se domu Judskému v radost a veselí, i v slavnosti rozkošné, ale pravdu a pokoj milujte.
20 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu a mitundu yambiri ndi anthu okhala mʼmizinda yambiri adzabwerabe,
Takto praví Hospodin zástupů: Ještěť budou přicházeti národové a obyvatelé měst mnohých,
21 ndipo nzika za mzinda wina zidzapita ku mzinda wina, kukanena kuti, ‘Tiyeni mwamsanga tikapemphe madalitso kwa Yehova ndi kukapembedza Yehova Wamphamvuzonse. Inenso ndikupita kumeneko.’
Přicházeti budou, pravím, obyvatelé jednoho k druhému, řkouce: Poďmež s ochotností kořiti se tváři Hospodinově, a hledati Hospodina zástupů. Půjdu i já.
22 Anthu ambiri ndiponso a ku mayiko amphamvu adzabwera ku Yerusalemu kudzapembedza Yehova Wamphamvuzonse ndi kudzapempha madalitso.”
A tak přijdou lidé mnozí a národové nesčíslní, aby hledali Hospodina zástupů v Jeruzalémě, a kořili se tváři Hospodinově.
23 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Masiku amenewo anthu khumi ochokera ku mitundu ya anthu a ziyankhulo zosiyana adzagwira mkanjo wa Myuda ndi kunena kuti, ‘Tipite nawo, chifukwa tamva kuti Mulungu ali nanu.’”
Takto praví Hospodin zástupů: V těch dnech chopí se deset mužů ze všech jazyků těch národů, chopí se, pravím, podolka jednoho Žida, řkouce: Půjdeme s vámi; nebo slyšíme, že jest Bůh s vámi.

< Zekariya 8 >