< Zekariya 7 >
1 Pa chaka chachinayi cha Mfumu Dariyo, pa tsiku lachinayi la Kisilevi, mwezi wachisanu ndi chinayi, Yehova anayankhula ndi Zekariya.
Aconteceu pois, no anno quarto do rei Dario, que a palavra do Senhor veiu a Zacharias, no dia quarto do nono mez, que é chisleu.
2 Anthu a ku Beteli anali atatuma Sarezeri ndi Regemu-Meleki pamodzi ndi anthu awo, kuti akapemphe chifundo kwa Yehova
Quando foram enviados á casa de Deus, Saresar, e Regemmelech, e os homens d'elle, para supplicarem o rosto do Senhor,
3 pokafunsa kwa ansembe a ku Nyumba ya Yehova Wamphamvuzonse ndi aneneri kuti, “Kodi ine ndizilira ndi kusala zakudya pa mwezi wachisanu, monga mmene ndakhala ndikuchitira pa zaka zambiri?”
Dizendo aos sacerdotes, que estavam na casa do Senhor dos Exercitos, e aos prophetas: Chorarei eu no quinto mez, separando-me, como o tenho feito por tantos annos?
4 Pamenepo Yehova Wamphamvuzonse anayankhula nane kuti,
Então a palavra do Senhor dos Exercitos veiu a mim, dizendo:
5 “Funsa anthu onse a mʼdziko ndi ansembe kuti, ‘Pamene munkasala zakudya pa mwezi wachisanu ndi wachisanu ndi chiwiri pa zaka 70 zapitazi, kodi munkasala chifukwa cha Ine?
Falla a todo o povo d'esta terra, o aos sacerdotes, dizendo: Quando jejuastes, e pranteastes, no quinto e no setimo mez, a saber, estes setenta annos, porventura, jejuando, jejuastes para mim, para mim, digo?
6 Ndipo pamene munkadya ndi kumwa, kodi simunkachita zimenezi podzisangalatsa nokha?
Ou quando comestes, e quando bebestes, não fostes vós os que comieis e vós os que bebieis?
7 Kodi awa si mawu amene Yehova ankanena kudzera mwa aneneri oyamba aja pamene Yerusalemu ndi mizinda yake yozungulira anali pa mtendere ndi pa ulemerero, ndi pamene Negevi ndi ku madera akumadzulo a mʼmbali mwa phiri munali anthu?’”
Não são estas as palavras que o Senhor prégou pelo ministerio dos prophetas primeiros, quando Jerusalem estava habitada e quieta, com as suas cidades ao redor d'ella? e o sul e a campina eram habitados?
8 Ndipo Yehova anayankhulanso ndi Zekariya kuti,
E a palavra do Senhor veiu a Zacharias, dizendo:
9 “Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Muziweruza molungama; muzichitirana chifundo ndi kumverana chisoni.
Assim fallou o Senhor dos Exercitos, dizendo: Julgae juizo verdadeiro, executae piedade e misericordias cada um com seu irmão;
10 Musamazunze akazi amasiye kapena ana amasiye, alendo kapena osauka. Musamaganizirane zoyipa mʼmitima mwanu.’
E não opprimaes a viuva, nem o orphão, nem o estrangeiro, nem o pobre, nem intente o mal cada um contra o seu irmão no seu coração.
11 “Koma makolo anu anakana kumvera uthenga umenewu; anawumitsa mtima nandifulatira, natseka makutu awo kuti asamve.
Porém não quizeram escutar, e me deram o hombro rebelde, e ensurdeceram os seus ouvidos, para que não ouvissem.
12 Anawumitsa mitima yawo ngati mwala wa sangalabwi ndipo sanamvere lamulo kapena mawu amene Yehova Wamphamvuzonse anawatumiza mwa Mzimu wake kudzera mwa aneneri oyamba aja. Kotero Yehova Wamphamvuzonse anakwiya kwambiri.
E fizeram o seu coração como diamante, para que não ouvissem a lei, nem as palavras que o Senhor dos Exercitos enviava pelo seu Espirito pelo ministerio dos prophetas primeiros: d'onde veiu a grande ira do Senhor dos Exercitos.
13 “‘Pamene ndinawayitana, iwo sanamvere; choncho pamene iwo anandiyitana, Ine sindinamverenso,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
E aconteceu que, como elle clamou, e elles não ouviram, assim tambem elles clamaram, mas eu não ouvi, diz o Senhor dos Exercitos.
14 ‘Ndinawamwaza ndi kamvuluvulu pakati pa mitundu yonse ya anthu, kumene anali alendo. Dziko lawo linatsala litasakazidwa kwambiri kotero kuti palibe amene amabwera kapena kupitamo. Umu ndi mmene anasandutsira dziko labwino kukhala chipululu.’”
E os espalhei com tempestade entre todas as nações, que elles não conheciam, e a terra foi assolada atraz d'elles, de sorte que ninguem passava por ella, nem se tornava: porque teem feito da terra desejada uma desolação.