< Zekariya 7 >

1 Pa chaka chachinayi cha Mfumu Dariyo, pa tsiku lachinayi la Kisilevi, mwezi wachisanu ndi chinayi, Yehova anayankhula ndi Zekariya.
Et il arriva dans la quatrième année du roi Darius, que la parole du Seigneur fut adressée à Zacharie, au quatrième jour du neuvième mois, qui est appelé Casleu.
2 Anthu a ku Beteli anali atatuma Sarezeri ndi Regemu-Meleki pamodzi ndi anthu awo, kuti akapemphe chifundo kwa Yehova
Or Sarasar et Rogommélech et les hommes qui étaient avec lui, envoyèrent à la maison de Dieu pour implorer la face du Seigneur,
3 pokafunsa kwa ansembe a ku Nyumba ya Yehova Wamphamvuzonse ndi aneneri kuti, “Kodi ine ndizilira ndi kusala zakudya pa mwezi wachisanu, monga mmene ndakhala ndikuchitira pa zaka zambiri?”
Afin de parler aux prêtres de la maison du Seigneur des armées et aux prophètes, en leur disant: Faut-il que je pleure dans le cinquième mois, ou dois-je me sanctifier comme je l’ai déjà fait pendant beaucoup d’années?
4 Pamenepo Yehova Wamphamvuzonse anayankhula nane kuti,
Et la parole du Seigneur des armées me fut adressée, disant:
5 “Funsa anthu onse a mʼdziko ndi ansembe kuti, ‘Pamene munkasala zakudya pa mwezi wachisanu ndi wachisanu ndi chiwiri pa zaka 70 zapitazi, kodi munkasala chifukwa cha Ine?
Parle à tout le peuple de la terre et aux prêtres, en disant: Lorsque vous avez jeûné et pleuré dans le cinquième et le septième mois, pendant ces soixante-dix années, est-ce pour moi que vous avez jeûné?
6 Ndipo pamene munkadya ndi kumwa, kodi simunkachita zimenezi podzisangalatsa nokha?
Et lorsque vous avez mangé et que vous avez bu, n’est-ce pas pour vous que vous avez mangé et pour vous que vous avez bu?
7 Kodi awa si mawu amene Yehova ankanena kudzera mwa aneneri oyamba aja pamene Yerusalemu ndi mizinda yake yozungulira anali pa mtendere ndi pa ulemerero, ndi pamene Negevi ndi ku madera akumadzulo a mʼmbali mwa phiri munali anthu?’”
Ne sont-ce pas là les paroles qu’a dites le Seigneur par l’entremise des prophètes antérieurs, lorsque Jérusalem était encore habitée, et qu’elle était opulente, elle-même et les villes autour d’elle, et qu’au midi et dans la plaine tout était habité?
8 Ndipo Yehova anayankhulanso ndi Zekariya kuti,
Et la parole du Seigneur des armées fut adressée à Zacharie, disant:
9 “Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Muziweruza molungama; muzichitirana chifundo ndi kumverana chisoni.
Voici ce que dit le Seigneur des armées: Jugez selon la vérité, usez de miséricorde et de clémence, chacun envers son frère.
10 Musamazunze akazi amasiye kapena ana amasiye, alendo kapena osauka. Musamaganizirane zoyipa mʼmitima mwanu.’
Et n’opprimez point la veuve, ni l’orphelin, ni l’étranger, ni le pauvre; et qu’un homme ne médite pas dans son cœur le mal contre son frère.
11 “Koma makolo anu anakana kumvera uthenga umenewu; anawumitsa mtima nandifulatira, natseka makutu awo kuti asamve.
Mais vos pères n’ont pas voulu être attentifs à ma voix, et ils ont détourné l’épaule en se retirant, et ils ont appesanti leurs oreilles pour ne pas entendre.
12 Anawumitsa mitima yawo ngati mwala wa sangalabwi ndipo sanamvere lamulo kapena mawu amene Yehova Wamphamvuzonse anawatumiza mwa Mzimu wake kudzera mwa aneneri oyamba aja. Kotero Yehova Wamphamvuzonse anakwiya kwambiri.
Et leur cœur, ils l’ont rendu dur comme un diamant, pour ne pas écouter la loi et la parole que le Seigneur des armées leur envoya avec son esprit, par l’entremise de ses prophètes antérieurs; et le Seigneur des armées conçut une grande indignation.
13 “‘Pamene ndinawayitana, iwo sanamvere; choncho pamene iwo anandiyitana, Ine sindinamverenso,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Or il est arrivé comme il a parlé, et ils n’ont pas écouté; ainsi ils crieront, et je ne les écouterai pas, dit le Seigneur des armées.
14 ‘Ndinawamwaza ndi kamvuluvulu pakati pa mitundu yonse ya anthu, kumene anali alendo. Dziko lawo linatsala litasakazidwa kwambiri kotero kuti palibe amene amabwera kapena kupitamo. Umu ndi mmene anasandutsira dziko labwino kukhala chipululu.’”
Et je les ai dispersés dans tous les royaumes qu’ils ne connaissent pas; et leur terre a été désolée derrière eux, en sorte qu’il n’y avait personne qui y passât, et qui en revînt; et ils ont fait d’une terre délicieuse un désert.

< Zekariya 7 >