< Zekariya 7 >
1 Pa chaka chachinayi cha Mfumu Dariyo, pa tsiku lachinayi la Kisilevi, mwezi wachisanu ndi chinayi, Yehova anayankhula ndi Zekariya.
II arriva, dans la quatrième année du roi Darius, que la parole de l’Eternel fut adressée à Zacharie le quatrième jour du neuvième mois, de Kislev.
2 Anthu a ku Beteli anali atatuma Sarezeri ndi Regemu-Meleki pamodzi ndi anthu awo, kuti akapemphe chifundo kwa Yehova
La ville de Béthel avait envoyé Charécer, Réghem-Mélec et ses gens pour disposer favorablement l’Eternel,
3 pokafunsa kwa ansembe a ku Nyumba ya Yehova Wamphamvuzonse ndi aneneri kuti, “Kodi ine ndizilira ndi kusala zakudya pa mwezi wachisanu, monga mmene ndakhala ndikuchitira pa zaka zambiri?”
et pour poser aux prêtres qui sont au service de la maison de l’Eternel et aux prophètes la question suivante: "Continuerai-je à pleurer au cinquième mois en pratiquant des abstinences, comme je l’ai fait voilà plusieurs années?"
4 Pamenepo Yehova Wamphamvuzonse anayankhula nane kuti,
Alors la parole de l’Eternel me fut adressée en ces termes:
5 “Funsa anthu onse a mʼdziko ndi ansembe kuti, ‘Pamene munkasala zakudya pa mwezi wachisanu ndi wachisanu ndi chiwiri pa zaka 70 zapitazi, kodi munkasala chifukwa cha Ine?
"Porte à tout le peuple du pays et aux prêtres la parole que voici: Quand vous avez jeûné et gardé le deuil au cinquième et au septième mois, et cela durant soixante-dix années, est-ce donc pour moi que vous avez observé ce jeûne?
6 Ndipo pamene munkadya ndi kumwa, kodi simunkachita zimenezi podzisangalatsa nokha?
Et quand vous mangez et que vous buvez, n’est-ce pas vous qui mangez, et n’est-ce pas vous qui buvez?
7 Kodi awa si mawu amene Yehova ankanena kudzera mwa aneneri oyamba aja pamene Yerusalemu ndi mizinda yake yozungulira anali pa mtendere ndi pa ulemerero, ndi pamene Negevi ndi ku madera akumadzulo a mʼmbali mwa phiri munali anthu?’”
Ne sont-ce pas là les paroles que l’Eternel proclama par l’organe des anciens prophètes, alors que Jérusalem était habitée et paisible de même que ses villes autour d’elle, et alors que le Midi en même temps que la Plaine était habité?"
8 Ndipo Yehova anayankhulanso ndi Zekariya kuti,
Puis la parole de l’Eternel fut adressée à Zacharie en ces termes:
9 “Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Muziweruza molungama; muzichitirana chifundo ndi kumverana chisoni.
"Ainsi parle l’Eternel-Cebaot: Rendez des jugements de vérité, pratiquez l’un envers l’autre la charité et la pitié.
10 Musamazunze akazi amasiye kapena ana amasiye, alendo kapena osauka. Musamaganizirane zoyipa mʼmitima mwanu.’
N’Opprimez pas la veuve et l’orphelin, l’étranger et le pauvre; ne méditez pas dans votre cœur de méchanceté l’un contre l’autre.
11 “Koma makolo anu anakana kumvera uthenga umenewu; anawumitsa mtima nandifulatira, natseka makutu awo kuti asamve.
Mais autrefois on avait refusé d’écouter, on avait présenté une nuque rebelle, on s’était bouché les oreilles pour ne pas entendre.
12 Anawumitsa mitima yawo ngati mwala wa sangalabwi ndipo sanamvere lamulo kapena mawu amene Yehova Wamphamvuzonse anawatumiza mwa Mzimu wake kudzera mwa aneneri oyamba aja. Kotero Yehova Wamphamvuzonse anakwiya kwambiri.
On avait rendu son cœur dur comme du diamant, pour rester sourd à l’enseignement et aux paroles dont l’Eternel-Cebaot, par son inspiration, avait chargé les anciens prophètes. Et il y eut un grand courroux de la part de l’Eternel-Cebaot.
13 “‘Pamene ndinawayitana, iwo sanamvere; choncho pamene iwo anandiyitana, Ine sindinamverenso,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Et de même qu’il avait appelé sans être écouté, ainsi appelaient-ils à leur tour sans que j’écoutasse, dit l’Eternel-Cebaot.
14 ‘Ndinawamwaza ndi kamvuluvulu pakati pa mitundu yonse ya anthu, kumene anali alendo. Dziko lawo linatsala litasakazidwa kwambiri kotero kuti palibe amene amabwera kapena kupitamo. Umu ndi mmene anasandutsira dziko labwino kukhala chipululu.’”
Je les ai dispersés parmi tous les peuples qu’ils ne connaissaient point, et le pays a été désolé derrière eux, abandonné par tout allant et venant. Ainsi ils ont fait d’un pays délicieux une solitude."