< Zekariya 7 >

1 Pa chaka chachinayi cha Mfumu Dariyo, pa tsiku lachinayi la Kisilevi, mwezi wachisanu ndi chinayi, Yehova anayankhula ndi Zekariya.
Et il arriva, la quatrième année du roi Darius, que la parole de l’Éternel vint à Zacharie, le quatrième [jour] du neuvième mois, [au mois] de Kislev,
2 Anthu a ku Beteli anali atatuma Sarezeri ndi Regemu-Meleki pamodzi ndi anthu awo, kuti akapemphe chifundo kwa Yehova
quand Béthel envoya Sharétser et Réguem-Mélec et ses hommes pour implorer l’Éternel,
3 pokafunsa kwa ansembe a ku Nyumba ya Yehova Wamphamvuzonse ndi aneneri kuti, “Kodi ine ndizilira ndi kusala zakudya pa mwezi wachisanu, monga mmene ndakhala ndikuchitira pa zaka zambiri?”
pour parler aux sacrificateurs qui étaient dans la maison de l’Éternel des armées, et aux prophètes, disant: Pleurerai-je au cinquième mois, en me séparant comme j’ai fait, voici tant d’années?
4 Pamenepo Yehova Wamphamvuzonse anayankhula nane kuti,
Et la parole de l’Éternel des armées vint à moi, disant:
5 “Funsa anthu onse a mʼdziko ndi ansembe kuti, ‘Pamene munkasala zakudya pa mwezi wachisanu ndi wachisanu ndi chiwiri pa zaka 70 zapitazi, kodi munkasala chifukwa cha Ine?
Parle à tout le peuple du pays, et aux sacrificateurs, disant: Quand vous avez jeûné et que vous vous êtes lamentés au cinquième et au septième [mois], et cela pendant 70 ans, est-ce réellement pour moi, pour moi, que vous avez jeûné?
6 Ndipo pamene munkadya ndi kumwa, kodi simunkachita zimenezi podzisangalatsa nokha?
Et quand vous avez mangé et bu, n’est-ce pas vous qui mangiez et qui buviez?
7 Kodi awa si mawu amene Yehova ankanena kudzera mwa aneneri oyamba aja pamene Yerusalemu ndi mizinda yake yozungulira anali pa mtendere ndi pa ulemerero, ndi pamene Negevi ndi ku madera akumadzulo a mʼmbali mwa phiri munali anthu?’”
Ne sont-ce pas là les paroles que l’Éternel a criées par les premiers prophètes, alors que Jérusalem était habitée et jouissait de la paix, ainsi que ses villes qui l’entouraient, et que le midi et le pays plat étaient habités?
8 Ndipo Yehova anayankhulanso ndi Zekariya kuti,
Et la parole de l’Éternel vint à Zacharie, disant:
9 “Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Muziweruza molungama; muzichitirana chifundo ndi kumverana chisoni.
Ainsi parle l’Éternel des armées, disant: Prononcez des jugements de vérité, et usez de bonté et de miséricorde l’un envers l’autre,
10 Musamazunze akazi amasiye kapena ana amasiye, alendo kapena osauka. Musamaganizirane zoyipa mʼmitima mwanu.’
et n’opprimez pas la veuve et l’orphelin, l’étranger et l’affligé; et ne méditez pas le mal dans votre cœur, l’un contre l’autre.
11 “Koma makolo anu anakana kumvera uthenga umenewu; anawumitsa mtima nandifulatira, natseka makutu awo kuti asamve.
Mais ils refusèrent d’être attentifs, et opposèrent une épaule revêche, et appesantirent leurs oreilles pour ne pas entendre,
12 Anawumitsa mitima yawo ngati mwala wa sangalabwi ndipo sanamvere lamulo kapena mawu amene Yehova Wamphamvuzonse anawatumiza mwa Mzimu wake kudzera mwa aneneri oyamba aja. Kotero Yehova Wamphamvuzonse anakwiya kwambiri.
et rendirent leur cœur [dur comme] un diamant, pour ne pas écouter la loi et les paroles que l’Éternel des armées envoyait par son Esprit, par les premiers prophètes; et il y eut une grande colère de la part de l’Éternel des armées.
13 “‘Pamene ndinawayitana, iwo sanamvere; choncho pamene iwo anandiyitana, Ine sindinamverenso,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Et il arriva que, comme il cria et qu’ils n’écoutèrent pas, de même ils crièrent, et je n’écoutai pas, dit l’Éternel des armées;
14 ‘Ndinawamwaza ndi kamvuluvulu pakati pa mitundu yonse ya anthu, kumene anali alendo. Dziko lawo linatsala litasakazidwa kwambiri kotero kuti palibe amene amabwera kapena kupitamo. Umu ndi mmene anasandutsira dziko labwino kukhala chipululu.’”
et je les dispersai, comme par un tourbillon, parmi toutes les nations qu’ils ne connaissaient pas, et le pays fut désolé derrière eux, de sorte qu’il n’y avait ni allants ni venants; et ils rendirent désolé le pays désirable.

< Zekariya 7 >