< Zekariya 7 >
1 Pa chaka chachinayi cha Mfumu Dariyo, pa tsiku lachinayi la Kisilevi, mwezi wachisanu ndi chinayi, Yehova anayankhula ndi Zekariya.
La quatrième année du roi Darius, la parole de Yahvé fut adressée à Zacharie, le quatrième jour du neuvième mois, le mois de Chislev.
2 Anthu a ku Beteli anali atatuma Sarezeri ndi Regemu-Meleki pamodzi ndi anthu awo, kuti akapemphe chifundo kwa Yehova
Le peuple de Béthel envoya Sharezer, Regem Melech et leurs hommes pour implorer la faveur de Yahvé,
3 pokafunsa kwa ansembe a ku Nyumba ya Yehova Wamphamvuzonse ndi aneneri kuti, “Kodi ine ndizilira ndi kusala zakudya pa mwezi wachisanu, monga mmene ndakhala ndikuchitira pa zaka zambiri?”
et pour parler aux prêtres de la maison de Yahvé des armées et aux prophètes, en disant: « Devrais-je pleurer au cinquième mois, en me séparant, comme je l'ai fait pendant tant d'années? »
4 Pamenepo Yehova Wamphamvuzonse anayankhula nane kuti,
Alors la parole de Yahvé des armées me fut adressée en ces termes:
5 “Funsa anthu onse a mʼdziko ndi ansembe kuti, ‘Pamene munkasala zakudya pa mwezi wachisanu ndi wachisanu ndi chiwiri pa zaka 70 zapitazi, kodi munkasala chifukwa cha Ine?
Parle à tout le peuple du pays et aux prêtres, et dis: « Lorsque vous avez jeûné et pleuré au cinquième et au septième mois pendant ces soixante-dix ans, n'avez-vous pas jeûné pour moi, vraiment pour moi?
6 Ndipo pamene munkadya ndi kumwa, kodi simunkachita zimenezi podzisangalatsa nokha?
Quand vous mangez et quand vous buvez, ne mangez-vous pas pour vous-mêmes et ne buvez-vous pas pour vous-mêmes?
7 Kodi awa si mawu amene Yehova ankanena kudzera mwa aneneri oyamba aja pamene Yerusalemu ndi mizinda yake yozungulira anali pa mtendere ndi pa ulemerero, ndi pamene Negevi ndi ku madera akumadzulo a mʼmbali mwa phiri munali anthu?’”
Ne sont-ce pas là les paroles que Yahvé a annoncées par les anciens prophètes, lorsque Jérusalem était habitée et prospère, ainsi que les villes qui l'entouraient, et que le Sud et la plaine étaient habités? ».
8 Ndipo Yehova anayankhulanso ndi Zekariya kuti,
La parole de Yahvé fut adressée à Zacharie, en ces termes:
9 “Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Muziweruza molungama; muzichitirana chifundo ndi kumverana chisoni.
Yahvé des armées a parlé ainsi: « Pratiquez un jugement équitable, et ayez de la bonté et de la compassion pour votre frère.
10 Musamazunze akazi amasiye kapena ana amasiye, alendo kapena osauka. Musamaganizirane zoyipa mʼmitima mwanu.’
N'opprimez pas la veuve, ni l'orphelin, ni l'étranger, ni le pauvre; et qu'aucun de vous ne médite dans son cœur le mal contre son frère.
11 “Koma makolo anu anakana kumvera uthenga umenewu; anawumitsa mtima nandifulatira, natseka makutu awo kuti asamve.
Mais ils refusèrent d'écouter, ils tournèrent le dos et bouchèrent leurs oreilles pour ne pas entendre.
12 Anawumitsa mitima yawo ngati mwala wa sangalabwi ndipo sanamvere lamulo kapena mawu amene Yehova Wamphamvuzonse anawatumiza mwa Mzimu wake kudzera mwa aneneri oyamba aja. Kotero Yehova Wamphamvuzonse anakwiya kwambiri.
Oui, ils ont rendu leur cœur dur comme du silex, de peur d'entendre la loi et les paroles que Yahvé des armées avait envoyées par son Esprit par les anciens prophètes. C'est pourquoi une grande colère est venue de l'Éternel des armées.
13 “‘Pamene ndinawayitana, iwo sanamvere; choncho pamene iwo anandiyitana, Ine sindinamverenso,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
De même qu'il a appelé et qu'ils ont refusé d'écouter, de même ils appelleront et je n'écouterai pas, dit Yahvé des armées,
14 ‘Ndinawamwaza ndi kamvuluvulu pakati pa mitundu yonse ya anthu, kumene anali alendo. Dziko lawo linatsala litasakazidwa kwambiri kotero kuti palibe amene amabwera kapena kupitamo. Umu ndi mmene anasandutsira dziko labwino kukhala chipululu.’”
mais je les disperserai dans un tourbillon parmi toutes les nations qu'ils n'ont pas connues. C'est ainsi que le pays a été dévasté après eux, de sorte que personne n'y passait ni n'y retournait, car ils ont rendu désolant le pays agréable. »