< Zekariya 7 >

1 Pa chaka chachinayi cha Mfumu Dariyo, pa tsiku lachinayi la Kisilevi, mwezi wachisanu ndi chinayi, Yehova anayankhula ndi Zekariya.
And it came to pass, in the fourth year of Darius the king, that the word of Yahweh came unto Zechariah, on the fourth of the ninth month, in Chisleu;
2 Anthu a ku Beteli anali atatuma Sarezeri ndi Regemu-Meleki pamodzi ndi anthu awo, kuti akapemphe chifundo kwa Yehova
yea when Bethel sent Sherezer and Regemmelech, and his men, —to pacify the face of Yahweh:
3 pokafunsa kwa ansembe a ku Nyumba ya Yehova Wamphamvuzonse ndi aneneri kuti, “Kodi ine ndizilira ndi kusala zakudya pa mwezi wachisanu, monga mmene ndakhala ndikuchitira pa zaka zambiri?”
to speak unto the priests that pertained to the house of Yahweh of hosts, and unto the prophets, saying, —Shall I weep in the fifth month, separating myself, as I have done these so many years?
4 Pamenepo Yehova Wamphamvuzonse anayankhula nane kuti,
Then came the word of Yahweh of hosts unto me, saying:
5 “Funsa anthu onse a mʼdziko ndi ansembe kuti, ‘Pamene munkasala zakudya pa mwezi wachisanu ndi wachisanu ndi chiwiri pa zaka 70 zapitazi, kodi munkasala chifukwa cha Ine?
Speak thou unto all the people of the land, and unto the priests, saying, —When ye fasted and lamented in the fifth and in the seventh, even these seventy years, did ye, really fast, unto, me?
6 Ndipo pamene munkadya ndi kumwa, kodi simunkachita zimenezi podzisangalatsa nokha?
And, when ye used to eat and when ye used to drink, was it not, of your own accord, ye did eat, and, of your own accord, ye did drink?
7 Kodi awa si mawu amene Yehova ankanena kudzera mwa aneneri oyamba aja pamene Yerusalemu ndi mizinda yake yozungulira anali pa mtendere ndi pa ulemerero, ndi pamene Negevi ndi ku madera akumadzulo a mʼmbali mwa phiri munali anthu?’”
Should ye not [have been doing] the things which Yahweh, had proclaimed, by the hand of the former prophets, while yet Jerusalem was inhabited and in peace, with her cities round about her, —and the South and the Lowland were inhabited?
8 Ndipo Yehova anayankhulanso ndi Zekariya kuti,
And the word of Yahweh came unto Zechariah, saying:
9 “Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Muziweruza molungama; muzichitirana chifundo ndi kumverana chisoni.
Thus, spake Yahweh of hosts, saying, —With true justice, give ye judgment, and, lovingkindness and compassions, observe ye, one with another;
10 Musamazunze akazi amasiye kapena ana amasiye, alendo kapena osauka. Musamaganizirane zoyipa mʼmitima mwanu.’
And, the widow and the fatherless, the sojourner and the humbled, do not ye oppress, —and, wickedness between one man and another, do not ye devise in your hearts.
11 “Koma makolo anu anakana kumvera uthenga umenewu; anawumitsa mtima nandifulatira, natseka makutu awo kuti asamve.
Howbeit they refused to give heed, but put forth a rebellious shoulder, —and, their ears, made they hard of hearing, that they might not hear;
12 Anawumitsa mitima yawo ngati mwala wa sangalabwi ndipo sanamvere lamulo kapena mawu amene Yehova Wamphamvuzonse anawatumiza mwa Mzimu wake kudzera mwa aneneri oyamba aja. Kotero Yehova Wamphamvuzonse anakwiya kwambiri.
and, their heart, turned they into adamant, that they might not hear the law, nor the words which Yahweh of hosts sent by his spirit, through the former prophets, —and so there came great wrath from Yahweh of hosts.
13 “‘Pamene ndinawayitana, iwo sanamvere; choncho pamene iwo anandiyitana, Ine sindinamverenso,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Therefore came it to pass that—just as he cried out and they hearkened not, so, used they to cry out, and I used not to hearken, saith Yahweh of hosts;
14 ‘Ndinawamwaza ndi kamvuluvulu pakati pa mitundu yonse ya anthu, kumene anali alendo. Dziko lawo linatsala litasakazidwa kwambiri kotero kuti palibe amene amabwera kapena kupitamo. Umu ndi mmene anasandutsira dziko labwino kukhala chipululu.’”
But I whirled them over all the nations whom they had not known, and, the land, was made desolate after them, that none passed through and returned, —Yea they made of a delightful land—a desolation.

< Zekariya 7 >