< Zekariya 7 >

1 Pa chaka chachinayi cha Mfumu Dariyo, pa tsiku lachinayi la Kisilevi, mwezi wachisanu ndi chinayi, Yehova anayankhula ndi Zekariya.
I Kong Darius's fjerde Regeringsaar kom HERRENS Ord til Zakarias paa den fjerde Dag i den niende Maaned, Kislev.
2 Anthu a ku Beteli anali atatuma Sarezeri ndi Regemu-Meleki pamodzi ndi anthu awo, kuti akapemphe chifundo kwa Yehova
Da sendte Betel-Sar'ezer og Regem-Melek og hans Mænd Bud for at bede HERREN om Naade
3 pokafunsa kwa ansembe a ku Nyumba ya Yehova Wamphamvuzonse ndi aneneri kuti, “Kodi ine ndizilira ndi kusala zakudya pa mwezi wachisanu, monga mmene ndakhala ndikuchitira pa zaka zambiri?”
og spørge Præsterne ved Hærskarers HERRES Hus og Profeterne: »Skal jeg græde og spæge mig i den femte Maaned, som jeg nu har gjort i saa mange Aar?«
4 Pamenepo Yehova Wamphamvuzonse anayankhula nane kuti,
Da kom Hærskarers HERRES Ord til mig saaledes:
5 “Funsa anthu onse a mʼdziko ndi ansembe kuti, ‘Pamene munkasala zakudya pa mwezi wachisanu ndi wachisanu ndi chiwiri pa zaka 70 zapitazi, kodi munkasala chifukwa cha Ine?
Sig til alt Folket i Landet og til Præsterne: Naar I har fastet og klaget i den femte og syvende Maaned i halvfjerdsindstyve Aar, var det da mig, I fastede for?
6 Ndipo pamene munkadya ndi kumwa, kodi simunkachita zimenezi podzisangalatsa nokha?
Og naar I spiser og drikker, er det da ikke eder, som spiser og drikker?
7 Kodi awa si mawu amene Yehova ankanena kudzera mwa aneneri oyamba aja pamene Yerusalemu ndi mizinda yake yozungulira anali pa mtendere ndi pa ulemerero, ndi pamene Negevi ndi ku madera akumadzulo a mʼmbali mwa phiri munali anthu?’”
Kender I ikke de Ord, HERREN forkyndte ved de tidligere Profeter, dengang Jerusalem og dets Byer trindt om var beboet og havde Fred, og Sydlandet og Lavlandet var beboet?
8 Ndipo Yehova anayankhulanso ndi Zekariya kuti,
Og HERRENS Ord kom til Zakarias saaledes:
9 “Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Muziweruza molungama; muzichitirana chifundo ndi kumverana chisoni.
Saa siger Hærskarers HERRE: Fæld redelig Dom, vis Miskundhed og Barmhjertighed mod hverandre,
10 Musamazunze akazi amasiye kapena ana amasiye, alendo kapena osauka. Musamaganizirane zoyipa mʼmitima mwanu.’
undertryk ikke Enker og faderløse, fremmede og nødlidende og tænk ikke i eders Hjerter ondt mod hverandre!
11 “Koma makolo anu anakana kumvera uthenga umenewu; anawumitsa mtima nandifulatira, natseka makutu awo kuti asamve.
Men de vilde ikke høre; de var stivnakkede og gjorde deres Ører døve
12 Anawumitsa mitima yawo ngati mwala wa sangalabwi ndipo sanamvere lamulo kapena mawu amene Yehova Wamphamvuzonse anawatumiza mwa Mzimu wake kudzera mwa aneneri oyamba aja. Kotero Yehova Wamphamvuzonse anakwiya kwambiri.
og deres Hjerter haarde som Diamant for ikke at høre Loven og de Ord, Hærskarers HERRE sendte gennem sin Aand ved de tidligere Profeter. Derfor kom der stor Vrede fra Hærskarers HERRE.
13 “‘Pamene ndinawayitana, iwo sanamvere; choncho pamene iwo anandiyitana, Ine sindinamverenso,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Ligesom de ikke hørte, naar han kaldte, saaledes vil jeg, sagde Hærskarers HERRE, ikke høre, naar de kalder;
14 ‘Ndinawamwaza ndi kamvuluvulu pakati pa mitundu yonse ya anthu, kumene anali alendo. Dziko lawo linatsala litasakazidwa kwambiri kotero kuti palibe amene amabwera kapena kupitamo. Umu ndi mmene anasandutsira dziko labwino kukhala chipululu.’”
og jeg blæste dem bort blandt alle de Folk, de ikke kendte, og Landet blev øde efter dem, saa ingen drog ud eller hjem; og de gjorde det yndige Land til en Ørk.

< Zekariya 7 >