< Zekariya 6 >
1 Ndinayangʼananso ndipo taonani ndinaona magaleta anayi akutuluka pakati pa mapiri awiri, mapiri amkuwa.
Potom opet podigoh oèi svoje, i vidjeh, a to èetvora kola izlažahu izmeðu dvije gore, a te gore bijahu od mjedi.
2 Galeta loyamba limakokedwa ndi akavalo ofiira, lachiwiri ndi akavalo akuda,
U prvijem kolima bjehu konji riði, a u drugim kolima konji vrani,
3 lachitatu ndi akavalo oyera, ndipo lachinayi ndi akavalo otuwa a mawanga ofiirira, onsewa anali akavalo amphamvu kwambiri.
A u treæim kolima konji bijeli, a u èetvrtijem kolima konji šareni, jaki.
4 Ndinafunsa mngelo amene amayankhula nane uja kuti, “Kodi mbuye wanga chimenechi nʼchiyani?”
I progovoriv rekoh anðelu koji govoraše sa mnom: šta je to, gospodaru moj?
5 Mngeloyo anandiyankha kuti, “Imeneyi ndi mizimu inayi yakumwamba, imene ikuchokera pamaso pa Ambuye wa dziko lonse.
A anðeo odgovori i reèe mi: to su èetiri vjetra nebeska, koji izlaze ispred Gospoda sve zemlje, gdje stajaše.
6 Galeta la akavalo akuda likupita ku dziko la kumpoto, galeta la akavalo oyera likutsatira, ndipo galeta la akavalo amawanga ofiirira likupita ku dziko la kummwera.”
Konji vrani što su u jednijem, oni idu u sjevernu zemlju; a bijeli idu za njima; a šareni idu u zemlju južnu.
7 Pamene akavalo amphamvuwa ankapita, anali ndi changu chofuna kuyendera dziko lapansi. Ndipo iye anati, “Pitani, kayendereni dziko lapansi!”
I jaki izašavši šæahu da idu i prolaze zemlju; i reèe: idite, prolazite zemlju. I stadoše prolaziti zemlju.
8 Pamenepo anandiyitana, “Taona, akavalo amene apita ku dziko la kumpoto apumulitsa Mzimu wanga kumeneko.”
Tada me zovnu, i reèe mi: vidi, koji otidoše u zemlju sjevernu, umiriše duh moj u zemlji sjevernoj.
9 Yehova anayankhula nane kuti,
Potom mi doðe rijeè Gospodnja govoreæi:
10 “Landira mphatso kuchokera kwa anthu amene abwera ku ukapolo, Helidai, Tobiya ndi Yedaya, amene achokera ku Babuloni. Tsiku lomwelo pita ku nyumba ya Yosiya mwana wa Zefaniya.
Uzmi od roblja, od Heldaja i od Tovije i od Jedaje, koji doðoše iz Vavilonske, pa doði istoga dana i uði u dom Josije sina Sofonijina.
11 Tenga siliva ndi golide upange chipewa chaufumu, ndipo uchiyike pamutu pa mkulu wa ansembe, Yoswa mwana wa Yehozadaki.
Uzmi srebra i zlata, i naèini vijence, i metni na glavu Isusu sinu Josedekovu, poglavaru sveštenièkom,
12 Muwuze kuti zimene akunena Yehova Wamphamvuzonse ndi izi: ‘Taonani, munthu wotchedwa Nthambi ndi ameneyu, ndipo adzaphuka pomwe alipo ndi kumanga Nyumba ya Yehova.
I reci mu govoreæi: ovako veli Gospod nad vojskama: evo èovjeka, kojemu je ime klica, koja æe klijati s mjesta svoga i sagradiæe crkvu Gospodnju.
13 Ndiye amene adzamange Nyumba ya Yehova, adzalandira ulemerero waufumu ndipo adzalamulira pa mpando wake waufumu. Adzakhalanso wansembe pa mpando wake waufumu. Ndipo padzakhala mtendere.’
Jer æe on sagraditi crkvu Gospodnju, i nosiæe slavu, i sjedjeæe i vladati na svom prijestolu, i biæe sveštenik na prijestolu svom, i svjet mirni biæe meðu objema.
14 Chipewa cha ufumucho adzachipereka kwa Helemu, Tobiya, Yedaya, ndi kwa Heni mwana wa Zefaniya, kuti chikhale chikumbutso mʼNyumba ya Yehova.
I vijenci neka budu Elemu i Toviji i Jedaji i Henu sinu Sofonijinu za spomen u crkvi Gospodnjoj.
15 Anthu okhala kutali adzabwera kudzathandiza kumanga Nyumba ya Yehova, ndipo iwe udzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse wandituma kwa iwe. Zimenezi zidzachitika ngati mudzamvera mwachangu Yehova Mulungu wanu.”
I koji su daleko, doæi æe i gradiæe crkvu Gospodnju, i poznaæete da me je Gospod nad vojskama poslao k vama. I to æe biti ako uzaslušate glas Gospoda Boga svojega.