< Zekariya 6 >
1 Ndinayangʼananso ndipo taonani ndinaona magaleta anayi akutuluka pakati pa mapiri awiri, mapiri amkuwa.
Potem obróciwszy się podniosłem oczu swych i ujrzałem, a oto cztery wozy wychodziły z pośrodku dwóch gór, a góry one były góry miedziane.
2 Galeta loyamba limakokedwa ndi akavalo ofiira, lachiwiri ndi akavalo akuda,
W pierwszym wozie były konie rydze, a w drugim wozie konie wrone (kare):
3 lachitatu ndi akavalo oyera, ndipo lachinayi ndi akavalo otuwa a mawanga ofiirira, onsewa anali akavalo amphamvu kwambiri.
W trzecim wozie konie białe, a w czwartym wozie były konie strokate, a wszystkie mocne.
4 Ndinafunsa mngelo amene amayankhula nane uja kuti, “Kodi mbuye wanga chimenechi nʼchiyani?”
Tedy odpowiadając rzekłem do Anioła, który mówił zemną: Co to jest, Panie mój?
5 Mngeloyo anandiyankha kuti, “Imeneyi ndi mizimu inayi yakumwamba, imene ikuchokera pamaso pa Ambuye wa dziko lonse.
I odpowiedział Anioł a rzekł do mnie: Te są cztery wiatry niebieskie, wychodzące z miejsca, gdzie stały, przed panującym nad wszystką ziemią.
6 Galeta la akavalo akuda likupita ku dziko la kumpoto, galeta la akavalo oyera likutsatira, ndipo galeta la akavalo amawanga ofiirira likupita ku dziko la kummwera.”
Konie wrone zaprzężone wychodzą do ziemi północnej, a białe wychodzą za nimi, strokate zaś wychodzą do ziemi południowej.
7 Pamene akavalo amphamvuwa ankapita, anali ndi changu chofuna kuyendera dziko lapansi. Ndipo iye anati, “Pitani, kayendereni dziko lapansi!”
Te tedy mocne konie wyszedłszy chciały iść, aby obeszły ziemię; tedy rzekł: Idźcie, a obejdźcie ziemię! I obeszły ziemię.
8 Pamenepo anandiyitana, “Taona, akavalo amene apita ku dziko la kumpoto apumulitsa Mzimu wanga kumeneko.”
A zawoławszy mię rzekł do mnie, mówiąc: Oto te, które wyszły do ziemi północnej, uspokoiły ducha mego w ziemi północnej.
9 Yehova anayankhula nane kuti,
I stało się słowo Pańskie do mnie, mówiąc:
10 “Landira mphatso kuchokera kwa anthu amene abwera ku ukapolo, Helidai, Tobiya ndi Yedaya, amene achokera ku Babuloni. Tsiku lomwelo pita ku nyumba ya Yosiya mwana wa Zefaniya.
Weźmij od tych, co byli pojmani od Cheldajego i od Tobijasza, i od Jedajasza; (a ty przyjdziesz tegoż dnia, i wnijdziesz do domu Josyjasza, syna Sofonijaszowego) którzy idą z Babilonu;
11 Tenga siliva ndi golide upange chipewa chaufumu, ndipo uchiyike pamutu pa mkulu wa ansembe, Yoswa mwana wa Yehozadaki.
Weźmij, mówię, srebro i złoto, a uczyń korony, a włóż je na głowę Jesuego, syna Jozedekowego, kapłana najwyższego.
12 Muwuze kuti zimene akunena Yehova Wamphamvuzonse ndi izi: ‘Taonani, munthu wotchedwa Nthambi ndi ameneyu, ndipo adzaphuka pomwe alipo ndi kumanga Nyumba ya Yehova.
I rzecz do niego, mówiąc: Tak powiada Pan zastępów, mówiąc: Oto mąż, którego imię jest Latorośl, który z miejsca swego wyrośnie, ten wystawi kościół Panu.
13 Ndiye amene adzamange Nyumba ya Yehova, adzalandira ulemerero waufumu ndipo adzalamulira pa mpando wake waufumu. Adzakhalanso wansembe pa mpando wake waufumu. Ndipo padzakhala mtendere.’
Bo ten ma wystawić kościół Panu, ten zaś przyniesie sławę, i siedzieć i panować będzie na stolicy swojej, i będzie kapłanem na stolicy swojej, a rada pokoju będzie między nimi obiema.
14 Chipewa cha ufumucho adzachipereka kwa Helemu, Tobiya, Yedaya, ndi kwa Heni mwana wa Zefaniya, kuti chikhale chikumbutso mʼNyumba ya Yehova.
A te korony zostaną Chelemowi, i Tobijaszowi, i Jedajaszowi, i Chenowi, synowi Sofonijaszowemu, na pamiątkę w kościele Pańskim.
15 Anthu okhala kutali adzabwera kudzathandiza kumanga Nyumba ya Yehova, ndipo iwe udzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse wandituma kwa iwe. Zimenezi zidzachitika ngati mudzamvera mwachangu Yehova Mulungu wanu.”
Bo dalecy przyjdą, a będą budować kościół Pański; i dowiecie się, że Pan zastępów posłał mię do was; a to się stanie, jeźli pilnie słuchać będziecie głosu Pana, Boga swego.