< Zekariya 6 >

1 Ndinayangʼananso ndipo taonani ndinaona magaleta anayi akutuluka pakati pa mapiri awiri, mapiri amkuwa.
Ngasengibuya ngaphakamisa amehlo ami, ngabona, khangela-ke, kwaphuma inqola ezine phakathi kwezintaba ezimbili; lezintaba zazizintaba zethusi.
2 Galeta loyamba limakokedwa ndi akavalo ofiira, lachiwiri ndi akavalo akuda,
Enqoleni yokuqala kwakulamabhiza abomvu, lenqoleni yesibili amabhiza amnyama,
3 lachitatu ndi akavalo oyera, ndipo lachinayi ndi akavalo otuwa a mawanga ofiirira, onsewa anali akavalo amphamvu kwambiri.
lenqoleni yesithathu amabhiza amhlophe, lenqoleni yesine amabhiza alamabala alamandla.
4 Ndinafunsa mngelo amene amayankhula nane uja kuti, “Kodi mbuye wanga chimenechi nʼchiyani?”
Ngasengiphendula ngathi kuyo ingilosi eyayikhuluma lami: Ayini lawo, nkosi yami?
5 Mngeloyo anandiyankha kuti, “Imeneyi ndi mizimu inayi yakumwamba, imene ikuchokera pamaso pa Ambuye wa dziko lonse.
Ingilosi yasiphendula yathi kimi: Lawo ayimimoya emine yamazulu, ephuma ekumeni phambi kweNkosi yomhlaba wonke.
6 Galeta la akavalo akuda likupita ku dziko la kumpoto, galeta la akavalo oyera likutsatira, ndipo galeta la akavalo amawanga ofiirira likupita ku dziko la kummwera.”
Amabhiza amnyama akhonapho aphuma esiya elizweni lenyakatho; lamhlophe aphuma ewalandela; lalamabala aphuma esiya elizweni leningizimu.
7 Pamene akavalo amphamvuwa ankapita, anali ndi changu chofuna kuyendera dziko lapansi. Ndipo iye anati, “Pitani, kayendereni dziko lapansi!”
Alamandla asephuma, adinga ukuhamba ukuze aye le lale emhlabeni. Yasisithi: Hambani liye le lale emhlabeni. Asesiya le lale emhlabeni.
8 Pamenepo anandiyitana, “Taona, akavalo amene apita ku dziko la kumpoto apumulitsa Mzimu wanga kumeneko.”
Yasingimemeza, yakhuluma kimi, isithi: Khangela, la aphuma aya elizweni lenyakatho awuphumuzile umoya wami elizweni lenyakatho.
9 Yehova anayankhula nane kuti,
Ilizwi leNkosi laselifika kimi lisithi:
10 “Landira mphatso kuchokera kwa anthu amene abwera ku ukapolo, Helidai, Tobiya ndi Yedaya, amene achokera ku Babuloni. Tsiku lomwelo pita ku nyumba ya Yosiya mwana wa Zefaniya.
Thatha kwabathunjiweyo, kuHelidayi, lakuTobiya, lakuJedaya, abavele eBhabhiloni, ubuye wena ngalolosuku, uye endlini kaJosiya indodana kaZefaniya,
11 Tenga siliva ndi golide upange chipewa chaufumu, ndipo uchiyike pamutu pa mkulu wa ansembe, Yoswa mwana wa Yehozadaki.
ubusuthatha isiliva legolide, wenze imiqhele, uyibeke phezu kwekhanda likaJoshuwa indodana kaJehozadaki, umpristi omkhulu;
12 Muwuze kuti zimene akunena Yehova Wamphamvuzonse ndi izi: ‘Taonani, munthu wotchedwa Nthambi ndi ameneyu, ndipo adzaphuka pomwe alipo ndi kumanga Nyumba ya Yehova.
ubusukhuluma kuye, usithi: Itsho njalo iNkosi yamabandla, isithi: Khangela, umuntu obizo lakhe nguHlumela, uzahluma-ke ephuma endaweni yakhe, akhe ithempeli leNkosi.
13 Ndiye amene adzamange Nyumba ya Yehova, adzalandira ulemerero waufumu ndipo adzalamulira pa mpando wake waufumu. Adzakhalanso wansembe pa mpando wake waufumu. Ndipo padzakhala mtendere.’
Yena-ke uzakwakha ithempeli leNkosi; yena athwale ubukhosi, ahlale abuse phezu kwesihlalo sakhe sobukhosi. Futhi uzakuba ngumpristi phezu kwesihlalo sakhe sobukhosi; leseluleko sokuthula sizakuba phakathi kwabo bobabili.
14 Chipewa cha ufumucho adzachipereka kwa Helemu, Tobiya, Yedaya, ndi kwa Heni mwana wa Zefaniya, kuti chikhale chikumbutso mʼNyumba ya Yehova.
Lemiqhele izakuba kuHelemi, lakuThobhiya, lakuJedaya, lakuHeni indodana kaZefaniya, kube yisikhumbuzo ethempelini leNkosi.
15 Anthu okhala kutali adzabwera kudzathandiza kumanga Nyumba ya Yehova, ndipo iwe udzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse wandituma kwa iwe. Zimenezi zidzachitika ngati mudzamvera mwachangu Yehova Mulungu wanu.”
Labakhatshana bazafika bakhe ethempelini leNkosi, beselisazi ukuthi iNkosi yamabandla ingithumile kini. Lokhu kuzakwenzeka, uba lilalela lokulalela ilizwi leNkosi uNkulunkulu wenu.

< Zekariya 6 >