< Zekariya 6 >
1 Ndinayangʼananso ndipo taonani ndinaona magaleta anayi akutuluka pakati pa mapiri awiri, mapiri amkuwa.
Ngaphinde ngaphakamisa amehlo njalo phambi kwami kwakulezinqola zempi ezine ziqhamuka okhalweni lwezintaba ezimbili, izintaba zethusi!
2 Galeta loyamba limakokedwa ndi akavalo ofiira, lachiwiri ndi akavalo akuda,
Inqola yakuqala yayilamabhiza abomvu, eyesibili ilamnyama,
3 lachitatu ndi akavalo oyera, ndipo lachinayi ndi akavalo otuwa a mawanga ofiirira, onsewa anali akavalo amphamvu kwambiri.
eyesithathu amhlophe, eyesine alamabala, wonke elamandla.
4 Ndinafunsa mngelo amene amayankhula nane uja kuti, “Kodi mbuye wanga chimenechi nʼchiyani?”
Ngayibuza ingilosi eyayikhuluma lami ngathi, “Kuyini lokhu, nkosi yami?”
5 Mngeloyo anandiyankha kuti, “Imeneyi ndi mizimu inayi yakumwamba, imene ikuchokera pamaso pa Ambuye wa dziko lonse.
Ingilosi yangiphendula yathi, “Le yimimoya emine yasezulwini, ephumayo ekumeni phambi kukaThixo womhlaba wonke.
6 Galeta la akavalo akuda likupita ku dziko la kumpoto, galeta la akavalo oyera likutsatira, ndipo galeta la akavalo amawanga ofiirira likupita ku dziko la kummwera.”
Le elamabhiza amnyama iqonda elizweni elisenyakatho, eyawamhlophe iqonda entshonalanga, kuthi eyawamabala iqonda eningizimu.”
7 Pamene akavalo amphamvuwa ankapita, anali ndi changu chofuna kuyendera dziko lapansi. Ndipo iye anati, “Pitani, kayendereni dziko lapansi!”
Kwathi lawomabhiza alamandla esephuma ayesadalala ezama ukuya kuwo wonke umhlaba. Yathi kuwo, “Hambani kuwo wonke umhlaba.” Lakanye aya kuwo wonke umhlaba.
8 Pamenepo anandiyitana, “Taona, akavalo amene apita ku dziko la kumpoto apumulitsa Mzimu wanga kumeneko.”
Yase ingibiza yathi, “Uyabona, lawana aqonda elizweni elisenyakatho asenike uMoya wami ukuphumula elizweni lasenyakatho.”
9 Yehova anayankhula nane kuti,
Ilizwi likaThixo lafika kimi lathi:
10 “Landira mphatso kuchokera kwa anthu amene abwera ku ukapolo, Helidai, Tobiya ndi Yedaya, amene achokera ku Babuloni. Tsiku lomwelo pita ku nyumba ya Yosiya mwana wa Zefaniya.
“Thatha isiliva legolide kwabathunjiweyo uHelidayi loThobhiya loJedaya asebebuyile eBhabhiloni. Hamba ngalelolanga endlini kaJosiya indodana kaZefaniya.
11 Tenga siliva ndi golide upange chipewa chaufumu, ndipo uchiyike pamutu pa mkulu wa ansembe, Yoswa mwana wa Yehozadaki.
Thatha isiliva legolide wenze umqhele uwethese umphristi omkhulu uJoshuwa indodana kaJozadaki.
12 Muwuze kuti zimene akunena Yehova Wamphamvuzonse ndi izi: ‘Taonani, munthu wotchedwa Nthambi ndi ameneyu, ndipo adzaphuka pomwe alipo ndi kumanga Nyumba ya Yehova.
Umtshele ukuthi nanku okutshiwo nguThixo uSomandla, uthi: ‘Nansi indoda obizo layo liHlumela, njalo uzahluma endaweni yakhe akhe ithempeli likaThixo.
13 Ndiye amene adzamange Nyumba ya Yehova, adzalandira ulemerero waufumu ndipo adzalamulira pa mpando wake waufumu. Adzakhalanso wansembe pa mpando wake waufumu. Ndipo padzakhala mtendere.’
Nguye ozakwakha ithempeli likaThixo, njalo uzagqokiswa ubukhosi, futhi uzahlala esihlalweni sakhe sobukhosi. Njalo uzakuba ngumphristi esihlalweni sakhe sobukhosi. Lokhu kokubili kuzahambelana kuhle.’
14 Chipewa cha ufumucho adzachipereka kwa Helemu, Tobiya, Yedaya, ndi kwa Heni mwana wa Zefaniya, kuti chikhale chikumbutso mʼNyumba ya Yehova.
Umqhele uzaphiwa uHelidayi, loThobhiya, loJedaya kanye loHeni indodana kaZefaniya njengesikhumbuzo ethempelini likaThixo.
15 Anthu okhala kutali adzabwera kudzathandiza kumanga Nyumba ya Yehova, ndipo iwe udzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse wandituma kwa iwe. Zimenezi zidzachitika ngati mudzamvera mwachangu Yehova Mulungu wanu.”
Labo abasekudeni bazakuza bazakwelekelela ukwakha ithempeli likaThixo njalo lizakwazi ukuthi uthixo uSomandla ungithumile kini. Lokhu kuzakwenzeka nxa limlalela ngokukhuthala uThixo uNkulunkulu wenu.”