< Zekariya 6 >

1 Ndinayangʼananso ndipo taonani ndinaona magaleta anayi akutuluka pakati pa mapiri awiri, mapiri amkuwa.
And once again I lifted mine eyes, and looked, and lo! four chariots, coming forward from between two mountains, —now, the mountains, were mountains of copper.
2 Galeta loyamba limakokedwa ndi akavalo ofiira, lachiwiri ndi akavalo akuda,
In the first chariot, were red horses, —and, in the second chariot, black horses;
3 lachitatu ndi akavalo oyera, ndipo lachinayi ndi akavalo otuwa a mawanga ofiirira, onsewa anali akavalo amphamvu kwambiri.
and, in the third chariot, white horses, —and, in the fourth chariot, horses spotted, deep red.
4 Ndinafunsa mngelo amene amayankhula nane uja kuti, “Kodi mbuye wanga chimenechi nʼchiyani?”
Then began I, and said, unto the messenger who was speaking with me, —What are these, my lord?
5 Mngeloyo anandiyankha kuti, “Imeneyi ndi mizimu inayi yakumwamba, imene ikuchokera pamaso pa Ambuye wa dziko lonse.
And the messenger answered, and said unto me, —These, are the four winds of the heavens, coming forward after each hath presented itself near the Lord of all the earth.
6 Galeta la akavalo akuda likupita ku dziko la kumpoto, galeta la akavalo oyera likutsatira, ndipo galeta la akavalo amawanga ofiirira likupita ku dziko la kummwera.”
They in whose chariot are the black horses, are going forth into the land of the North, and, the white, have gone forth after them, —and, the spotted, have gone forth into the land of the South;
7 Pamene akavalo amphamvuwa ankapita, anali ndi changu chofuna kuyendera dziko lapansi. Ndipo iye anati, “Pitani, kayendereni dziko lapansi!”
and, the deep red, have come forward and sought to go their way, that they might journey to and fro in the land, so he said, Go your way, journey to and fro in the land, —and they journeyed to and fro in the land.
8 Pamenepo anandiyitana, “Taona, akavalo amene apita ku dziko la kumpoto apumulitsa Mzimu wanga kumeneko.”
Then made he outcry beside me, and spake unto me, saying, —See, these who are going forth into the land of the North, have settled my spirit in the land of the North.
9 Yehova anayankhula nane kuti,
Then came the word of Yahweh unto me, saying:
10 “Landira mphatso kuchokera kwa anthu amene abwera ku ukapolo, Helidai, Tobiya ndi Yedaya, amene achokera ku Babuloni. Tsiku lomwelo pita ku nyumba ya Yosiya mwana wa Zefaniya.
Take of them of the exile, of Heldai, and of Tobijah, and of Jedaiah, —then shalt, thou thyself, enter, on that day, yea thou shalt enter the house of Josiah son of Zephaniah, [with them] who have come in out of Babylon;
11 Tenga siliva ndi golide upange chipewa chaufumu, ndipo uchiyike pamutu pa mkulu wa ansembe, Yoswa mwana wa Yehozadaki.
yea thou shalt take silver and gold, and make a crown, —and set [it] upon the head of Jehoshua son of Jehozadak, the high priest;
12 Muwuze kuti zimene akunena Yehova Wamphamvuzonse ndi izi: ‘Taonani, munthu wotchedwa Nthambi ndi ameneyu, ndipo adzaphuka pomwe alipo ndi kumanga Nyumba ya Yehova.
then shalt thou speak unto him, saying, Thus, speaketh Yahweh of hosts, saying, —Lo! a man! Bud, is his name, and, out of his own place, shall he bud forth, and shall build the temple of Yahweh;
13 Ndiye amene adzamange Nyumba ya Yehova, adzalandira ulemerero waufumu ndipo adzalamulira pa mpando wake waufumu. Adzakhalanso wansembe pa mpando wake waufumu. Ndipo padzakhala mtendere.’
Yea, he, shall build the temple of Yahweh, and, he, shall bear the honour, and shall sit and rule upon his throne, —and shall become a priest upon his throne, and, the counsel of peace, shall be between the two of them.
14 Chipewa cha ufumucho adzachipereka kwa Helemu, Tobiya, Yedaya, ndi kwa Heni mwana wa Zefaniya, kuti chikhale chikumbutso mʼNyumba ya Yehova.
But, the crown, shall belong to Heldai and to Tobiah and to Jedaiah, and to Hen son of Zephaniah, —for a memorial in the temple of Yahweh.
15 Anthu okhala kutali adzabwera kudzathandiza kumanga Nyumba ya Yehova, ndipo iwe udzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse wandituma kwa iwe. Zimenezi zidzachitika ngati mudzamvera mwachangu Yehova Mulungu wanu.”
And, they who are afar off, shall come in and shall build at the temple of Yahweh, so shall yea know that, Yahweh of hosts, hath sent me unto you, —and it shall come to pass if ye will, indeed hearken, unto the voice of Yahweh your God.

< Zekariya 6 >