< Zekariya 6 >
1 Ndinayangʼananso ndipo taonani ndinaona magaleta anayi akutuluka pakati pa mapiri awiri, mapiri amkuwa.
And again I lifted up mine eyes, and saw, and, behold, there came four chariots out from between the two mountains; and the mountains were mountains of brass.
2 Galeta loyamba limakokedwa ndi akavalo ofiira, lachiwiri ndi akavalo akuda,
In the first chariot were red horses; and in the second chariot black horses;
3 lachitatu ndi akavalo oyera, ndipo lachinayi ndi akavalo otuwa a mawanga ofiirira, onsewa anali akavalo amphamvu kwambiri.
and in the third chariot white horses; and in the fourth chariot grizzled bay horses.
4 Ndinafunsa mngelo amene amayankhula nane uja kuti, “Kodi mbuye wanga chimenechi nʼchiyani?”
Then I answered and said unto the angel that spoke with me: 'What are these, my lord?'
5 Mngeloyo anandiyankha kuti, “Imeneyi ndi mizimu inayi yakumwamba, imene ikuchokera pamaso pa Ambuye wa dziko lonse.
And the angel answered and said unto me: 'These chariots go forth to the four winds of heaven, after presenting themselves before the Lord of all the earth.
6 Galeta la akavalo akuda likupita ku dziko la kumpoto, galeta la akavalo oyera likutsatira, ndipo galeta la akavalo amawanga ofiirira likupita ku dziko la kummwera.”
That wherein are the black horses goeth forth toward the north country; and the white went forth after them; and the grizzled went forth toward the south country;
7 Pamene akavalo amphamvuwa ankapita, anali ndi changu chofuna kuyendera dziko lapansi. Ndipo iye anati, “Pitani, kayendereni dziko lapansi!”
and the bay went forth'. And they sought to go that they might walk to and fro through the earth; and he said: 'Get you hence, walk to and fro through the earth.' So they walked to and fro through the earth.
8 Pamenepo anandiyitana, “Taona, akavalo amene apita ku dziko la kumpoto apumulitsa Mzimu wanga kumeneko.”
Then cried he upon me, and spoke unto me, saying: 'Behold, they that go toward the north country have eased My spirit in the north country.'
9 Yehova anayankhula nane kuti,
And the word of the LORD came unto me, saying:
10 “Landira mphatso kuchokera kwa anthu amene abwera ku ukapolo, Helidai, Tobiya ndi Yedaya, amene achokera ku Babuloni. Tsiku lomwelo pita ku nyumba ya Yosiya mwana wa Zefaniya.
'Take of them of the captivity, even of Heldai, of Tobijah, and of Jedaiah, that are come from Babylon; and come thou the same day, and go into the house of Josiah the son of Zephaniah;
11 Tenga siliva ndi golide upange chipewa chaufumu, ndipo uchiyike pamutu pa mkulu wa ansembe, Yoswa mwana wa Yehozadaki.
yea, take silver and gold, and make crowns, and set the one upon the head of Joshua the son of Jehozadak, the high priest;
12 Muwuze kuti zimene akunena Yehova Wamphamvuzonse ndi izi: ‘Taonani, munthu wotchedwa Nthambi ndi ameneyu, ndipo adzaphuka pomwe alipo ndi kumanga Nyumba ya Yehova.
and speak unto him, saying: Thus speaketh the LORD of hosts, saying: Behold, a man whose name is the Shoot, and who shall shoot up out of his place, and build the temple of the LORD;
13 Ndiye amene adzamange Nyumba ya Yehova, adzalandira ulemerero waufumu ndipo adzalamulira pa mpando wake waufumu. Adzakhalanso wansembe pa mpando wake waufumu. Ndipo padzakhala mtendere.’
even he shall build the temple of the LORD; and he shall bear the glory, and shall sit and rule upon his throne; and there shall be a priest before his throne; and the counsel of peace shall be between them both.
14 Chipewa cha ufumucho adzachipereka kwa Helemu, Tobiya, Yedaya, ndi kwa Heni mwana wa Zefaniya, kuti chikhale chikumbutso mʼNyumba ya Yehova.
And the crowns shall be to Helem, and to Tobijah, and to Jedaiah, and to Hen the son of Zephaniah, as a memorial in the temple of the LORD.
15 Anthu okhala kutali adzabwera kudzathandiza kumanga Nyumba ya Yehova, ndipo iwe udzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse wandituma kwa iwe. Zimenezi zidzachitika ngati mudzamvera mwachangu Yehova Mulungu wanu.”
And they that are far off shall come and build in the temple of the LORD, and ye shall know that the LORD of hosts hath sent me unto you. And it shall come to pass, if ye will diligently hearken to the voice of the LORD your God —.'