< Zekariya 5 >

1 Ndinayangʼananso ndipo taonani ndinaona chikalata chimene chimawuluka.
Andin mǝn yǝnǝ beximni kɵtürüp, mana bir uqar oram yazmini kɵrdüm.
2 Mngelo uja anandifunsa kuti, “Kodi ukuona chiyani?” Ndinayankha kuti, “Ndikuona chikalata chikuwuluka, mulitali mwake mamita asanu ndi anayi ndipo mulifupi mwake mamita anayi ndi theka.”
U mǝndin: «Nemini kɵrdüng?» dǝp soridi. Mǝn: «Bir uqar oram yazmini kɵrdüm; uzunluⱪi yigirmǝ gǝz, kǝngliki on gǝz ikǝn» — dedim.
3 Ndipo mngeloyo anandiwuza kuti, “Awa ndi matemberero amene akupita pa dziko lonse lapansi; potsata zimene zalembedwa mʼkati mwa chikalatamo, aliyense wakuba adzachotsedwa, ndipo potsata zomwe zalembedwa kunja kwake, aliyense wolumbira zabodza adzachotsedwanso.
U manga: «Bu bolsa pütün zemin üstigǝ qiⱪirilƣan lǝnǝttur; qünki ⱨǝrbir oƣriliⱪ ⱪilƣuqi bu tǝripigǝ yezilƣini boyiqǝ üzüp taxlinidu; wǝ ⱪǝsǝm iqküqilǝrning ⱨǝrbiri u tǝripigǝ yezilƣini boyiqǝ üzüp taxlinidu».
4 Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti, ‘Temberero limeneli ndidzalitumiza, ndipo lidzalowa mʼnyumba ya munthu wakuba ndi munthu wolumbira zabodza mʼdzina langa. Lidzakhala mʼnyumbamo mpaka kuyiwonongeratu, matabwa ake ndi miyala yake yomwe.’”
— «Mǝn bu [yazmini] qiⱪirimǝn» — dǝydu samawi ⱪoxunlarning Sǝrdari bolƣan Pǝrwǝrdigar, «wǝ u oƣrining ɵyigǝ ⱨǝmdǝ namim bilǝn yalƣandin ⱪǝsǝm iqküqining ɵyigǝ kiridu wǝ xu ɵydǝ ⱪonup uni yaƣaq-taxliri bilǝn ⱪoxupla yǝwetidu».
5 Kenaka mngelo amene amayankhula nane uja anabwera patsogolo panga ndipo anandiwuza kuti, “Kweza maso ako tsopano kuti uwone kuti ndi chiyani chikubwerachi.”
Andin mǝn bilǝn sɵzlixiwatⱪan pǝrixtǝ qiⱪip manga: «Əmdi bexingni kɵtürgin, nemining qiⱪiwatⱪinini kɵrüp baⱪ» — dedi.
6 Ndinafunsa kuti, “Kodi chimenechi nʼchiyani?” Mngeloyo anayankha kuti, “Limeneli ndi dengu loyezera.” Ndipo anawonjezera kunena kuti, “Umenewu ndi uchimo wa anthu mʼdziko lonse.”
Mǝn: «U nemǝ?» — dǝp soridim. U manga: «Bu qiⱪiwatⱪan «ǝfaⱨ» sewitidur», wǝ: «Bu bolsa [xu rǝzillǝrning] pütün zemindiki ⱪiyapitidur» — dedi.
7 Pamenepo chovundikira chake chamtovu chinatukulidwa, ndipo mʼdengumo munali mutakhala mkazi.
Əfaⱨ sewitining aƣzidin dumilaⱪ bir ⱪoƣuxun kɵtürüldi, mana, ǝfaⱨ sewiti iqidǝ bir ayal olturatti.
8 Mngeloyo anati, “Chimenechi ndi choyipa,” ndipo anamukankhira mkaziyo mʼdengu muja, nabwezera chovundikira chamtovu chija pamwamba pake.
U: «Bu bolsa, rǝzillik»tur» — dǝp, uni ǝfaⱨ sewiti iqigǝ ⱪayturup taxlap, ǝfaⱨning aƣziƣa eƣir ⱪoƣuxunni taxlap ⱪoydi.
9 Kenaka ndinayangʼananso, ndipo ndinaona akazi awiri akuwuluka kubwera kumene kunali ine; akuwuluzika ndi mphepo. Iwo anali ndi mapiko ngati a kakowa, ndipo ananyamula dengu lija, kupita nalo pakati pa mlengalenga ndi dziko lapansi.
Beximni kɵtürüp, mana ikki ayalning qiⱪⱪanliⱪini kɵrdüm; xamal ularning ⱪanatlirini yǝlpütüp turatti (ularning lǝylǝkningkidǝk ⱪanatliri bar idi); ular ǝfaⱨni asman bilǝn zeminning otturisiƣa kɵtürdi.
10 Ine ndinafunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Dengulo akupita nalo kuti?”
Mǝn bilǝn sɵzlixiwatⱪan pǝrixtidin: «Ular ǝfaⱨni nǝgǝ kɵtürüp mangidu?» — dǝp soridim.
11 Iye anayankha kuti, “Ku dziko la Babuloni kuti akalimangire nyumba. Nyumbayo ikadzatha, adzayikamo dengulo.”
U manga: Ular ǝfaⱨ üqün «Xinar zemini»da bir ɵy selixⱪa kǝtti; ɵy bǝrpa ⱪilinƣandin keyin, ǝfaⱨ sewiti xu yǝrdǝ ɵz turalƣusiƣa ⱪoyulidu, — dǝp jawab bǝrdi.

< Zekariya 5 >