< Zekariya 5 >

1 Ndinayangʼananso ndipo taonani ndinaona chikalata chimene chimawuluka.
A LAWA hou ae la ko'u mau maka iluna, ike aku la au, aia hoi, he owili pepa e lele ana.
2 Mngelo uja anandifunsa kuti, “Kodi ukuona chiyani?” Ndinayankha kuti, “Ndikuona chikalata chikuwuluka, mulitali mwake mamita asanu ndi anayi ndipo mulifupi mwake mamita anayi ndi theka.”
I mai la kela ia'u, Heaha kau mea ike? I aku la au, Ke ike aku nei au i ka owili pepa lele ana; he iwakalua hailima ka loa, a he umi hailima ka laula.
3 Ndipo mngeloyo anandiwuza kuti, “Awa ndi matemberero amene akupita pa dziko lonse lapansi; potsata zimene zalembedwa mʼkati mwa chikalatamo, aliyense wakuba adzachotsedwa, ndipo potsata zomwe zalembedwa kunja kwake, aliyense wolumbira zabodza adzachotsedwanso.
Olelo mai la kela ia'u, Eia ka hoahewa ana e hele aku maluna o ka ili a pau o ka honua. No ka mea, o kela mea keia mea aihue, e hookiia auanei oia ma keia aoao, e like me ka keia; a o kela mea keia mea e hoohiki wahahee ana, e hookiia'e oia ma kela aoao, e like me ka kela.
4 Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti, ‘Temberero limeneli ndidzalitumiza, ndipo lidzalowa mʼnyumba ya munthu wakuba ndi munthu wolumbira zabodza mʼdzina langa. Lidzakhala mʼnyumbamo mpaka kuyiwonongeratu, matabwa ake ndi miyala yake yomwe.’”
Ua lawe mai nei au in, wahi a Iehova o na kaua, a e komo aku ia iloko o ka hale o ka aihue, a o ka hale o ka mea e hoohiki wahahee ana ma ko'u inoa; e noho ia iloko o kona hale, a e hoopau oia ia mea me ka laau a me ka pohaku ona.
5 Kenaka mngelo amene amayankhula nane uja anabwera patsogolo panga ndipo anandiwuza kuti, “Kweza maso ako tsopano kuti uwone kuti ndi chiyani chikubwerachi.”
Alaila, hele aku la ka anela i kamailio pu me au, a i mai la ia'u, E nana ae oe iluna, a e ike i kela mea e hele aku ana.
6 Ndinafunsa kuti, “Kodi chimenechi nʼchiyani?” Mngeloyo anayankha kuti, “Limeneli ndi dengu loyezera.” Ndipo anawonjezera kunena kuti, “Umenewu ndi uchimo wa anthu mʼdziko lonse.”
I aku la au, Heaha ia mea? I mai la kela, He epa ia mea e hele aku ana. I mai la hoi oia, Eia ko lakou helehelena ma ka honua a pau.
7 Pamenepo chovundikira chake chamtovu chinatukulidwa, ndipo mʼdengumo munali mutakhala mkazi.
Aia hoi, ua kaikaiia'e he popo kepau; a o ka mea e noho ana iwaenakonu o ka epa, he wahine ia.
8 Mngeloyo anati, “Chimenechi ndi choyipa,” ndipo anamukankhira mkaziyo mʼdengu muja, nabwezera chovundikira chamtovu chija pamwamba pake.
I mai la kela, O keia ka aia. A hoolei aku la oia ia mea mawaena konu o ka epa; a hoolei iho la ia i ka pohaku kepau maluna iho o kona waha.
9 Kenaka ndinayangʼananso, ndipo ndinaona akazi awiri akuwuluka kubwera kumene kunali ine; akuwuluzika ndi mphepo. Iwo anali ndi mapiko ngati a kakowa, ndipo ananyamula dengu lija, kupita nalo pakati pa mlengalenga ndi dziko lapansi.
Alaila, nana ae la au iluna, ike aku la, aia hoi, puka mai la na wahine elua iwaho, a iloko o ko laua mau eheu ka makani; no ka mea, he mau eheu ia laua e like me na eheu o ka setoreka: a kaikai ae la lakou i ka epa iluna iwaena o ka honua a me ka lani.
10 Ine ndinafunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Dengulo akupita nalo kuti?”
Ninau aku la au i ka anela i kamailio me au, Mahea la laua nei e lawe aku ai i ka epa?
11 Iye anayankha kuti, “Ku dziko la Babuloni kuti akalimangire nyumba. Nyumbayo ikadzatha, adzayikamo dengulo.”
I mai la kela ia'u, No ka hana i hale nona ma ka aina i Sinara; ilaila ia e hoonohoia'i, a e kau ia maluna o kona kumu.

< Zekariya 5 >