< Zekariya 5 >

1 Ndinayangʼananso ndipo taonani ndinaona chikalata chimene chimawuluka.
Et de nouveau je levai les yeux et regardai, et voici un volume qui volait.
2 Mngelo uja anandifunsa kuti, “Kodi ukuona chiyani?” Ndinayankha kuti, “Ndikuona chikalata chikuwuluka, mulitali mwake mamita asanu ndi anayi ndipo mulifupi mwake mamita anayi ndi theka.”
Et il me dit: Que vois-tu? Et je dis: Je vois un volume qui vole; sa longueur est de vingt coudées, et sa largeur de dix coudées.
3 Ndipo mngeloyo anandiwuza kuti, “Awa ndi matemberero amene akupita pa dziko lonse lapansi; potsata zimene zalembedwa mʼkati mwa chikalatamo, aliyense wakuba adzachotsedwa, ndipo potsata zomwe zalembedwa kunja kwake, aliyense wolumbira zabodza adzachotsedwanso.
Et il me dit: C'est la malédiction qui se promène sur tout le pays, et ensuite de laquelle, d'une part, tout voleur sera exterminé, et d'autre part, tout parjure sera exterminé.
4 Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti, ‘Temberero limeneli ndidzalitumiza, ndipo lidzalowa mʼnyumba ya munthu wakuba ndi munthu wolumbira zabodza mʼdzina langa. Lidzakhala mʼnyumbamo mpaka kuyiwonongeratu, matabwa ake ndi miyala yake yomwe.’”
Je l'ai lancée, dit l'Éternel des armées, afin qu'elle entre dans la maison du voleur, et dans la maison de qui fait par mon nom de faux serments, qu'elle séjourne dans sa maison et la détruise toute, et son bois et ses pierres.
5 Kenaka mngelo amene amayankhula nane uja anabwera patsogolo panga ndipo anandiwuza kuti, “Kweza maso ako tsopano kuti uwone kuti ndi chiyani chikubwerachi.”
Et l'ange qui parlait avec moi, parut et me dit: Lève donc les yeux et regarde! qu'est-ce qui sort là? Et je dis: Qu'est-ce?
6 Ndinafunsa kuti, “Kodi chimenechi nʼchiyani?” Mngeloyo anayankha kuti, “Limeneli ndi dengu loyezera.” Ndipo anawonjezera kunena kuti, “Umenewu ndi uchimo wa anthu mʼdziko lonse.”
Et il dit: C'est l'épha sortant. Et il dit: C'est à cela qu'ils visent dans tout le pays.
7 Pamenepo chovundikira chake chamtovu chinatukulidwa, ndipo mʼdengumo munali mutakhala mkazi.
Et voici, une masse de plomb fut soulevée, et il y avait dans l'épha une femme assise.
8 Mngeloyo anati, “Chimenechi ndi choyipa,” ndipo anamukankhira mkaziyo mʼdengu muja, nabwezera chovundikira chamtovu chija pamwamba pake.
Et il dit: C'est l'Impiété. Et il la repoussa au dedans de l'épha dont il referma l'ouverture avec la masse de plomb.
9 Kenaka ndinayangʼananso, ndipo ndinaona akazi awiri akuwuluka kubwera kumene kunali ine; akuwuluzika ndi mphepo. Iwo anali ndi mapiko ngati a kakowa, ndipo ananyamula dengu lija, kupita nalo pakati pa mlengalenga ndi dziko lapansi.
Et je levai les yeux et regardai, et voici, deux femmes parurent: le vent était dans leurs ailes, et elles avaient des ailes comme des ailes de cigogne, et elles enlevèrent l'épha entre la terre et le ciel.
10 Ine ndinafunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Dengulo akupita nalo kuti?”
Et je dis à l'ange qui parlait avec moi: Où emportent-elles l'épha?
11 Iye anayankha kuti, “Ku dziko la Babuloni kuti akalimangire nyumba. Nyumbayo ikadzatha, adzayikamo dengulo.”
Et il me dit: Elles vont lui établir une demeure dans le pays de Sinear, et une fois consolidée, il y sera posé sur son piédestal.

< Zekariya 5 >