< Zekariya 5 >

1 Ndinayangʼananso ndipo taonani ndinaona chikalata chimene chimawuluka.
And Y was conuertid, and reiside myn iyen, and siy, and lo! a book fleynge.
2 Mngelo uja anandifunsa kuti, “Kodi ukuona chiyani?” Ndinayankha kuti, “Ndikuona chikalata chikuwuluka, mulitali mwake mamita asanu ndi anayi ndipo mulifupi mwake mamita anayi ndi theka.”
And he seide to me, What seest thou? And Y seide, Lo! Y se a book fleynge; the lengthe therof was of twenti cubitis, and the breede therof of ten cubitis.
3 Ndipo mngeloyo anandiwuza kuti, “Awa ndi matemberero amene akupita pa dziko lonse lapansi; potsata zimene zalembedwa mʼkati mwa chikalatamo, aliyense wakuba adzachotsedwa, ndipo potsata zomwe zalembedwa kunja kwake, aliyense wolumbira zabodza adzachotsedwanso.
And he seide to me, This is the curs, that goith on the face of al erthe; for ech theef schal be demed, as it is writun there; and ech man swerynge, schal be demyd of this also.
4 Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti, ‘Temberero limeneli ndidzalitumiza, ndipo lidzalowa mʼnyumba ya munthu wakuba ndi munthu wolumbira zabodza mʼdzina langa. Lidzakhala mʼnyumbamo mpaka kuyiwonongeratu, matabwa ake ndi miyala yake yomwe.’”
Y schal lede out it, seith the Lord of oostis, and it schal come to the hous of a theef, and to the hous of hym that swerith falsli in my name; and it schal dwelle in myddil of hys hous, and schal waaste hym, and hise trees, and hise stoonys.
5 Kenaka mngelo amene amayankhula nane uja anabwera patsogolo panga ndipo anandiwuza kuti, “Kweza maso ako tsopano kuti uwone kuti ndi chiyani chikubwerachi.”
And the aungel wente out, that spak in me, and seide to me, Reyse thin iyen, and se, what this thing is, that goith out.
6 Ndinafunsa kuti, “Kodi chimenechi nʼchiyani?” Mngeloyo anayankha kuti, “Limeneli ndi dengu loyezera.” Ndipo anawonjezera kunena kuti, “Umenewu ndi uchimo wa anthu mʼdziko lonse.”
And Y seide, What is it? And he seide, This is a pot goyng out. And he seide, This is the iye of hem in al erthe.
7 Pamenepo chovundikira chake chamtovu chinatukulidwa, ndipo mʼdengumo munali mutakhala mkazi.
And lo! a talent of leed was borun; and lo! a womman sittynge in myddil of the pot.
8 Mngeloyo anati, “Chimenechi ndi choyipa,” ndipo anamukankhira mkaziyo mʼdengu muja, nabwezera chovundikira chamtovu chija pamwamba pake.
And he seide, This is vnpite, ether vnfeithfulnesse. And he castide doun hir in myddil of the pot, and sente a gobet of leed in to the mouth therof.
9 Kenaka ndinayangʼananso, ndipo ndinaona akazi awiri akuwuluka kubwera kumene kunali ine; akuwuluzika ndi mphepo. Iwo anali ndi mapiko ngati a kakowa, ndipo ananyamula dengu lija, kupita nalo pakati pa mlengalenga ndi dziko lapansi.
And Y reiside myn iyen, and siy, and lo! twei wymmen goynge out, and a spirit in wyngis of hem; and thei hadden wyngis as wyngis of a kite, and reisiden the pot bitwixe heuene and erthe.
10 Ine ndinafunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Dengulo akupita nalo kuti?”
And Y seide to the aungel that spak in me, Whidur beren these the pot?
11 Iye anayankha kuti, “Ku dziko la Babuloni kuti akalimangire nyumba. Nyumbayo ikadzatha, adzayikamo dengulo.”
And he seide to me, That an hous be bildid therto in the lond of Sennaar, and be stablischid, and set there on his foundement.

< Zekariya 5 >