< Zekariya 5 >

1 Ndinayangʼananso ndipo taonani ndinaona chikalata chimene chimawuluka.
And I turned and lifted up my eyes. And I saw, and behold, a book flying.
2 Mngelo uja anandifunsa kuti, “Kodi ukuona chiyani?” Ndinayankha kuti, “Ndikuona chikalata chikuwuluka, mulitali mwake mamita asanu ndi anayi ndipo mulifupi mwake mamita anayi ndi theka.”
And he said to me, “What do you see?” And I said, “I see a book flying. Its length is twenty cubits, and its width is ten cubits.”
3 Ndipo mngeloyo anandiwuza kuti, “Awa ndi matemberero amene akupita pa dziko lonse lapansi; potsata zimene zalembedwa mʼkati mwa chikalatamo, aliyense wakuba adzachotsedwa, ndipo potsata zomwe zalembedwa kunja kwake, aliyense wolumbira zabodza adzachotsedwanso.
And he said to me, “This is the curse that goes forth over the face of the whole earth. For every thief will be judged, just as it has been written there, and everyone who swears by this, will be judged in like manner.”
4 Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti, ‘Temberero limeneli ndidzalitumiza, ndipo lidzalowa mʼnyumba ya munthu wakuba ndi munthu wolumbira zabodza mʼdzina langa. Lidzakhala mʼnyumbamo mpaka kuyiwonongeratu, matabwa ake ndi miyala yake yomwe.’”
I will bring it forth, says the Lord of hosts, and it will approach to the house of the thief, and to the house of him who swears falsely by my name, and it will remain in the midst of his house and will consume it, with its wood and its stones.
5 Kenaka mngelo amene amayankhula nane uja anabwera patsogolo panga ndipo anandiwuza kuti, “Kweza maso ako tsopano kuti uwone kuti ndi chiyani chikubwerachi.”
And the angel had departed, who was speaking with me. And he said to me, “Lift up your eyes, and see what this is, that goes forth.”
6 Ndinafunsa kuti, “Kodi chimenechi nʼchiyani?” Mngeloyo anayankha kuti, “Limeneli ndi dengu loyezera.” Ndipo anawonjezera kunena kuti, “Umenewu ndi uchimo wa anthu mʼdziko lonse.”
And I said, “What, then, is it?” And he said, “This is a container going forth.” And he said, “This is their eye in all the earth.”
7 Pamenepo chovundikira chake chamtovu chinatukulidwa, ndipo mʼdengumo munali mutakhala mkazi.
And behold, a talent of lead was being carried; and behold, one woman sitting in the middle of the container.
8 Mngeloyo anati, “Chimenechi ndi choyipa,” ndipo anamukankhira mkaziyo mʼdengu muja, nabwezera chovundikira chamtovu chija pamwamba pake.
And he said, “This is impiety.” And he cast her into the middle of the container, and he sent the weight of lead into its mouth.
9 Kenaka ndinayangʼananso, ndipo ndinaona akazi awiri akuwuluka kubwera kumene kunali ine; akuwuluzika ndi mphepo. Iwo anali ndi mapiko ngati a kakowa, ndipo ananyamula dengu lija, kupita nalo pakati pa mlengalenga ndi dziko lapansi.
And I lifted up my eyes and I saw. And behold, two women were departing, and a spirit was in their wings, and they had wings like the wings of a kite, and they lifted up the container between earth and heaven.
10 Ine ndinafunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Dengulo akupita nalo kuti?”
And I said to the angel who was speaking with me, “Where are they taking the container?”
11 Iye anayankha kuti, “Ku dziko la Babuloni kuti akalimangire nyumba. Nyumbayo ikadzatha, adzayikamo dengulo.”
And he said to me, “To a house that may be built for it in the land of Shinar, and so that it may be established and set there upon its own base.”

< Zekariya 5 >