< Zekariya 4 >

1 Kenaka mngelo amene amayankhula nane anabwerera nandidzutsa, ngati mmene amadzutsira munthu amene ali mʼtulo.
Angel, ki je govoril z menoj, je ponovno prišel in me prebudil, kakor človeka, ki je prebujen iz svojega spanja
2 Anandifunsa kuti, “Kodi ukuona chiyani?” Ndinayankha kuti, “Ine ndikuona choyikapo nyale, chonse chagolide ndi mbale pamwamba pake ndi nyale zoyaka zisanu ndi ziwiri, iliyonse ili ndi zibowo zisanu ndi ziwiri zolowetsera zingwe zoyatsira.
ter mi rekel: »Kaj vidiš?« Rekel sem: »Pogledal sem in glej, svečnik, ves iz zlata, s skledico na njegovem vrhu in njegovih sedem svetilk na njem in sedem cevk k sedmim svetilkam, ki so na njegovem vrhu.
3 Ndiponso pambali pake pali mitengo ya olivi iwiri, umodzi uli kumanja kwa mbaleyo ndipo winawo kumanzere.”
In ob njem dve oljki, eno na desni strani skledice in drugo na njeni levi strani.«
4 Ndinamufunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Kodi zimenezi nʼchiyani mbuye wanga?”
Tako sem odgovoril in spregovoril angelu, ki je govoril z menoj, rekoč: »Kaj so ti, moj gospod?«
5 Iye anandiyankha kuti, “Kodi iwe sukuzidziwa zimenezi?” Ndinayankha kuti, “Ayi mbuye wanga.”
Potem je angel, ki je govoril z menoj, odgovoril in mi rekel: »Ali ne veš kaj so ti?« Rekel sem: »Ne, moj gospod.«
6 Choncho iye anandiwuza kuti, “Mawu a Yehova kwa Zerubabeli ndi awa: ‘Osati mwa nkhondo kapena ndi mphamvu, koma ndi Mzimu wanga,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Potem je odgovoril in mi spregovoril, rekoč: »To je beseda od Gospoda Zerubabélu, rekoč: ›Ne z močjo niti ne z oblastjo, temveč z mojim duhom, ‹« govori Gospod nad bojevniki.
7 “Kodi ndiwe yani, iwe phiri lamphamvu? Pamaso pa Zerubabeli udzasanduka dziko losalala. Pamenepo adzabweretsa mwala wotsiriza. Akamadzawuyika pamwamba anthu adzafuwula kuti, ‘Mulungu adalitse Nyumbayi! Mulungu adalitse Nyumbayi!’”
›Kdo si ti, oh velika gora? Pred Zerubabélom boš postala ravnina in on bo privedel njen zaključni kamen z vriskanji, kličoč: ›Milost, milost njemu.‹«
8 Ndipo Yehova anayankhulanso nane kuti,
Poleg tega je prišla k meni Gospodova beseda, rekoč:
9 “Manja a Zerubabeli ndiwo ayika maziko a Nyumbayi; adzatsiriza ndi manja ake omwewo. Pamenepo iwe udzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse ndiye anakutuma.
»Zerubabélove roke so položile temelj tej hiši. Njegove roke jo bodo tudi dokončale in vedel boš, da me je k vam poslal Gospod nad bojevniki.
10 “Ndani wanyoza tsiku la zinthu zazingʼono? Anthu adzasangalala akadzaona chingwe choyezera mʼmanja mwa Zerubabeli. (“Nyale zisanu ndi ziwirizi ndi maso a Yehova, amene amayangʼanayangʼana pa dziko lapansi.”)
Kajti kdo je preziral dan majhnih stvari? Kajti razveseljevali se bodo in videli grezilo v roki Zerubabéla s tistimi sedmimi. Te so Gospodove oči, ki tečejo sem ter tja po celotni zemlji.«
11 Kenaka ndinafunsa mngelo uja kuti, “Kodi mitengo ya olivi iwiri ili kumanja ndi kumanzere kwa choyikapo nyalechi ikutanthauza chiyani?”
Potem sem odgovoril in mu rekel: »Kaj sta ti dve oljki na desni strani svečnika in na njegovi levi strani?«
12 Ndinamufunsanso kuti, “Kodi nthambi ziwiri za mtengo wa olivi zomwe zili pambali pa mipopi yodzera mafuta iwiri yagolide zikutanthauza chiyani?”
Ponovno sem odgovoril in mu rekel: »Kaj sta ti dve oljkovi mladiki, ki skozi dve zlati cevki praznita zlato olje iz njiju.«
13 Iye anandiyankha kuti, “Kodi iwe sukuzidziwa zimenezi?” Ine ndinati, “Ayi mbuye wanga.”
Odgovoril mi je in rekel: »Ne veš kaj sta le-ti? Rekel sem: »Ne, moj gospod.«
14 Choncho iye anati, “Amenewa ndi anthu awiri amene adzozedwa kuti atumikire Ambuye pa dziko lonse lapansi.”
Potem je rekel: »To sta dva maziljenca, ki stojita pri Gospodu celotne zemlje.«

< Zekariya 4 >