< Zekariya 4 >

1 Kenaka mngelo amene amayankhula nane anabwerera nandidzutsa, ngati mmene amadzutsira munthu amene ali mʼtulo.
Ingilosi eyayikhuluma lami yabuya njalo yazangivusa njengomuntu evuswa ebuthongweni.
2 Anandifunsa kuti, “Kodi ukuona chiyani?” Ndinayankha kuti, “Ine ndikuona choyikapo nyale, chonse chagolide ndi mbale pamwamba pake ndi nyale zoyaka zisanu ndi ziwiri, iliyonse ili ndi zibowo zisanu ndi ziwiri zolowetsera zingwe zoyatsira.
Yangibuza yathi, “Ubonani na?” Ngaphendula ngathi, “Ngibona uluthi lwesibane olwenziwe ngokugcweleyo ngegolide, lulomganu phezulu lezibane eziyisikhombisa lezimbobo zezibane eziyisikhombisa.
3 Ndiponso pambali pake pali mitengo ya olivi iwiri, umodzi uli kumanja kwa mbaleyo ndipo winawo kumanzere.”
Njalo kulezihlahla zama-oliva ezimbili eduze kwalo, esinye ngakwesokunene komganu, esinye kwesokhohlo.”
4 Ndinamufunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Kodi zimenezi nʼchiyani mbuye wanga?”
Ngayibuza ingilosi eyayikhuluma lami, ngathi, “Kuyini lokhu, nkosi yami?”
5 Iye anandiyankha kuti, “Kodi iwe sukuzidziwa zimenezi?” Ndinayankha kuti, “Ayi mbuye wanga.”
Yaphendula yathi, “Kawukwazi ukuthi yizinto bani lezi?” Ngathi, “Hatshi, nkosi yami.”
6 Choncho iye anandiwuza kuti, “Mawu a Yehova kwa Zerubabeli ndi awa: ‘Osati mwa nkhondo kapena ndi mphamvu, koma ndi Mzimu wanga,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Yasisithi kimi, “Nanti ilizwi likaThixo kuZerubhabheli, ‘Hatshi ngempi kumbe ngamandla, kodwa ngoMoya wami,’ kutsho uThixo uSomandla.
7 “Kodi ndiwe yani, iwe phiri lamphamvu? Pamaso pa Zerubabeli udzasanduka dziko losalala. Pamenepo adzabweretsa mwala wotsiriza. Akamadzawuyika pamwamba anthu adzafuwula kuti, ‘Mulungu adalitse Nyumbayi! Mulungu adalitse Nyumbayi!’”
Uvele uyini, wena ntaba enkulu? KuZerubhabheli uzakuba ngumhlabathi owendlalekileyo. Khonapho usezaletha ilitshe lokuphetha abantu bememeza besithi, ‘Nkulunkulu libusise! Nkulunkulu libusise!’”
8 Ndipo Yehova anayankhulanso nane kuti,
Kwasekufika ilizwi likaThixo kimi lisithi:
9 “Manja a Zerubabeli ndiwo ayika maziko a Nyumbayi; adzatsiriza ndi manja ake omwewo. Pamenepo iwe udzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse ndiye anakutuma.
“Izandla zikaZerubhabheli zisibekile isisekelo saleli ithempeli; izandla zakhe zizaliqedisa ukulakha. Ngakho lizakwazi ukuthi uThixo uSomandla ungithumile kini.
10 “Ndani wanyoza tsiku la zinthu zazingʼono? Anthu adzasangalala akadzaona chingwe choyezera mʼmanja mwa Zerubabeli. (“Nyale zisanu ndi ziwirizi ndi maso a Yehova, amene amayangʼanayangʼana pa dziko lapansi.”)
Ngubani oludelelayo usuku lwezinto ezincane? Amehlo kaThixo ayisikhombisa agcwala umhlaba wonke jikelele azathokozelela ukubona intambo yokuqondisa esandleni sikaZerubhabheli?”
11 Kenaka ndinafunsa mngelo uja kuti, “Kodi mitengo ya olivi iwiri ili kumanja ndi kumanzere kwa choyikapo nyalechi ikutanthauza chiyani?”
Ngasengiyibuza ingilosi, ngathi, “Lezi zihlahla ezimbili zama-oliva kwesokunene lakwesokhohlo phezu koluthi lwesibane ngezani?”
12 Ndinamufunsanso kuti, “Kodi nthambi ziwiri za mtengo wa olivi zomwe zili pambali pa mipopi yodzera mafuta iwiri yagolide zikutanthauza chiyani?”
Ngayibuza futhi ngathi, “Amahlumela la amabili omʼoliva eceleni kwezinti ezimbili zegolide okumpompoza kuzo amafutha aligolide zona ziyini?”
13 Iye anandiyankha kuti, “Kodi iwe sukuzidziwa zimenezi?” Ine ndinati, “Ayi mbuye wanga.”
Yaphendula yathi, “Kawuzazi ukuthi ziyini na?” Ngathi, “Hatshi, nkosi yami.”
14 Choncho iye anati, “Amenewa ndi anthu awiri amene adzozedwa kuti atumikire Ambuye pa dziko lonse lapansi.”
Yasisithi, “Laba yibo ababili abagcotshiweyo ukukhonza iNkosi yomhlaba wonke.”

< Zekariya 4 >