< Zekariya 4 >

1 Kenaka mngelo amene amayankhula nane anabwerera nandidzutsa, ngati mmene amadzutsira munthu amene ali mʼtulo.
Kalpasanna, nagsubli ti anghel a nakisarsarita kaniak ket riniingnak a kas iti maysa a tao a nagriing iti pannaturogna.
2 Anandifunsa kuti, “Kodi ukuona chiyani?” Ndinayankha kuti, “Ine ndikuona choyikapo nyale, chonse chagolide ndi mbale pamwamba pake ndi nyale zoyaka zisanu ndi ziwiri, iliyonse ili ndi zibowo zisanu ndi ziwiri zolowetsera zingwe zoyatsira.
Kinunana kaniak, “Ania ti makitkitam? Kinunak, “Makitkitak ti maysa a kandelero a pasig a balitok, nga adda malukong iti rabawna. Addaan daytoy iti pito a pagsilawan ken addaan iti pito a pabelo iti rabaw ti tunggal pagsilawan.
3 Ndiponso pambali pake pali mitengo ya olivi iwiri, umodzi uli kumanja kwa mbaleyo ndipo winawo kumanzere.”
Adda dua a kayo nga olibo iti abay daytoy, maysa iti makannawan ti malukong ken maysa iti makannigid.”
4 Ndinamufunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Kodi zimenezi nʼchiyani mbuye wanga?”
Isu a kinasaritak manen ti anghel a nakisarsarita kaniak. Kinunak, “Apok ania ti kaipapanan dagitoy a banbanag?”
5 Iye anandiyankha kuti, “Kodi iwe sukuzidziwa zimenezi?” Ndinayankha kuti, “Ayi mbuye wanga.”
Simmungbat ti anghel a nakisarsarita kaniak a kunana, “Apay saanmo pay nga ammo ti kaipapanan dagitoy a banbanag?” Kinunak, “Saan apok,”.
6 Choncho iye anandiwuza kuti, “Mawu a Yehova kwa Zerubabeli ndi awa: ‘Osati mwa nkhondo kapena ndi mphamvu, koma ndi Mzimu wanga,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Isu a kinunana kaniak, “Daytoy ti sao ni Yahweh a para kenni Zerubbabel: 'Saan a babaen iti pigsa wenno pannakabalin, ngem babaen iti Espirituk,' kuna ni Yahweh a Mannakabalin-amin.
7 “Kodi ndiwe yani, iwe phiri lamphamvu? Pamaso pa Zerubabeli udzasanduka dziko losalala. Pamenepo adzabweretsa mwala wotsiriza. Akamadzawuyika pamwamba anthu adzafuwula kuti, ‘Mulungu adalitse Nyumbayi! Mulungu adalitse Nyumbayi!’”
'Aniaka koma, dakkel a bantay? Iti sangoanan ni Zerubbabel, agbalinkanto a patad, ket iruarna ti kangrunaan a bato a mangipukkaw, “Parabur! Parabur!””
8 Ndipo Yehova anayankhulanso nane kuti,
Immay kaniak ti sao ni Yahweh:
9 “Manja a Zerubabeli ndiwo ayika maziko a Nyumbayi; adzatsiriza ndi manja ake omwewo. Pamenepo iwe udzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse ndiye anakutuma.
“Impasdek ni Zerubabel ti pundasion daytoy a balay ket leppasennanto daytoy. Ket maammoanyonto nga imbaonnak ni Yahweh a Mannakabalin-amin kadakayo.
10 “Ndani wanyoza tsiku la zinthu zazingʼono? Anthu adzasangalala akadzaona chingwe choyezera mʼmanja mwa Zerubabeli. (“Nyale zisanu ndi ziwirizi ndi maso a Yehova, amene amayangʼanayangʼana pa dziko lapansi.”)
Siasino ti nangumsi kadagiti aldaw dagiti babassit a banbanag a nagappuanan? Agrag-onto dagitoy a tattao ket makitadanto ti bato a pangrukod iti kalinteg ti pasdek iti ima ni Zerubbabel. (Ibagbagi dagitoy pito a pagsilawan dagiti mata ni Yahweh a mangwanwanawan iti entero a daga.)”
11 Kenaka ndinafunsa mngelo uja kuti, “Kodi mitengo ya olivi iwiri ili kumanja ndi kumanzere kwa choyikapo nyalechi ikutanthauza chiyani?”
Ket sinaludsodko ti anghel, “Ania dagitoy dua a kayo nga olibo a nakatakder iti makannigid ken makannawan a sikigan ti kandelero?”
12 Ndinamufunsanso kuti, “Kodi nthambi ziwiri za mtengo wa olivi zomwe zili pambali pa mipopi yodzera mafuta iwiri yagolide zikutanthauza chiyani?”
Sinaludsodko pay kenkuana iti maminsan, “Ania dagitoy a dua a sanga ti olibo iti abay dagiti dua a balitok a tubo a pagay-ayusan ti maris balitok a lana?
13 Iye anandiyankha kuti, “Kodi iwe sukuzidziwa zimenezi?” Ine ndinati, “Ayi mbuye wanga.”
“Apay saanmo pay nga ammo no ania dagitoy?” Ket kinunak, “Saan, apok.”
14 Choncho iye anati, “Amenewa ndi anthu awiri amene adzozedwa kuti atumikire Ambuye pa dziko lonse lapansi.”
Isu a kinunana, “Ibagbagi dagitoy dua a kayo nga olibo ti dua a lallaki nga agserserbi iti Apo iti entero a daga.”

< Zekariya 4 >