< Zekariya 4 >
1 Kenaka mngelo amene amayankhula nane anabwerera nandidzutsa, ngati mmene amadzutsira munthu amene ali mʼtulo.
Et l’ange qui parlait en moi revint, et me réveilla comme un homme qu’on réveille de son sommeil.
2 Anandifunsa kuti, “Kodi ukuona chiyani?” Ndinayankha kuti, “Ine ndikuona choyikapo nyale, chonse chagolide ndi mbale pamwamba pake ndi nyale zoyaka zisanu ndi ziwiri, iliyonse ili ndi zibowo zisanu ndi ziwiri zolowetsera zingwe zoyatsira.
Et il me dit: Que vois-tu, toi? Et je répondis: J’ai vu, et voilà un chandelier tout d’or, et sa lampe sur son sommet, et ses sept lampes au-dessus; et sept canaux aux lampes qui étaient sur son sommet;
3 Ndiponso pambali pake pali mitengo ya olivi iwiri, umodzi uli kumanja kwa mbaleyo ndipo winawo kumanzere.”
Et deux oliviers au-dessus; un à la droite de la lampe, et un à sa gauche.
4 Ndinamufunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Kodi zimenezi nʼchiyani mbuye wanga?”
Et je pris la parole, et je dis à l’ange qui parlait en moi: Qu’est ceci, mon Seigneur?
5 Iye anandiyankha kuti, “Kodi iwe sukuzidziwa zimenezi?” Ndinayankha kuti, “Ayi mbuye wanga.”
Et l’ange qui parlait en moi me répondit et me dit: Est-ce que tu ne sais pas ce que c’est? Et je dis: Non, mon Seigneur.
6 Choncho iye anandiwuza kuti, “Mawu a Yehova kwa Zerubabeli ndi awa: ‘Osati mwa nkhondo kapena ndi mphamvu, koma ndi Mzimu wanga,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Et il reprit, et s’adressa à moi, disant: Voici la parole du Seigneur à Zorobabel. Ce n’est point par une armée, ni par la force, que tu achèveras le temple, mais par mon esprit, dit le Seigneur des armées.
7 “Kodi ndiwe yani, iwe phiri lamphamvu? Pamaso pa Zerubabeli udzasanduka dziko losalala. Pamenepo adzabweretsa mwala wotsiriza. Akamadzawuyika pamwamba anthu adzafuwula kuti, ‘Mulungu adalitse Nyumbayi! Mulungu adalitse Nyumbayi!’”
Qu’es-tu, grande montagne, devant Zorobabel? tu seras aplanie; il posera la pierre principale, et il ajoutera une beauté égale à sa beauté.
8 Ndipo Yehova anayankhulanso nane kuti,
Et la parole du Seigneur me fut adressée, disant:
9 “Manja a Zerubabeli ndiwo ayika maziko a Nyumbayi; adzatsiriza ndi manja ake omwewo. Pamenepo iwe udzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse ndiye anakutuma.
Les mains de Zorobabel ont fondé cette maison, et ses mains l’achèveront; et vous saurez que le Seigneur des armées m’a envoyé vers vous.
10 “Ndani wanyoza tsiku la zinthu zazingʼono? Anthu adzasangalala akadzaona chingwe choyezera mʼmanja mwa Zerubabeli. (“Nyale zisanu ndi ziwirizi ndi maso a Yehova, amene amayangʼanayangʼana pa dziko lapansi.”)
Car qui a vu avec mépris les jours courts? Mais on se réjouira, et on verra le plomb à la main de Zorobabel. Ce sont là les sept yeux du Seigneur qui parcourent toute la terre.
11 Kenaka ndinafunsa mngelo uja kuti, “Kodi mitengo ya olivi iwiri ili kumanja ndi kumanzere kwa choyikapo nyalechi ikutanthauza chiyani?”
Et je repris et je lui dis: Que sont ces deux oliviers à la droite du chandelier, et à sa gauche?
12 Ndinamufunsanso kuti, “Kodi nthambi ziwiri za mtengo wa olivi zomwe zili pambali pa mipopi yodzera mafuta iwiri yagolide zikutanthauza chiyani?”
Et je repris une seconde fois, et je lui dis: Que sont ces deux branches d’oliviers qui sont auprès de deux becs d’or dans lesquels sont les canaux d’or par où coule l’huile?
13 Iye anandiyankha kuti, “Kodi iwe sukuzidziwa zimenezi?” Ine ndinati, “Ayi mbuye wanga.”
Et il m’interpella, en disant: Est-ce que tu ne sais pas ce que c’est? Et je répondis: Non, mon Seigneur.
14 Choncho iye anati, “Amenewa ndi anthu awiri amene adzozedwa kuti atumikire Ambuye pa dziko lonse lapansi.”
Et il dit: Ce sont les deux fils de l’huile sainte, qui assistent devant le Dominateur de toute la terre.