< Zekariya 4 >

1 Kenaka mngelo amene amayankhula nane anabwerera nandidzutsa, ngati mmene amadzutsira munthu amene ali mʼtulo.
L'ange qui parlait avec moi revint et me réveilla, comme un homme qu'on réveille de son sommeil.
2 Anandifunsa kuti, “Kodi ukuona chiyani?” Ndinayankha kuti, “Ine ndikuona choyikapo nyale, chonse chagolide ndi mbale pamwamba pake ndi nyale zoyaka zisanu ndi ziwiri, iliyonse ili ndi zibowo zisanu ndi ziwiri zolowetsera zingwe zoyatsira.
Il me dit: « Que vois-tu? » J'ai dit: « J'ai vu, et voici un chandelier tout d'or, avec sa coupe au sommet, et ses sept lampes dessus; il y a sept tuyaux à chacune des lampes qui sont au sommet;
3 Ndiponso pambali pake pali mitengo ya olivi iwiri, umodzi uli kumanja kwa mbaleyo ndipo winawo kumanzere.”
et deux oliviers près de lui, l'un à droite de la coupe, et l'autre à gauche. »
4 Ndinamufunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Kodi zimenezi nʼchiyani mbuye wanga?”
J'ai répondu et j'ai parlé à l'ange qui m'a parlé, en disant: « Qu'est-ce que c'est, mon seigneur? »
5 Iye anandiyankha kuti, “Kodi iwe sukuzidziwa zimenezi?” Ndinayankha kuti, “Ayi mbuye wanga.”
Alors l'ange qui parlait avec moi me répondit: « Ne sais-tu pas ce que c'est? » J'ai dit, « Non, mon seigneur. »
6 Choncho iye anandiwuza kuti, “Mawu a Yehova kwa Zerubabeli ndi awa: ‘Osati mwa nkhondo kapena ndi mphamvu, koma ndi Mzimu wanga,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Alors il prit la parole et me dit: « Voici la parole que Yahvé a adressée à Zorobabel: Ce n'est ni par la force, ni par la puissance, mais par mon Esprit, dit Yahvé des armées.
7 “Kodi ndiwe yani, iwe phiri lamphamvu? Pamaso pa Zerubabeli udzasanduka dziko losalala. Pamenepo adzabweretsa mwala wotsiriza. Akamadzawuyika pamwamba anthu adzafuwula kuti, ‘Mulungu adalitse Nyumbayi! Mulungu adalitse Nyumbayi!’”
Qui es-tu, grande montagne? Devant Zorobabel, tu n'es qu'une plaine, et il fera sortir la pierre de faîte aux cris de « Grâce, grâce, à elle! ».
8 Ndipo Yehova anayankhulanso nane kuti,
La parole de Yahvé me fut adressée, en ces termes:
9 “Manja a Zerubabeli ndiwo ayika maziko a Nyumbayi; adzatsiriza ndi manja ake omwewo. Pamenepo iwe udzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse ndiye anakutuma.
Les mains de Zorobabel ont posé les fondements de cette maison. Ses mains l'achèveront aussi, et vous saurez que l'Éternel des armées m'a envoyé vers vous.
10 “Ndani wanyoza tsiku la zinthu zazingʼono? Anthu adzasangalala akadzaona chingwe choyezera mʼmanja mwa Zerubabeli. (“Nyale zisanu ndi ziwirizi ndi maso a Yehova, amene amayangʼanayangʼana pa dziko lapansi.”)
En effet, qui méprise le jour des petites choses? Car ces sept-là se réjouiront, et ils verront le fil à plomb dans la main de Zorobabel. Ce sont les yeux de Yahvé, qui parcourent de long en large toute la terre. »
11 Kenaka ndinafunsa mngelo uja kuti, “Kodi mitengo ya olivi iwiri ili kumanja ndi kumanzere kwa choyikapo nyalechi ikutanthauza chiyani?”
Et je lui demandai: « Que sont ces deux oliviers à droite du chandelier et à gauche de celui-ci? ».
12 Ndinamufunsanso kuti, “Kodi nthambi ziwiri za mtengo wa olivi zomwe zili pambali pa mipopi yodzera mafuta iwiri yagolide zikutanthauza chiyani?”
Je lui demandai une seconde fois: « Que sont ces deux branches d'olivier, qui sont à côté des deux becs d'or qui versent l'huile d'or d'eux-mêmes? »
13 Iye anandiyankha kuti, “Kodi iwe sukuzidziwa zimenezi?” Ine ndinati, “Ayi mbuye wanga.”
Il m'a répondu: « Tu ne sais pas ce que c'est? » J'ai dit, « Non, mon seigneur. »
14 Choncho iye anati, “Amenewa ndi anthu awiri amene adzozedwa kuti atumikire Ambuye pa dziko lonse lapansi.”
Puis il dit: « Ce sont les deux oints qui se tiennent auprès du Seigneur de toute la terre. »

< Zekariya 4 >