< Zekariya 4 >

1 Kenaka mngelo amene amayankhula nane anabwerera nandidzutsa, ngati mmene amadzutsira munthu amene ali mʼtulo.
And once more the messenger who was speaking with me, roused me up, just as a man might be roused up out of his sleep.
2 Anandifunsa kuti, “Kodi ukuona chiyani?” Ndinayankha kuti, “Ine ndikuona choyikapo nyale, chonse chagolide ndi mbale pamwamba pake ndi nyale zoyaka zisanu ndi ziwiri, iliyonse ili ndi zibowo zisanu ndi ziwiri zolowetsera zingwe zoyatsira.
Then said he unto me, What canst thou see? And I said—I have looked, and lo! a Lampstand—all of gold, with the Bowl thereof upon the top thereof, and its Seven Lamps upon it, Seven Pipes each, to the lamps which are upon the top thereof;
3 Ndiponso pambali pake pali mitengo ya olivi iwiri, umodzi uli kumanja kwa mbaleyo ndipo winawo kumanzere.”
and, Two Olive-trees, by it, —one upon the right hand of the bowl, and one upon the left hand thereof.
4 Ndinamufunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Kodi zimenezi nʼchiyani mbuye wanga?”
Then responded I, and said unto the messenger who was speaking with me, saying, —What are these, my lord?
5 Iye anandiyankha kuti, “Kodi iwe sukuzidziwa zimenezi?” Ndinayankha kuti, “Ayi mbuye wanga.”
Then answered the messenger who was speaking with me, and said unto me, Knowest thou not what these, are? And I said, No my lord.
6 Choncho iye anandiwuza kuti, “Mawu a Yehova kwa Zerubabeli ndi awa: ‘Osati mwa nkhondo kapena ndi mphamvu, koma ndi Mzimu wanga,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Then responded he, and spake unto me, saying, This, is the word of Yahweh, unto Zerubbabel, saying, —Not by wealth, nor by strength, but by my spirit, saith Yahweh of hosts.
7 “Kodi ndiwe yani, iwe phiri lamphamvu? Pamaso pa Zerubabeli udzasanduka dziko losalala. Pamenepo adzabweretsa mwala wotsiriza. Akamadzawuyika pamwamba anthu adzafuwula kuti, ‘Mulungu adalitse Nyumbayi! Mulungu adalitse Nyumbayi!’”
Who, art, thou, O great mountain? Before Zerubbabel, [brought down] to a plain! So shall he bring forth the headstone, with thundering shouts Beautiful! Beautiful! thereunto.
8 Ndipo Yehova anayankhulanso nane kuti,
Then came the word of Yahweh unto me, saying:
9 “Manja a Zerubabeli ndiwo ayika maziko a Nyumbayi; adzatsiriza ndi manja ake omwewo. Pamenepo iwe udzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse ndiye anakutuma.
The hands of Zerubbabel, have founded this house, and, his hands, shall finish it, —So shalt thou know that, Yahweh of hosts, hath sent me unto you.
10 “Ndani wanyoza tsiku la zinthu zazingʼono? Anthu adzasangalala akadzaona chingwe choyezera mʼmanja mwa Zerubabeli. (“Nyale zisanu ndi ziwirizi ndi maso a Yehova, amene amayangʼanayangʼana pa dziko lapansi.”)
For who hath despised the day of small things? Yet shall they rejoice, when they see the plummet-stone in the hand of Zerubbabel, —these seven! The eyes of Yahweh, they are—running to and fro throughout all the earth.
11 Kenaka ndinafunsa mngelo uja kuti, “Kodi mitengo ya olivi iwiri ili kumanja ndi kumanzere kwa choyikapo nyalechi ikutanthauza chiyani?”
Then responded I, and said unto him, —What are these two olive-trees, upon the right of the lampstand, and upon the left thereof?
12 Ndinamufunsanso kuti, “Kodi nthambi ziwiri za mtengo wa olivi zomwe zili pambali pa mipopi yodzera mafuta iwiri yagolide zikutanthauza chiyani?”
And I responded a second time, and said unto him, —What are the two branches of the olive- trees which join the two golden tubes, which empty out of them the golden oil?
13 Iye anandiyankha kuti, “Kodi iwe sukuzidziwa zimenezi?” Ine ndinati, “Ayi mbuye wanga.”
And he spake unto me, saying, Knowest thou not what these are? And I said, No, my lord.
14 Choncho iye anati, “Amenewa ndi anthu awiri amene adzozedwa kuti atumikire Ambuye pa dziko lonse lapansi.”
Then said he, These, are the two Anointed Ones, —who stand near the Lord of all the earth.

< Zekariya 4 >