< Zekariya 2 >

1 Kenaka ndinayangʼananso, ndipo ndinaona munthu atanyamula chingwe choyezera mʼmanja mwake.
Opet podigoh oèi svoje i vidjeh, i gle, èovjek, i u ruci mu uže mjeraèko.
2 Ndipo ndinafunsa kuti, “Kodi ukupita kuti?” Anandiyankha kuti, “Akukayeza Yerusalemu kuti ndidziwe mulifupi mwake ndi mulitali mwake.”
I rekoh: kuda ideš? A on mi reèe: da izmjerim Jerusalim da vidim kolika mu je širina i kolika mu je dužina.
3 Taonani, mngelo amene amayankhula nane uja akuchoka, mngelo wina anabwera kudzakumana naye
I gle, anðeo koji govoraše sa mnom izide, i drugi anðeo izide mu na susret.
4 ndipo anamuwuza kuti, “Thamanga, kamuwuze mnyamatayo kuti, ‘Yerusalemu udzakhala mzinda wopanda malinga chifukwa mudzakhala anthu ambiri ndiponso ziweto zochuluka.
I reèe mu: trèi, govori onom mladiæu i reci: Jerusalimljani æe se naseliti po selima radi mnoštva ljudi i stoke što æe biti u njemu.
5 Ndipo Ine mwini ndidzakhala linga lamoto kuteteza mzindawo,’ akutero Yehova, ‘ndipo ndidzakhala ulemerero mʼkati mwake.’
I ja æu mu, govori Gospod, biti zid ognjen unaokolo i biæu za slavu usred njega.
6 “Tulukani! Tulukani! Thawaniko ku dziko la kumpoto,” akutero Yehova, “pakuti ndinakumwazirani ku mphepo zinayi zamlengalenga,” akutero Yehova.
Ej, ej, bježite iz zemlje sjeverne, govori Gospod, jer vas razasuh u èetiri vjetra nebeska, govori Gospod.
7 “Tuluka, iwe Ziyoni! Thawa, iwe amene umakhala mʼdziko la mwana wamkazi wa Babuloni!”
Ej Sione, koji sjediš kod kæeri Vavilonske, izbavi se.
8 Pakuti Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Atatha kundilemekeza wanditumiza kwa anthu a mitundu ina amene anakufunkhani; pakuti aliyense wokhudza inu wakhudza mwanadiso wanga.
Jer ovako veli Gospod nad vojskama: za slavom posla me k narodima, koji vas oplijeniše; jer ko tièe u vas, tièe u zjenicu oka njegova.
9 Ndithu Ine ndidzawamenya anthuwo ndi dzanja langa ndipo amene anali akapolo awo ndiye adzawalande zinthu. Pamenepo mudzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse ndiye wandituma.
Jer evo ja æu mahnuti rukom svojom na njih, i biæe plijen slugama svojim, i poznaæete da me je poslao Gospod nad vojskama.
10 “Iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, fuwula ndipo sangalala. Pakuti taona ndikubwera, ndipo ndidzakhala pakati pako,” akutero Yehova.
Pjevaj i veseli se, kæeri Sionska, jer evo ja idem i nastavaæu usred tebe, govori Gospod.
11 “Nthawi imeneyo anthu a mitundu yambiri adzabwera kwa Yehova ndipo adzasanduka anthu anga. Ndidzakhala pakati pako ndipo iwe udzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse wandituma kwa iwe.
I mnogi æe se narodi prilijepiti ka Gospodu u taj dan, i biæe mi narod, i ja æu nastavati usred tebe, i poznaæeš da me je poslao k tebi Gospod nad vojskama.
12 Yehova adzachititsa kuti Yuda akhale chuma chake mʼdziko lopatulika ndipo adzasankhanso Yerusalemu.
I Gospod æe naslijediti Judu, svoj dio, u zemlji svetoj, i opet æe izabrati Jerusalim.
13 Khalani chete pamaso pa Yehova anthu nonse, chifukwa Iye wavumbuluka kuchoka ku malo ake opatulika.”
Neka muèi svako tijelo pred Gospodom, jer usta iz svetoga stana svojega.

< Zekariya 2 >