< Zekariya 2 >

1 Kenaka ndinayangʼananso, ndipo ndinaona munthu atanyamula chingwe choyezera mʼmanja mwake.
Ам ридикат окий ши м-ам уйтат, ши ятэ кэ ера ун ом каре циня ын мынэ о фуние де мэсурат.
2 Ndipo ndinafunsa kuti, “Kodi ukupita kuti?” Anandiyankha kuti, “Akukayeza Yerusalemu kuti ndidziwe mulifupi mwake ndi mulitali mwake.”
Л-ам ынтребат: „Унде те дучь?” Ши ел мь-а зис: „Мэ дук сэ мэсор Иерусалимул, ка сэ вэд че лэциме ши че лунӂиме аре.”
3 Taonani, mngelo amene amayankhula nane uja akuchoka, mngelo wina anabwera kudzakumana naye
Ши ынӂерул каре ворбя ку мине а ынаинтат, ши ун алт ынӂер й-а ешит ынаинте.
4 ndipo anamuwuza kuti, “Thamanga, kamuwuze mnyamatayo kuti, ‘Yerusalemu udzakhala mzinda wopanda malinga chifukwa mudzakhala anthu ambiri ndiponso ziweto zochuluka.
Ел й-а зис: „Аляргэ де ворбеште тынэрулуй ачестуя ши спуне-й: ‘Иерусалимул ва фи о четате дескисэ дин причина мулцимий оаменилор ши вителор каре вор фи ын мижлокул луй;
5 Ndipo Ine mwini ndidzakhala linga lamoto kuteteza mzindawo,’ akutero Yehova, ‘ndipo ndidzakhala ulemerero mʼkati mwake.’
Еу Ынсумь’, зиче Домнул, ‘вой фи ун зид де фок де жур ымпрежурул луй ши вой фи слава луй ын мижлокул луй!’”
6 “Tulukani! Tulukani! Thawaniko ku dziko la kumpoto,” akutero Yehova, “pakuti ndinakumwazirani ku mphepo zinayi zamlengalenga,” akutero Yehova.
„Фуӂиць, фуӂиць дин цара де ла мязэноапте!”, зиче Домнул. „Кэч в-ам ымпрэштият ын челе патру вынтурь але черурилор”, зиче Домнул.
7 “Tuluka, iwe Ziyoni! Thawa, iwe amene umakhala mʼdziko la mwana wamkazi wa Babuloni!”
„Скапэ, Сиоане, ту каре локуешть ла фийка Бабилонулуй!”
8 Pakuti Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Atatha kundilemekeza wanditumiza kwa anthu a mitundu ina amene anakufunkhani; pakuti aliyense wokhudza inu wakhudza mwanadiso wanga.
Кэч аша ворбеште Домнул оштирилор: „Дупэ славэ м-а тримис Ел ла нямуриле каре в-ау жефуит; кэч чел че се атинӂе де вой се атинӂе де лумина окилор Луй.
9 Ndithu Ine ndidzawamenya anthuwo ndi dzanja langa ndipo amene anali akapolo awo ndiye adzawalande zinthu. Pamenepo mudzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse ndiye wandituma.
Ятэ, Ымь ридик мына ымпотрива лор”, зиче Домнул, „ши еле вор фи прада челор че ле ерау супушь, ка сэ штиць кэ Домнул оштирилор м-а тримис.
10 “Iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, fuwula ndipo sangalala. Pakuti taona ndikubwera, ndipo ndidzakhala pakati pako,” akutero Yehova.
Стригэ де веселие ши букурэ-те, фийка Сионулуй! Кэч, ятэ, Еу вин ши вой локуи ын мижлокул тэу”, зиче Домнул.
11 “Nthawi imeneyo anthu a mitundu yambiri adzabwera kwa Yehova ndipo adzasanduka anthu anga. Ndidzakhala pakati pako ndipo iwe udzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse wandituma kwa iwe.
„Мулте нямурь се вор алипи де Домнул ын зиуа ачея ши вор фи попорул Меу. Еу вой локуи ын мижлокул тэу ши вей шти кэ Домнул оштирилор м-а тримис ла тине.”
12 Yehova adzachititsa kuti Yuda akhale chuma chake mʼdziko lopatulika ndipo adzasankhanso Yerusalemu.
Домнул ва луа ын стэпынире пе Иуда, ка партя Луй де моштенире ын пэмынтул сфынт, ши ва алеӂе ярэшь Иерусалимул.
13 Khalani chete pamaso pa Yehova anthu nonse, chifukwa Iye wavumbuluka kuchoka ku malo ake opatulika.”
Орьче фэптурэ сэ такэ ынаинтя Домнулуй, кэч Ел С-а ши скулат дин Локашул Луй чел Сфынт!

< Zekariya 2 >