< Zekariya 2 >
1 Kenaka ndinayangʼananso, ndipo ndinaona munthu atanyamula chingwe choyezera mʼmanja mwake.
Et je levai les yeux, et je vis; et voilà un homme, et dans sa main un cordeau d’arpenteur.
2 Ndipo ndinafunsa kuti, “Kodi ukupita kuti?” Anandiyankha kuti, “Akukayeza Yerusalemu kuti ndidziwe mulifupi mwake ndi mulitali mwake.”
Et je dis: Où vas-tu? Et il me répondit: Mesurer Jérusalem, et voir quelle est sa largeur et quelle est sa longueur.
3 Taonani, mngelo amene amayankhula nane uja akuchoka, mngelo wina anabwera kudzakumana naye
Et voilà que l’ange qui parlait en moi sortit, et un autre ange sortait à sa rencontre.
4 ndipo anamuwuza kuti, “Thamanga, kamuwuze mnyamatayo kuti, ‘Yerusalemu udzakhala mzinda wopanda malinga chifukwa mudzakhala anthu ambiri ndiponso ziweto zochuluka.
Et il lui dit: Cours, parle à ce jeune homme, en disant: Jérusalem sera habitée sans mur, à cause de la multitude des hommes et des troupeaux qui seront au milieu d’elle.
5 Ndipo Ine mwini ndidzakhala linga lamoto kuteteza mzindawo,’ akutero Yehova, ‘ndipo ndidzakhala ulemerero mʼkati mwake.’
Et moi je lui serai, dit le Seigneur, un mur de feu tout autour, et je serai dans la gloire au milieu d’elle.
6 “Tulukani! Tulukani! Thawaniko ku dziko la kumpoto,” akutero Yehova, “pakuti ndinakumwazirani ku mphepo zinayi zamlengalenga,” akutero Yehova.
Ah! ah! fuyez de la terre de l’aquilon, dit le Seigneur; parce que vers les quatre vents du ciel, je vous ai dispersés, dit le Seigneur.
7 “Tuluka, iwe Ziyoni! Thawa, iwe amene umakhala mʼdziko la mwana wamkazi wa Babuloni!”
Fuis, ô Sion, qui habites chez la fille de Babylone.
8 Pakuti Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Atatha kundilemekeza wanditumiza kwa anthu a mitundu ina amene anakufunkhani; pakuti aliyense wokhudza inu wakhudza mwanadiso wanga.
Parce que voici ce que dit le Seigneur des armées: Après la gloire établie au milieu de vous, il m’a envoyé vers les nations qui vous ont dépouillés; car celui qui vous touche, touche la prunelle de mon œil.
9 Ndithu Ine ndidzawamenya anthuwo ndi dzanja langa ndipo amene anali akapolo awo ndiye adzawalande zinthu. Pamenepo mudzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse ndiye wandituma.
Parce que voici que je lève ma main sur eux, et ils seront la proie de ceux qui étaient leurs esclaves; et vous reconnaîtrez que c’est le Seigneur des armées qui m’a envoyé.
10 “Iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, fuwula ndipo sangalala. Pakuti taona ndikubwera, ndipo ndidzakhala pakati pako,” akutero Yehova.
Loue le Seigneur, et réjouis-toi, fille de Sion; car voici que je viens moi-même, et que j’habiterai au milieu de toi, dit le Seigneur.
11 “Nthawi imeneyo anthu a mitundu yambiri adzabwera kwa Yehova ndipo adzasanduka anthu anga. Ndidzakhala pakati pako ndipo iwe udzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse wandituma kwa iwe.
Et beaucoup de nations s’attacheront au Seigneur en ce jour; et elles seront mon peuple, et j’habiterai au milieu de toi; et tu sauras que le Seigneur des armées m’a envoyé vers toi.
12 Yehova adzachititsa kuti Yuda akhale chuma chake mʼdziko lopatulika ndipo adzasankhanso Yerusalemu.
Et le Seigneur possédera Juda comme son partage dans la terre sainte, et il choisira encore Jérusalem.
13 Khalani chete pamaso pa Yehova anthu nonse, chifukwa Iye wavumbuluka kuchoka ku malo ake opatulika.”
Que toute chair soit en silence devant la face du Seigneur; parce qu’il s’est réveillé du milieu de son habitacle saint