< Zekariya 2 >
1 Kenaka ndinayangʼananso, ndipo ndinaona munthu atanyamula chingwe choyezera mʼmanja mwake.
Je levai les yeux et je vis: Et voici un homme ayant à la main un cordeau à mesurer.
2 Ndipo ndinafunsa kuti, “Kodi ukupita kuti?” Anandiyankha kuti, “Akukayeza Yerusalemu kuti ndidziwe mulifupi mwake ndi mulitali mwake.”
Et je dis: « Où vas-tu? » Et il me dit: « Je vais mesurer Jérusalem pour voir quelle en doit être la largeur et quelle en doit être la longueur. »
3 Taonani, mngelo amene amayankhula nane uja akuchoka, mngelo wina anabwera kudzakumana naye
Et voici que parut l’ange qui parlait avec moi; et un autre ange apparut, allant à sa rencontre;
4 ndipo anamuwuza kuti, “Thamanga, kamuwuze mnyamatayo kuti, ‘Yerusalemu udzakhala mzinda wopanda malinga chifukwa mudzakhala anthu ambiri ndiponso ziweto zochuluka.
et il lui dit: « Cours! Parle à ce jeune homme en ces termes: C’est comme une ville ouverte que sera habitée Jérusalem, tant il y aura en son sein d’hommes et de bêtes.
5 Ndipo Ine mwini ndidzakhala linga lamoto kuteteza mzindawo,’ akutero Yehova, ‘ndipo ndidzakhala ulemerero mʼkati mwake.’
Et moi, je serai pour elle, — oracle de Yahweh, — une muraille de feu à l’entour, et je serai en gloire au milieu d’elle.
6 “Tulukani! Tulukani! Thawaniko ku dziko la kumpoto,” akutero Yehova, “pakuti ndinakumwazirani ku mphepo zinayi zamlengalenga,” akutero Yehova.
Holà! Holà! Fuyez du pays du septentrion, — oracle de Yahweh, car je vous ai dispersés aux quatre vents du ciel, — oracle de Yahweh.
7 “Tuluka, iwe Ziyoni! Thawa, iwe amene umakhala mʼdziko la mwana wamkazi wa Babuloni!”
Holà! Sion, sauve-toi, toi qui habites chez la fille de Babylone!
8 Pakuti Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Atatha kundilemekeza wanditumiza kwa anthu a mitundu ina amene anakufunkhani; pakuti aliyense wokhudza inu wakhudza mwanadiso wanga.
Car ainsi parle Yahweh des armées: Pour sa gloire il m’a envoyé vers les nations qui vous ont pillés; car qui vous touche touche la prunelle de son œil.
9 Ndithu Ine ndidzawamenya anthuwo ndi dzanja langa ndipo amene anali akapolo awo ndiye adzawalande zinthu. Pamenepo mudzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse ndiye wandituma.
Car voici que j’agite ma main sur elles, et elles seront un butin pour ceux qui leur sont asservis; et vous saurez que Yahweh des armées m’a envoyé.
10 “Iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, fuwula ndipo sangalala. Pakuti taona ndikubwera, ndipo ndidzakhala pakati pako,” akutero Yehova.
Pousse des cris de joie et sois dans l’allégresse, fille de Sion; car voici que je viens et j’habiterai au milieu de toi, — oracle de Yahweh.
11 “Nthawi imeneyo anthu a mitundu yambiri adzabwera kwa Yehova ndipo adzasanduka anthu anga. Ndidzakhala pakati pako ndipo iwe udzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse wandituma kwa iwe.
Beaucoup de nations s’attacheront à Yahweh en ce jour-là, et elles seront mon peuple; et j’habiterai au milieu de toi, et tu sauras que Yahweh des armées m’a envoyé vers toi.
12 Yehova adzachititsa kuti Yuda akhale chuma chake mʼdziko lopatulika ndipo adzasankhanso Yerusalemu.
Yahweh possédera Juda comme sa portion sur la terre sainte, et il choisira encore Jérusalem.
13 Khalani chete pamaso pa Yehova anthu nonse, chifukwa Iye wavumbuluka kuchoka ku malo ake opatulika.”
Que toute chair fasse silence devant Yahweh, car il s’est élevé de sa sainte demeure.