< Zekariya 2 >

1 Kenaka ndinayangʼananso, ndipo ndinaona munthu atanyamula chingwe choyezera mʼmanja mwake.
Je levai les yeux, et je vis, et voici, un homme qui tenait un cordeau à mesurer dans sa main.
2 Ndipo ndinafunsa kuti, “Kodi ukupita kuti?” Anandiyankha kuti, “Akukayeza Yerusalemu kuti ndidziwe mulifupi mwake ndi mulitali mwake.”
Alors je demandai: « Où vas-tu? » Il m'a dit: « Pour mesurer Jérusalem, pour voir quelle est sa largeur et quelle est sa longueur. »
3 Taonani, mngelo amene amayankhula nane uja akuchoka, mngelo wina anabwera kudzakumana naye
Voici que l'ange qui m'a parlé sort, et un autre ange va à sa rencontre,
4 ndipo anamuwuza kuti, “Thamanga, kamuwuze mnyamatayo kuti, ‘Yerusalemu udzakhala mzinda wopanda malinga chifukwa mudzakhala anthu ambiri ndiponso ziweto zochuluka.
et lui dit: « Cours, parle à ce jeune homme, en disant: 'Jérusalem sera habitée comme des villages sans murs, à cause de la multitude d'hommes et de bêtes qui s'y trouvent.
5 Ndipo Ine mwini ndidzakhala linga lamoto kuteteza mzindawo,’ akutero Yehova, ‘ndipo ndidzakhala ulemerero mʼkati mwake.’
Car moi, dit Yahvé, je serai pour elle une muraille de feu tout autour, et je serai la gloire au milieu d'elle.
6 “Tulukani! Tulukani! Thawaniko ku dziko la kumpoto,” akutero Yehova, “pakuti ndinakumwazirani ku mphepo zinayi zamlengalenga,” akutero Yehova.
Viens! Venez! Fuyez du pays du nord, dit Yahvé, car je vous ai dispersés comme les quatre vents du ciel, dit Yahvé.
7 “Tuluka, iwe Ziyoni! Thawa, iwe amene umakhala mʼdziko la mwana wamkazi wa Babuloni!”
« Viens, Sion! Fuis, toi qui habites avec la fille de Babylone!
8 Pakuti Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Atatha kundilemekeza wanditumiza kwa anthu a mitundu ina amene anakufunkhani; pakuti aliyense wokhudza inu wakhudza mwanadiso wanga.
Car Yahvé des armées dit: « C'est pour l'honneur qu'il m'a envoyé vers les nations qui t'ont pillée, car celui qui te touche touche la prunelle de ses yeux.
9 Ndithu Ine ndidzawamenya anthuwo ndi dzanja langa ndipo amene anali akapolo awo ndiye adzawalande zinthu. Pamenepo mudzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse ndiye wandituma.
Car voici, j'agiterai ma main sur elles, et elles seront un butin pour ceux qui les ont servies; et vous saurez que l'Éternel des armées m'a envoyé.
10 “Iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, fuwula ndipo sangalala. Pakuti taona ndikubwera, ndipo ndidzakhala pakati pako,” akutero Yehova.
Chante et réjouis-toi, fille de Sion! Car voici, je viens et j'habiterai au milieu de toi, dit Yahvé.
11 “Nthawi imeneyo anthu a mitundu yambiri adzabwera kwa Yehova ndipo adzasanduka anthu anga. Ndidzakhala pakati pako ndipo iwe udzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse wandituma kwa iwe.
En ce jour-là, des nations nombreuses se joindront à Yahvé et seront mon peuple; j'habiterai au milieu de vous, et vous saurez que Yahvé des armées m'a envoyé vers vous.
12 Yehova adzachititsa kuti Yuda akhale chuma chake mʼdziko lopatulika ndipo adzasankhanso Yerusalemu.
L'Éternel fera de Juda sa part dans la terre sainte, et il choisira de nouveau Jérusalem.
13 Khalani chete pamaso pa Yehova anthu nonse, chifukwa Iye wavumbuluka kuchoka ku malo ake opatulika.”
Silence, toute chair, devant l'Éternel, car il s'est réveillé de sa demeure sainte! »

< Zekariya 2 >