< Zekariya 2 >

1 Kenaka ndinayangʼananso, ndipo ndinaona munthu atanyamula chingwe choyezera mʼmanja mwake.
Og jeg opløftede mine Øjne og saa, og se, en Mand og en Maalesnor i hans Haand!
2 Ndipo ndinafunsa kuti, “Kodi ukupita kuti?” Anandiyankha kuti, “Akukayeza Yerusalemu kuti ndidziwe mulifupi mwake ndi mulitali mwake.”
Og jeg sagde: Hvor gaar du hen? og han sagde til mig: Hen at maale Jerusalem for at se, hvor stor dens Bredde, og hvor stor dens Længde er.
3 Taonani, mngelo amene amayankhula nane uja akuchoka, mngelo wina anabwera kudzakumana naye
Og se, Engelen, som talte med mig, gik ud, og en anden Engel gik ud imod ham.
4 ndipo anamuwuza kuti, “Thamanga, kamuwuze mnyamatayo kuti, ‘Yerusalemu udzakhala mzinda wopanda malinga chifukwa mudzakhala anthu ambiri ndiponso ziweto zochuluka.
Og han sagde til ham: Løb, tal til denne unge Karl, og sig: Jerusalem skal ligge som aabne Byer, formedelst den Mangfoldighed af Mennesker og Kvæg, som er midt i den.
5 Ndipo Ine mwini ndidzakhala linga lamoto kuteteza mzindawo,’ akutero Yehova, ‘ndipo ndidzakhala ulemerero mʼkati mwake.’
Og jeg, jeg vil være den en Ildmur trindt omkring, siger Herren, og jeg vil være til Herlighed midt i den.
6 “Tulukani! Tulukani! Thawaniko ku dziko la kumpoto,” akutero Yehova, “pakuti ndinakumwazirani ku mphepo zinayi zamlengalenga,” akutero Yehova.
Ve! ve! flyr da ud af Nordens Land, siger Herren; thi som Himmelens fire Vejr har jeg udbredet eder, siger Herren.
7 “Tuluka, iwe Ziyoni! Thawa, iwe amene umakhala mʼdziko la mwana wamkazi wa Babuloni!”
Ve! Zion, red dig, du, som bor hos Babels Datter!
8 Pakuti Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Atatha kundilemekeza wanditumiza kwa anthu a mitundu ina amene anakufunkhani; pakuti aliyense wokhudza inu wakhudza mwanadiso wanga.
Thi saa siger den Herre Zebaoth, at han har sendt mig efter Ære ud til Hedningerne, som plyndrede eder; thi den, som rører ved eder, rører ved hans Øjesten.
9 Ndithu Ine ndidzawamenya anthuwo ndi dzanja langa ndipo amene anali akapolo awo ndiye adzawalande zinthu. Pamenepo mudzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse ndiye wandituma.
Thi se, jeg svinger min Haand over dem, og de skulle blive et Bytte for dem, som tjente dem; og I skulle fornemme, at den Herre Zebaoth har sendt mig.
10 “Iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, fuwula ndipo sangalala. Pakuti taona ndikubwera, ndipo ndidzakhala pakati pako,” akutero Yehova.
Syng og vær glad, du Zions Datter! thi se, jeg kommer og vil bo i din Midte, siger Herren.
11 “Nthawi imeneyo anthu a mitundu yambiri adzabwera kwa Yehova ndipo adzasanduka anthu anga. Ndidzakhala pakati pako ndipo iwe udzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse wandituma kwa iwe.
Og mange Hedningefolk skulle slutte sig til Herren paa den Dag, og de skulle blive mig et Folk, og jeg vil bo i din Midte, og du skal fornemme, at den Herre Zebaoth har sendt mig til dig.
12 Yehova adzachititsa kuti Yuda akhale chuma chake mʼdziko lopatulika ndipo adzasankhanso Yerusalemu.
Og Herren skal tage Juda som sin Del til Eje paa den hellige Jordbund, og han skal fremdeles udvælge Jerusalem.
13 Khalani chete pamaso pa Yehova anthu nonse, chifukwa Iye wavumbuluka kuchoka ku malo ake opatulika.”
Stille, alt Kød, for Herrens Ansigt; thi han har rejst sig fra sin hellige Bolig.

< Zekariya 2 >