< Zekariya 14 >
1 Taonani tsiku la Yehova likubwera pamene zinthu zimene adani ako anakulanda azidzagawana iwe ukuona.
»Poglej, dan Gospodov prihaja in tvoj plen bo razdeljen v tvoji sredi.
2 Ndidzasonkhanitsa anthu a mitundu yonse kuti adzathire nkhondo Yerusalemu; mzindawu udzalandidwa, nyumba zidzaphwasulidwa, ndipo akazi adzagwiriridwa. Theka la anthu a mu mzindamu lidzapita ku ukapolo, koma ena onse otsala mu mzindamu sadzachotsedwa.
Kajti vse narode bom zbral, da se borijo zoper Jeruzalem. Mesto bo zavzeto, hiše oplenjene in ženske posiljene. Polovica mesta bo odšla v ujetništvo, preostanek ljudstva pa ne bo iztrebljen iz mesta.«
3 Pamenepo Yehova adzabwera kudzamenyana ndi mitundu ya anthu imeneyi, ngati mmene amachitira pa nthawi ya nkhondo.
Takrat bo prišel Gospod in se boril zoper te narode, kakor ko se je boril na dan bitke.
4 Tsiku limenelo adzayimirira pa Phiri la Olivi, kummawa kwa Yerusalemu, ndipo Phiri la Olivilo lidzagawikana pawiri kuyambira kummawa mpaka kumadzulo, kupanga chigwa chachikulu, kuchititsa kuti theka la phiri lisunthire kumpoto ndi linalo kummwera.
Na tisti dan bodo njegova stopala stopila na Oljsko goro, ki je na vzhodu, pred Jeruzalemom in Oljska gora se bo razklala po sredi proti vzhodu in proti zahodu in tam bo zelo velika dolina. Polovica gore bo odstranjena proti severu, polovica pa proti jugu.
5 Inu mudzathawa podzera mʼchigwa chapakati pa phirilo, pakuti chidzafika mpaka ku Azeli. Mudzathawa monga munachitira pa tsiku la chivomerezi nthawi ya Uziya mfumu ya Yuda. Kenaka Yehova Mulungu wanga adzabwera, pamodzi ndi oyera ake onse.
Bežali boste k dolini [med] gorama, kajti dolina [med] gorama bo segala do Azela. Da, bežali boste, podobno kakor ste bežali pred potresom v dneh Judovega kralja Uzíjaha. In Gospod, moj Bog, bo prišel in vsi sveti [bodo] s teboj.
6 Tsiku limenelo sipadzakhala kuwala, kuzizira kapena chisanu.
In zgodilo se bo na tisti dan, da svetloba ne bo razločna, niti tema,
7 Lidzakhala tsiku lapaderadera, silidzakhala usana kapena usiku; tsiku limeneli akulidziwa ndi Yehova yekha. Ikadzafika nthawi ya madzulo, kudzakhala kukuwalabe.
temveč bo en dan, ki bo poznan Gospodu, niti dan, niti noč, temveč se bo zgodilo, da bo ob večernem času svetloba.
8 Tsiku limenelo madzi amoyo adzatuluka mu Yerusalemu, theka lidzapita ku nyanja ya kummawa ndipo theka lina ku nyanja ya kumadzulo, nthawi yachilimwe ndi nthawi yozizira yomwe.
In to bo na tisti dan, da bodo žive vode izšle iz Jeruzalema. Polovica izmed njih proti prvemu morju in polovica proti zadnjemu morju. To bo poleti in pozimi.
9 Ndipo Yehova adzakhala mfumu pa dziko lonse lapansi. Tsiku limenelo padzakhala Ambuye mmodzi yekha, ndipo dzina lidzakhala limodzi lomwelo.
In Gospod bo kralj nad vso zemljo. Na tisti dan bo en Gospod in njegovo ime eno.
10 Dziko lonse, kuyambira ku Geba mpaka ku Rimoni, kummwera kwa Yerusalemu, lidzakhala ngati Araba. Koma Yerusalemu adzakwezedwa ndipo adzakhala pamalo pakepo, kuyambira ku Chipata cha Benjamini mpaka ku malo amene ali ku Chipata Choyamba, ku Chipata Chapangodya, ndipo kuyambira ku Nsanja ya Hananeli mpaka ku malo opsinyira mphesa za mfumu.
Vsa dežela bo narejena kakor ravnina od Gebe do Rimóna, južno od Jeruzalema, in ta bo dvignjen in naseljen na svojem kraju, od Benjaminovih velikih vrat, do mesta prvih velikih vrat, do Vogalnih velikih vrat in od Hananélovega stolpa do kraljevih vinskih stiskalnic.
11 Mʼmenemo mudzakhala anthu; sadzawonongedwanso. Yerusalemu adzakhala pa mtendere.
V njem bodo prebivali ljudje in tam ne bo več skrajnega uničenja, temveč bo Jeruzalem varno naseljen.
12 Mliri umene Yehova adzakanthire nawo mitundu yonse ya anthu imene inkamenyana ndi Yerusalemu ndi uwu: Matupi awo adzawola iwo eni akuyenda, maso awo adzawola ali mʼmalo mwake, ndipo malilime awo adzawola ali mʼkamwa mwawo.
To pa bo kuga, s katero bo Gospod udaril vsa ljudstva, ki so se borila zoper Jeruzalem. Njihovo meso bo zgnilo, medtem ko stojijo na svojih stopalih in njihove oči bodo zgnile v njihovih jamicah in njihov jezik bo zgnil v njihovih ustih.
13 Pa tsiku limenelo Yehova adzasokoneza anthu akuluakulu. Munthu aliyense adzagwira dzanja la mnzake, ndi kuyamba kumenyana okhaokha.
Na tisti dan se bo zgodilo, da bo med njimi velika zmešnjava od Gospoda, in vsakdo bo zgrabil roko svojega soseda in svojo roko bo vzdignil zoper roko svojega soseda.
14 Yuda nayenso adzachita nkhondo ku Yerusalemu. Chuma chonse cha anthu a mitundu yozungulira adzachisonkhanitsa pamodzi; golide, siliva ndi zovala zochuluka kwambiri.
Tudi Juda se bo bojeval v Jeruzalemu in premoženje vseh poganov naokoli se bo zbralo skupaj, zlata, srebra in oblačil v velikem obilju.
15 Mliri womwewo udzapha akavalo ndi nyulu, ngamira ndi abulu, pamodzi ndi nyama zonse zokhala ku misasako.
Kakor ta kuga, takšna bo kuga konja, mule, kamele, osla in vseh živali, ki bodo v teh šotoriščih.
16 Kenaka opulumuka ochokera mwa mitundu yonse ya anthu amene anathira nkhondo Yerusalemu, azidzapita chaka ndi chaka kukapembedza Mfumu Yehova Wamphamvuzonse, ndiponso kukachita Chikondwerero cha Misasa.
Zgodilo se bo, da kdor preostane izmed vseh narodov, ki so prišli zoper Jeruzalem, bo torej hodil gor iz leta v leto, da obožuje kralja, Gospoda nad bojevniki in da praznuje šotorski praznik.
17 Ngati mitundu ina ya anthu pa dziko lapansi sidzapita ku Yerusalemu kukapembedza Mfumu Yehova Wamphamvuzonse, idzakhala wopanda mvula.
In zgodilo se bo, da kdorkoli, izmed vseh družin zemlje, ne bo prišel gor v Jeruzalem, da obožuje Kralja, Gospoda nad bojevniki, celo nad njim ne bo dežja.
18 Ndipo ngati anthu a ku Igupto sadzapita ndi kukakhala nawo kumeneko, adzakhala wopanda mvula. Yehova adzabweretsa pa iwo mliri umene analangira mitundu ina ya anthu imene sinapite ku Chikondwerero cha Misasa.
In če družina iz Egipta ne gre gor in ne pride, da tam ni dežja, bo tam kuga, s katero bo Gospod udaril pogane, ki ne pridejo gor, da praznujejo šotorski praznik.
19 Chimenechi chidzakhala chilango cha Igupto ndiponso mitundu ina yonse imene sidzapita ku Chikondwerero cha Misasa.
To bo kazen Egiptu in kazen vsem narodom, ki ne pridejo gor, da praznujejo šotorski praznik.
20 Pa tsiku limenelo pa maberu a akavalo padzalembedwa mawu oti wopatulikira Yehova, ndipo miphika ya mʼNyumba ya Yehova idzakhala yopatulika ngati mbale za ku guwa.
Na tisti dan bo na konjskih zvončkih SVETO Gospodu in lonci v Gospodovi hiši bodo podobni skledicam pred oltarjem.
21 Mʼphika uliwonse ku Yerusalemu ndi ku Yuda udzakhala wopatulikira Yehova Wamphamvuzonse, ndipo onse amene adzabwera kudzapereka nsembe adzatenga miphika ina ndi kuphikiramo. Ndipo nthawi imeneyo simudzakhalanso Akanaani mʼNyumba ya Yehova Wamphamvuzonse.
Da, vsak lonec v Jeruzalemu in v Judeji bo svetost Gospodu nad bojevniki. Vsi tisti, ki žrtvujejo, bodo prišli in jemali iz njih in kuhali v njih. Na tisti dan ne bo več Kánaancev v hiši Gospoda nad bojevniki.