< Zekariya 14 >
1 Taonani tsiku la Yehova likubwera pamene zinthu zimene adani ako anakulanda azidzagawana iwe ukuona.
Ево иде дан Господњи, и плен ће се твој разделити усред тебе.
2 Ndidzasonkhanitsa anthu a mitundu yonse kuti adzathire nkhondo Yerusalemu; mzindawu udzalandidwa, nyumba zidzaphwasulidwa, ndipo akazi adzagwiriridwa. Theka la anthu a mu mzindamu lidzapita ku ukapolo, koma ena onse otsala mu mzindamu sadzachotsedwa.
Јер ћу скупити све народе на Јерусалим у бој, и град ће се узети, и куће опленити и жене осрамотити и половина ће града отићи у ропство, а остали народ неће се истребити из града.
3 Pamenepo Yehova adzabwera kudzamenyana ndi mitundu ya anthu imeneyi, ngati mmene amachitira pa nthawi ya nkhondo.
Јер ће Господ изаћи, и војеваће на народе као што војује на дан кад је бој.
4 Tsiku limenelo adzayimirira pa Phiri la Olivi, kummawa kwa Yerusalemu, ndipo Phiri la Olivilo lidzagawikana pawiri kuyambira kummawa mpaka kumadzulo, kupanga chigwa chachikulu, kuchititsa kuti theka la phiri lisunthire kumpoto ndi linalo kummwera.
И ноге ће Његове стати у тај дан на гори Маслинској која је према Јерусалиму с истока, и гора ће се Маслинска распасти по среди на исток и на запад да ће бити продол врло велика, и половина ће горе уступити на север а половина на југ.
5 Inu mudzathawa podzera mʼchigwa chapakati pa phirilo, pakuti chidzafika mpaka ku Azeli. Mudzathawa monga munachitira pa tsiku la chivomerezi nthawi ya Uziya mfumu ya Yuda. Kenaka Yehova Mulungu wanga adzabwera, pamodzi ndi oyera ake onse.
И бежаћете у продол горску, јер ће продол горска допирати до Асала, и бежаћете као што бежасте од труса у време Озије, цара Јудиног; и доћи ће Господ Бог мој, и сви ће свети бити с тобом.
6 Tsiku limenelo sipadzakhala kuwala, kuzizira kapena chisanu.
И у тај дан неће бити видело светло и мрачно;
7 Lidzakhala tsiku lapaderadera, silidzakhala usana kapena usiku; tsiku limeneli akulidziwa ndi Yehova yekha. Ikadzafika nthawi ya madzulo, kudzakhala kukuwalabe.
Него ће бити један дан, који је познат Господу, неће бити дан и ноћ, јер ће и увече бити светлост.
8 Tsiku limenelo madzi amoyo adzatuluka mu Yerusalemu, theka lidzapita ku nyanja ya kummawa ndipo theka lina ku nyanja ya kumadzulo, nthawi yachilimwe ndi nthawi yozizira yomwe.
И у тај ће дан протећи из Јерусалима вода жива, пола к источном мору а пола к западном мору, и биће и лети и зими.
9 Ndipo Yehova adzakhala mfumu pa dziko lonse lapansi. Tsiku limenelo padzakhala Ambuye mmodzi yekha, ndipo dzina lidzakhala limodzi lomwelo.
И Господ ће бити цар над свом земљом, у онај дан биће Господ један и име Његово једно.
10 Dziko lonse, kuyambira ku Geba mpaka ku Rimoni, kummwera kwa Yerusalemu, lidzakhala ngati Araba. Koma Yerusalemu adzakwezedwa ndipo adzakhala pamalo pakepo, kuyambira ku Chipata cha Benjamini mpaka ku malo amene ali ku Chipata Choyamba, ku Chipata Chapangodya, ndipo kuyambira ku Nsanja ya Hananeli mpaka ku malo opsinyira mphesa za mfumu.
И сва ће се земља претворити у равницу од Гаваје до Римона с југа Јерусалиму, који ће се подигнути и населити на свом месту од врата Венијаминових до места где су прва врата, до врата на углу, и од куле Ананеилове до теска царевог.
11 Mʼmenemo mudzakhala anthu; sadzawonongedwanso. Yerusalemu adzakhala pa mtendere.
И они ће наставати у њему, и неће више бити проклетства, и Јерусалим ће стајати без страха.
12 Mliri umene Yehova adzakanthire nawo mitundu yonse ya anthu imene inkamenyana ndi Yerusalemu ndi uwu: Matupi awo adzawola iwo eni akuyenda, maso awo adzawola ali mʼmalo mwake, ndipo malilime awo adzawola ali mʼkamwa mwawo.
А ово ће бити зло којим ће Господ ударити све народе који би војевали на Јерусалим: тело ће сваком посахнути док још стоји на ногу, и очи ће сваком посахнути у рупама својим, и језик ће сваком посахнути у устима.
13 Pa tsiku limenelo Yehova adzasokoneza anthu akuluakulu. Munthu aliyense adzagwira dzanja la mnzake, ndi kuyamba kumenyana okhaokha.
И у то ће време бити велика сметња међу њима од Господа, и хватаће један другог за руку, и рука ће се једног подигнути на руку другог.
14 Yuda nayenso adzachita nkhondo ku Yerusalemu. Chuma chonse cha anthu a mitundu yozungulira adzachisonkhanitsa pamodzi; golide, siliva ndi zovala zochuluka kwambiri.
А и Јуда ће војевати на Јерусалим, и благо свих народа унаоколо сабраће се, злато и сребро и одело врло много.
15 Mliri womwewo udzapha akavalo ndi nyulu, ngamira ndi abulu, pamodzi ndi nyama zonse zokhala ku misasako.
И зло као то зло снаћи ће коње, мазге, камиле и магарце и сву стоку која буде у том логору.
16 Kenaka opulumuka ochokera mwa mitundu yonse ya anthu amene anathira nkhondo Yerusalemu, azidzapita chaka ndi chaka kukapembedza Mfumu Yehova Wamphamvuzonse, ndiponso kukachita Chikondwerero cha Misasa.
И ко год остане од свих народа који дођу на Јерусалим, свак ће долазити од године до године да се поклони цару Господу над војскама и да празнује празник сеница.
17 Ngati mitundu ina ya anthu pa dziko lapansi sidzapita ku Yerusalemu kukapembedza Mfumu Yehova Wamphamvuzonse, idzakhala wopanda mvula.
И ако које од племена земаљских не би дошло у Јерусалим да се поклони цару Господу над војскама, на њих неће бити дажда;
18 Ndipo ngati anthu a ku Igupto sadzapita ndi kukakhala nawo kumeneko, adzakhala wopanda mvula. Yehova adzabweretsa pa iwo mliri umene analangira mitundu ina ya anthu imene sinapite ku Chikondwerero cha Misasa.
И ако се племе мисирско не би подигло и дошло, на које не дажди, биће исто зло којим ће Господ ударити народе који не би долазили да празнују празник сеница.
19 Chimenechi chidzakhala chilango cha Igupto ndiponso mitundu ina yonse imene sidzapita ku Chikondwerero cha Misasa.
Такав ће бити грех Мисирцима и грех свим народима који не би долазили да празнују празник сеница.
20 Pa tsiku limenelo pa maberu a akavalo padzalembedwa mawu oti wopatulikira Yehova, ndipo miphika ya mʼNyumba ya Yehova idzakhala yopatulika ngati mbale za ku guwa.
У тај ће дан бити на звонцима коњским: Светиња Господу; и лонци ће у дому Господњем бити као зделе пред олтаром;
21 Mʼphika uliwonse ku Yerusalemu ndi ku Yuda udzakhala wopatulikira Yehova Wamphamvuzonse, ndipo onse amene adzabwera kudzapereka nsembe adzatenga miphika ina ndi kuphikiramo. Ndipo nthawi imeneyo simudzakhalanso Akanaani mʼNyumba ya Yehova Wamphamvuzonse.
И сви ће лонци у Јерусалиму и у Јуди бити светиња Господу над војскама, и сви који хоће да принесу жртву долазећи узимаће их и кувати у њима; и у тај дан неће више бити Хананејца у дому Господа над војскама.