< Zekariya 14 >

1 Taonani tsiku la Yehova likubwera pamene zinthu zimene adani ako anakulanda azidzagawana iwe ukuona.
Eis que um dia de Javé chega, quando seu saque será dividido dentro de você.
2 Ndidzasonkhanitsa anthu a mitundu yonse kuti adzathire nkhondo Yerusalemu; mzindawu udzalandidwa, nyumba zidzaphwasulidwa, ndipo akazi adzagwiriridwa. Theka la anthu a mu mzindamu lidzapita ku ukapolo, koma ena onse otsala mu mzindamu sadzachotsedwa.
Pois eu congregarei todas as nações contra Jerusalém para a batalha; e a cidade será tomada, as casas serão espingidas, e as mulheres arrebatadas. Metade da cidade sairá em cativeiro, e o resto do povo não será cortado da cidade.
3 Pamenepo Yehova adzabwera kudzamenyana ndi mitundu ya anthu imeneyi, ngati mmene amachitira pa nthawi ya nkhondo.
Então Yahweh sairá e lutará contra essas nações, como quando ele lutou no dia da batalha.
4 Tsiku limenelo adzayimirira pa Phiri la Olivi, kummawa kwa Yerusalemu, ndipo Phiri la Olivilo lidzagawikana pawiri kuyambira kummawa mpaka kumadzulo, kupanga chigwa chachikulu, kuchititsa kuti theka la phiri lisunthire kumpoto ndi linalo kummwera.
Seus pés estarão naquele dia no Monte das Oliveiras, que está diante de Jerusalém no leste; e o Monte das Oliveiras será dividido em dois de leste a oeste, formando um vale muito grande. Metade da montanha se moverá para o norte, e a outra metade para o sul.
5 Inu mudzathawa podzera mʼchigwa chapakati pa phirilo, pakuti chidzafika mpaka ku Azeli. Mudzathawa monga munachitira pa tsiku la chivomerezi nthawi ya Uziya mfumu ya Yuda. Kenaka Yehova Mulungu wanga adzabwera, pamodzi ndi oyera ake onse.
Você fugirá pelo vale de minhas montanhas, pois o vale das montanhas chegará até Azel. Sim, você fugirá, assim como fugiu antes do terremoto nos dias de Uzias, rei de Judá. Yahweh meu Deus virá, e todos os santos contigo.
6 Tsiku limenelo sipadzakhala kuwala, kuzizira kapena chisanu.
Acontecerá naquele dia que não haverá luz, frio ou geada.
7 Lidzakhala tsiku lapaderadera, silidzakhala usana kapena usiku; tsiku limeneli akulidziwa ndi Yehova yekha. Ikadzafika nthawi ya madzulo, kudzakhala kukuwalabe.
Será um dia único que é conhecido por Javé - não dia, e não noite; mas acontecerá que à noite haverá luz.
8 Tsiku limenelo madzi amoyo adzatuluka mu Yerusalemu, theka lidzapita ku nyanja ya kummawa ndipo theka lina ku nyanja ya kumadzulo, nthawi yachilimwe ndi nthawi yozizira yomwe.
Acontecerá nesse dia que águas vivas sairão de Jerusalém, metade delas em direção ao mar oriental, e a outra metade em direção ao mar ocidental. Será assim no verão e no inverno.
9 Ndipo Yehova adzakhala mfumu pa dziko lonse lapansi. Tsiku limenelo padzakhala Ambuye mmodzi yekha, ndipo dzina lidzakhala limodzi lomwelo.
Yahweh será Rei sobre toda a terra. Naquele dia Yahweh será um só, e seu nome será um só.
10 Dziko lonse, kuyambira ku Geba mpaka ku Rimoni, kummwera kwa Yerusalemu, lidzakhala ngati Araba. Koma Yerusalemu adzakwezedwa ndipo adzakhala pamalo pakepo, kuyambira ku Chipata cha Benjamini mpaka ku malo amene ali ku Chipata Choyamba, ku Chipata Chapangodya, ndipo kuyambira ku Nsanja ya Hananeli mpaka ku malo opsinyira mphesa za mfumu.
Toda a terra será feita como a Arabah, de Geba a Rimmon ao sul de Jerusalém; e ela será erguida e morará em seu lugar, do portão de Benjamin ao lugar do primeiro portão, ao portão da esquina, e da torre de Hananel às prensas de vinho do rei.
11 Mʼmenemo mudzakhala anthu; sadzawonongedwanso. Yerusalemu adzakhala pa mtendere.
Men habitará ali, e não haverá mais maldição; mas Jerusalém habitará em segurança.
12 Mliri umene Yehova adzakanthire nawo mitundu yonse ya anthu imene inkamenyana ndi Yerusalemu ndi uwu: Matupi awo adzawola iwo eni akuyenda, maso awo adzawola ali mʼmalo mwake, ndipo malilime awo adzawola ali mʼkamwa mwawo.
Esta será a praga com que Iavé atacará todos os povos que lutaram contra Jerusalém: sua carne consumirá enquanto estiverem de pé, e seus olhos consumirão em suas bases, e sua língua consumirá em sua boca.
13 Pa tsiku limenelo Yehova adzasokoneza anthu akuluakulu. Munthu aliyense adzagwira dzanja la mnzake, ndi kuyamba kumenyana okhaokha.
Acontecerá naquele dia que um grande pânico de Iavé estará entre eles; e cada um deles agarrará a mão de seu próximo, e sua mão se levantará contra a mão de seu vizinho.
14 Yuda nayenso adzachita nkhondo ku Yerusalemu. Chuma chonse cha anthu a mitundu yozungulira adzachisonkhanitsa pamodzi; golide, siliva ndi zovala zochuluka kwambiri.
Judá também lutará em Jerusalém; e as riquezas de todas as nações vizinhas serão reunidas: ouro, prata e roupas, em grande abundância.
15 Mliri womwewo udzapha akavalo ndi nyulu, ngamira ndi abulu, pamodzi ndi nyama zonse zokhala ku misasako.
Uma praga como esta cairá sobre o cavalo, sobre a mula, sobre o camelo, sobre o burro, e sobre todos os animais que estarão nesses acampamentos.
16 Kenaka opulumuka ochokera mwa mitundu yonse ya anthu amene anathira nkhondo Yerusalemu, azidzapita chaka ndi chaka kukapembedza Mfumu Yehova Wamphamvuzonse, ndiponso kukachita Chikondwerero cha Misasa.
Acontecerá que todos os que restarem de todas as nações que vieram contra Jerusalém subirão de ano para ano para adorar o Rei, Javé dos Exércitos, e para manter a festa dos estandes.
17 Ngati mitundu ina ya anthu pa dziko lapansi sidzapita ku Yerusalemu kukapembedza Mfumu Yehova Wamphamvuzonse, idzakhala wopanda mvula.
Será que quem de todas as famílias da terra não subir a Jerusalém para adorar o Rei, Javé dos Exércitos, sobre eles não haverá chuva.
18 Ndipo ngati anthu a ku Igupto sadzapita ndi kukakhala nawo kumeneko, adzakhala wopanda mvula. Yehova adzabweretsa pa iwo mliri umene analangira mitundu ina ya anthu imene sinapite ku Chikondwerero cha Misasa.
Se a família do Egito não subir e não vier, também não haverá chuva sobre eles. Esta será a praga com que Iavé atacará as nações que não subirem para manter a festa dos estandes.
19 Chimenechi chidzakhala chilango cha Igupto ndiponso mitundu ina yonse imene sidzapita ku Chikondwerero cha Misasa.
Esta será a punição do Egito e a punição de todas as nações que não subirem para manter a festa das cabines.
20 Pa tsiku limenelo pa maberu a akavalo padzalembedwa mawu oti wopatulikira Yehova, ndipo miphika ya mʼNyumba ya Yehova idzakhala yopatulika ngati mbale za ku guwa.
Naquele dia serão inscritos nos sinos dos cavalos, “SANTOS A Jeová”; e as panelas da casa de Yahweh serão como as tigelas diante do altar.
21 Mʼphika uliwonse ku Yerusalemu ndi ku Yuda udzakhala wopatulikira Yehova Wamphamvuzonse, ndipo onse amene adzabwera kudzapereka nsembe adzatenga miphika ina ndi kuphikiramo. Ndipo nthawi imeneyo simudzakhalanso Akanaani mʼNyumba ya Yehova Wamphamvuzonse.
Yes, todas as panelas em Jerusalém e em Judá serão sagradas para Iavé dos Exércitos; e todos aqueles que sacrificarem virão e tomarão delas, e cozinharão nelas. Naquele dia não haverá mais um cananeu na casa de Yahweh dos Exércitos.

< Zekariya 14 >