< Zekariya 14 >

1 Taonani tsiku la Yehova likubwera pamene zinthu zimene adani ako anakulanda azidzagawana iwe ukuona.
Watch out! For the day of the Lord is coming when what has been plundered from you will be divided up right in front of you.
2 Ndidzasonkhanitsa anthu a mitundu yonse kuti adzathire nkhondo Yerusalemu; mzindawu udzalandidwa, nyumba zidzaphwasulidwa, ndipo akazi adzagwiriridwa. Theka la anthu a mu mzindamu lidzapita ku ukapolo, koma ena onse otsala mu mzindamu sadzachotsedwa.
I will bring together all the nations to attack Jerusalem. The city will be captured, the houses looted, and the women raped. Half the population will be taken into exile, but the rest of the people will not be removed from the city.
3 Pamenepo Yehova adzabwera kudzamenyana ndi mitundu ya anthu imeneyi, ngati mmene amachitira pa nthawi ya nkhondo.
Then the Lord will go out to fight against the nations as he fights in times of war.
4 Tsiku limenelo adzayimirira pa Phiri la Olivi, kummawa kwa Yerusalemu, ndipo Phiri la Olivilo lidzagawikana pawiri kuyambira kummawa mpaka kumadzulo, kupanga chigwa chachikulu, kuchititsa kuti theka la phiri lisunthire kumpoto ndi linalo kummwera.
On that day his feet will stand on the Mount of Olives which faces Jerusalem to the east. The Mount of Olives will split apart, with half moving north and half moving south, creating a wide valley from east to west.
5 Inu mudzathawa podzera mʼchigwa chapakati pa phirilo, pakuti chidzafika mpaka ku Azeli. Mudzathawa monga munachitira pa tsiku la chivomerezi nthawi ya Uziya mfumu ya Yuda. Kenaka Yehova Mulungu wanga adzabwera, pamodzi ndi oyera ake onse.
You will run away through this mountain valley for it will reach as far as Azal. You will run away like people did at the time of the earthquake during the reign of Uzzah, king of Judah. Then the Lord will come, accompanied by all his holy ones.
6 Tsiku limenelo sipadzakhala kuwala, kuzizira kapena chisanu.
On that day there will be no longer cold and frost.
7 Lidzakhala tsiku lapaderadera, silidzakhala usana kapena usiku; tsiku limeneli akulidziwa ndi Yehova yekha. Ikadzafika nthawi ya madzulo, kudzakhala kukuwalabe.
It will be one continuous day (only the Lord knows how this could happen). It won't be day or night, because in the evening it will still be light.
8 Tsiku limenelo madzi amoyo adzatuluka mu Yerusalemu, theka lidzapita ku nyanja ya kummawa ndipo theka lina ku nyanja ya kumadzulo, nthawi yachilimwe ndi nthawi yozizira yomwe.
On that day living waters will flow out of Jerusalem, half of it going east to the Dead Sea and half going west to the Mediterranean Sea, flowing in summer and winter alike.
9 Ndipo Yehova adzakhala mfumu pa dziko lonse lapansi. Tsiku limenelo padzakhala Ambuye mmodzi yekha, ndipo dzina lidzakhala limodzi lomwelo.
The Lord will be king over all the earth. On that day there will be one true Lord, and his name the only one.
10 Dziko lonse, kuyambira ku Geba mpaka ku Rimoni, kummwera kwa Yerusalemu, lidzakhala ngati Araba. Koma Yerusalemu adzakwezedwa ndipo adzakhala pamalo pakepo, kuyambira ku Chipata cha Benjamini mpaka ku malo amene ali ku Chipata Choyamba, ku Chipata Chapangodya, ndipo kuyambira ku Nsanja ya Hananeli mpaka ku malo opsinyira mphesa za mfumu.
The whole land will be transformed into a plain, from Geba to Rimmon, south of Jerusalem. But Jerusalem will be raised up to where it was, and people will live there from the Benjamin Gate to where the old gate was, to the Corner Gate, and from the Tower of Hananel to the king's winepresses.
11 Mʼmenemo mudzakhala anthu; sadzawonongedwanso. Yerusalemu adzakhala pa mtendere.
It will be inhabited and never again condemned to destruction again—people will be able to live in safety in Jerusalem.
12 Mliri umene Yehova adzakanthire nawo mitundu yonse ya anthu imene inkamenyana ndi Yerusalemu ndi uwu: Matupi awo adzawola iwo eni akuyenda, maso awo adzawola ali mʼmalo mwake, ndipo malilime awo adzawola ali mʼkamwa mwawo.
This will be the plague that the Lord will use to strike all the nations that attacked Jerusalem. Their flesh shall rot while they are still standing on their feet; their eyes will rot in their sockets; their tongues will rot in their mouths.
13 Pa tsiku limenelo Yehova adzasokoneza anthu akuluakulu. Munthu aliyense adzagwira dzanja la mnzake, ndi kuyamba kumenyana okhaokha.
On that day the Lord will strike them with a terrible panic, and they will seize one another, and fight hand-to-hand.
14 Yuda nayenso adzachita nkhondo ku Yerusalemu. Chuma chonse cha anthu a mitundu yozungulira adzachisonkhanitsa pamodzi; golide, siliva ndi zovala zochuluka kwambiri.
Even Judah will fight in Jerusalem. The wealth of the surrounding nations shall be collected: lots of gold, silver, and clothes.
15 Mliri womwewo udzapha akavalo ndi nyulu, ngamira ndi abulu, pamodzi ndi nyama zonse zokhala ku misasako.
A similar plague will strike the horses, mules, camels, donkeys, and all other animals that may be in their camps.
16 Kenaka opulumuka ochokera mwa mitundu yonse ya anthu amene anathira nkhondo Yerusalemu, azidzapita chaka ndi chaka kukapembedza Mfumu Yehova Wamphamvuzonse, ndiponso kukachita Chikondwerero cha Misasa.
After this every one of the survivors from the nations that attacked Jerusalem will go there to worship the King, the Lord Almighty, and to celebrate the Festival of Shelters.
17 Ngati mitundu ina ya anthu pa dziko lapansi sidzapita ku Yerusalemu kukapembedza Mfumu Yehova Wamphamvuzonse, idzakhala wopanda mvula.
If any of the peoples of the world refuse to go to Jerusalem to worship the King, the Lord Almighty, they will have no rain.
18 Ndipo ngati anthu a ku Igupto sadzapita ndi kukakhala nawo kumeneko, adzakhala wopanda mvula. Yehova adzabweretsa pa iwo mliri umene analangira mitundu ina ya anthu imene sinapite ku Chikondwerero cha Misasa.
If the Egyptian people refuse to go and attend, then the Lord will inflict on them the same plague as on the other nations who will not go celebrate the Festival of Shelters.
19 Chimenechi chidzakhala chilango cha Igupto ndiponso mitundu ina yonse imene sidzapita ku Chikondwerero cha Misasa.
This will be the punishment on Egypt and all the nations if they do not go to Jerusalem and celebrate.
20 Pa tsiku limenelo pa maberu a akavalo padzalembedwa mawu oti wopatulikira Yehova, ndipo miphika ya mʼNyumba ya Yehova idzakhala yopatulika ngati mbale za ku guwa.
On that day the bells worn by horses will be engraved with the words “Holy to the Lord.” The household cooking pots used in the Lord's Temple will be as holy as the bowls used on the altar in the presence of the Lord.
21 Mʼphika uliwonse ku Yerusalemu ndi ku Yuda udzakhala wopatulikira Yehova Wamphamvuzonse, ndipo onse amene adzabwera kudzapereka nsembe adzatenga miphika ina ndi kuphikiramo. Ndipo nthawi imeneyo simudzakhalanso Akanaani mʼNyumba ya Yehova Wamphamvuzonse.
Every pot in Jerusalem and in Judah will be holy to the Lord Almighty, so that everyone who comes to sacrifice can take them and cook their sacrificial meat in them. On that day there will no longer be traders in the Lord's Temple.

< Zekariya 14 >