< Zekariya 14 >

1 Taonani tsiku la Yehova likubwera pamene zinthu zimene adani ako anakulanda azidzagawana iwe ukuona.
Behold the days of the Lord shall come, and thy spoils shall be divided in the midst of thee.
2 Ndidzasonkhanitsa anthu a mitundu yonse kuti adzathire nkhondo Yerusalemu; mzindawu udzalandidwa, nyumba zidzaphwasulidwa, ndipo akazi adzagwiriridwa. Theka la anthu a mu mzindamu lidzapita ku ukapolo, koma ena onse otsala mu mzindamu sadzachotsedwa.
And I will gather all nations to Jerusalem to battle, and the city shall be taken, and the houses shall be rifled, and the women shall be defiled: and half of the city shall go forth into captivity, and the rest of the people shall not be taken away out of the city.
3 Pamenepo Yehova adzabwera kudzamenyana ndi mitundu ya anthu imeneyi, ngati mmene amachitira pa nthawi ya nkhondo.
Then the Lord shall go forth, and shall fight against those nations, as when he fought in the day of battle.
4 Tsiku limenelo adzayimirira pa Phiri la Olivi, kummawa kwa Yerusalemu, ndipo Phiri la Olivilo lidzagawikana pawiri kuyambira kummawa mpaka kumadzulo, kupanga chigwa chachikulu, kuchititsa kuti theka la phiri lisunthire kumpoto ndi linalo kummwera.
And his feet shall stand in that day upon the mount of Olives, which is over against Jerusalem toward the east: and the mount of Olives shall be divided in the midst thereof to the east, and to the west with a very great opening, and half of the mountain shall be separated to the north, and half thereof to the south.
5 Inu mudzathawa podzera mʼchigwa chapakati pa phirilo, pakuti chidzafika mpaka ku Azeli. Mudzathawa monga munachitira pa tsiku la chivomerezi nthawi ya Uziya mfumu ya Yuda. Kenaka Yehova Mulungu wanga adzabwera, pamodzi ndi oyera ake onse.
And you shall flee to the valley of those mountains, for the valley of the mountains shall be joined even to the next, and you shall flee as you fled from the face of the earthquake in the days of Ozias king of Juda: and the Lord my God shall come, and all the saints with him.
6 Tsiku limenelo sipadzakhala kuwala, kuzizira kapena chisanu.
And it shall come to pass in that day, that there shall be no light, but cold and frost.
7 Lidzakhala tsiku lapaderadera, silidzakhala usana kapena usiku; tsiku limeneli akulidziwa ndi Yehova yekha. Ikadzafika nthawi ya madzulo, kudzakhala kukuwalabe.
And there shall be one day, which is known to the Lord, not day nor night: and in the time of the evening there shall be light.
8 Tsiku limenelo madzi amoyo adzatuluka mu Yerusalemu, theka lidzapita ku nyanja ya kummawa ndipo theka lina ku nyanja ya kumadzulo, nthawi yachilimwe ndi nthawi yozizira yomwe.
And it shall come to pass in that day, that living waters shall go out from Jerusalem: half of them to the east sea, and half of them to the last sea: they shall be in summer and in winter.
9 Ndipo Yehova adzakhala mfumu pa dziko lonse lapansi. Tsiku limenelo padzakhala Ambuye mmodzi yekha, ndipo dzina lidzakhala limodzi lomwelo.
And the Lord shall be king over all the earth: in that day there shall be one Lord, and his name shall be one.
10 Dziko lonse, kuyambira ku Geba mpaka ku Rimoni, kummwera kwa Yerusalemu, lidzakhala ngati Araba. Koma Yerusalemu adzakwezedwa ndipo adzakhala pamalo pakepo, kuyambira ku Chipata cha Benjamini mpaka ku malo amene ali ku Chipata Choyamba, ku Chipata Chapangodya, ndipo kuyambira ku Nsanja ya Hananeli mpaka ku malo opsinyira mphesa za mfumu.
And all the land shall return even to the desert, from the hill to Remmon to the south of Jerusalem: and she shall be exalted, and shall dwell in her own place, from the gate of Benjamin even to the place of the former gate, and even to the gate of the corners: and from the tower of Hananeel even to the king’s wine-presses.
11 Mʼmenemo mudzakhala anthu; sadzawonongedwanso. Yerusalemu adzakhala pa mtendere.
And people shall dwell in it, and there shall be no more an anathema: but Jerusalem shall sit secure.
12 Mliri umene Yehova adzakanthire nawo mitundu yonse ya anthu imene inkamenyana ndi Yerusalemu ndi uwu: Matupi awo adzawola iwo eni akuyenda, maso awo adzawola ali mʼmalo mwake, ndipo malilime awo adzawola ali mʼkamwa mwawo.
And this shall be the plague where with the Lord shall strike all nations that have fought against Jerusalem: the flesh of every one shall consume away while they stand upon their feet, and their eyes shall consume away in their holes, and their tongue shall consume away in their mouth.
13 Pa tsiku limenelo Yehova adzasokoneza anthu akuluakulu. Munthu aliyense adzagwira dzanja la mnzake, ndi kuyamba kumenyana okhaokha.
In that day there shall be a great tumult from the Lord among them: and a man shall take the hand of his neighbour, and his hand shall be clasped upon his neighbour’s hand.
14 Yuda nayenso adzachita nkhondo ku Yerusalemu. Chuma chonse cha anthu a mitundu yozungulira adzachisonkhanitsa pamodzi; golide, siliva ndi zovala zochuluka kwambiri.
And even Juda shall fight against Jerusalem: and the riches of all nations round about shall be gathered together, gold, and silver, and garments in great abundance.
15 Mliri womwewo udzapha akavalo ndi nyulu, ngamira ndi abulu, pamodzi ndi nyama zonse zokhala ku misasako.
And the destruction of the horse, and of the mule, and of the camel, and of the ass, and of all the beasts, that shall be in those tents, shall be like this destruction.
16 Kenaka opulumuka ochokera mwa mitundu yonse ya anthu amene anathira nkhondo Yerusalemu, azidzapita chaka ndi chaka kukapembedza Mfumu Yehova Wamphamvuzonse, ndiponso kukachita Chikondwerero cha Misasa.
And all they that shall be left of all nations that came against Jerusalem, shall go up from year to year, to adore the King, the Lord of hosts, and to keep the feast of tabernacles.
17 Ngati mitundu ina ya anthu pa dziko lapansi sidzapita ku Yerusalemu kukapembedza Mfumu Yehova Wamphamvuzonse, idzakhala wopanda mvula.
And it shall come to pass, that he that shall not go up of the families of the land to Jerusalem, to adore the King, the Lord of hosts, there shall be no rain upon them.
18 Ndipo ngati anthu a ku Igupto sadzapita ndi kukakhala nawo kumeneko, adzakhala wopanda mvula. Yehova adzabweretsa pa iwo mliri umene analangira mitundu ina ya anthu imene sinapite ku Chikondwerero cha Misasa.
And if the family of Egypt go not up nor come: neither shall it be upon them, but there shall be destruction wherewith the Lord will strike all nations that will not go up to keep the feast of tabernacles.
19 Chimenechi chidzakhala chilango cha Igupto ndiponso mitundu ina yonse imene sidzapita ku Chikondwerero cha Misasa.
This shall be the sin of Egypt, and this the sin of all nations, that will not go up to keep the feast of tabernacles.
20 Pa tsiku limenelo pa maberu a akavalo padzalembedwa mawu oti wopatulikira Yehova, ndipo miphika ya mʼNyumba ya Yehova idzakhala yopatulika ngati mbale za ku guwa.
In that day that which is upon the bridle of the horse shall be holy to the Lord: and the caldrons in the house of the Lord shall be as the phials before the altar.
21 Mʼphika uliwonse ku Yerusalemu ndi ku Yuda udzakhala wopatulikira Yehova Wamphamvuzonse, ndipo onse amene adzabwera kudzapereka nsembe adzatenga miphika ina ndi kuphikiramo. Ndipo nthawi imeneyo simudzakhalanso Akanaani mʼNyumba ya Yehova Wamphamvuzonse.
And every caldron in Jerusalem and Juda shall be sanctified to the Lord of hosts: and all that sacrifice shall come, and take of them, and shall seethe in them: and the merchant shall be no more in the house of the Lord of hosts in that day.

< Zekariya 14 >