< Zekariya 14 >

1 Taonani tsiku la Yehova likubwera pamene zinthu zimene adani ako anakulanda azidzagawana iwe ukuona.
Odiechiengʼ mar Jehova Nyasaye biro ma nopogie giu duto moyaki ka uneno.
2 Ndidzasonkhanitsa anthu a mitundu yonse kuti adzathire nkhondo Yerusalemu; mzindawu udzalandidwa, nyumba zidzaphwasulidwa, ndipo akazi adzagwiriridwa. Theka la anthu a mu mzindamu lidzapita ku ukapolo, koma ena onse otsala mu mzindamu sadzachotsedwa.
Abiro choko pinje duto mi akelgi Jerusalem mondo giked kode. Dala maduongʼ mar Jerusalem nokaw, udi manie iye noyaki, kendo mon noterruokgo githuon. Nus mar joma odak e dala maduongʼno noter e twech, to ji duto modongʼ ok nogol e dala.
3 Pamenepo Yehova adzabwera kudzamenyana ndi mitundu ya anthu imeneyi, ngati mmene amachitira pa nthawi ya nkhondo.
Eka Jehova Nyasaye nowuog oko kendo noked gi pinjego, kaka okedo e sa lweny.
4 Tsiku limenelo adzayimirira pa Phiri la Olivi, kummawa kwa Yerusalemu, ndipo Phiri la Olivilo lidzagawikana pawiri kuyambira kummawa mpaka kumadzulo, kupanga chigwa chachikulu, kuchititsa kuti theka la phiri lisunthire kumpoto ndi linalo kummwera.
Chiengʼno, Jehova Nyasaye nochungʼ ewi Got Zeituni mantiere yo wuok chiengʼ mar Jerusalem. To Got mar Zeituni-no nopogre nyadiriyo chakre wuok chiengʼ nyaka podho chiengʼ milos holo maduongʼ. Nus mar godno nomukre kochomo yo nyandwat, to nus machielo ochomo yo milambo.
5 Inu mudzathawa podzera mʼchigwa chapakati pa phirilo, pakuti chidzafika mpaka ku Azeli. Mudzathawa monga munachitira pa tsiku la chivomerezi nthawi ya Uziya mfumu ya Yuda. Kenaka Yehova Mulungu wanga adzabwera, pamodzi ndi oyera ake onse.
To unutony kuluwo holono, nikech enoyawre nyaka Azel. Unuring utony mana kaka ne uringo ka utony ne yiengni piny mane otimore ndalo loch Uzia ruodh Juda. Eka Jehova Nyasaye ma Nyasacha nobi, ka jomaler duto ni kode.
6 Tsiku limenelo sipadzakhala kuwala, kuzizira kapena chisanu.
Chiengʼno ler kata koyo kata ngʼich ok nobedie.
7 Lidzakhala tsiku lapaderadera, silidzakhala usana kapena usiku; tsiku limeneli akulidziwa ndi Yehova yekha. Ikadzafika nthawi ya madzulo, kudzakhala kukuwalabe.
Enobed odiechiengʼ ma kite yore, maonge gi odiechiengʼ kata otieno. En odiechiengʼ ma Jehova Nyasaye kende ema ongʼeyo kore. Sa monego piny imre ema ler mar chiengʼ nobedie.
8 Tsiku limenelo madzi amoyo adzatuluka mu Yerusalemu, theka lidzapita ku nyanja ya kummawa ndipo theka lina ku nyanja ya kumadzulo, nthawi yachilimwe ndi nthawi yozizira yomwe.
Chiengʼno pi makelo ngima nomol koa Jerusalem, ka nusne ochomo nam ma yo podho chiengʼ. Pigno nosik kamol kinde duto, ndalo oro kata ndalo chwiri.
9 Ndipo Yehova adzakhala mfumu pa dziko lonse lapansi. Tsiku limenelo padzakhala Ambuye mmodzi yekha, ndipo dzina lidzakhala limodzi lomwelo.
Jehova Nyasaye nobed gi loch e piny duto. Chiengʼno Jehova Nyasaye nobed achiel, kendo nyinge nobed achiel kende.
10 Dziko lonse, kuyambira ku Geba mpaka ku Rimoni, kummwera kwa Yerusalemu, lidzakhala ngati Araba. Koma Yerusalemu adzakwezedwa ndipo adzakhala pamalo pakepo, kuyambira ku Chipata cha Benjamini mpaka ku malo amene ali ku Chipata Choyamba, ku Chipata Chapangodya, ndipo kuyambira ku Nsanja ya Hananeli mpaka ku malo opsinyira mphesa za mfumu.
Piny duto, chakre Geba nyaka Rimon, yo milambo mar Jerusalem nobed machal gi Araba. To Jerusalem notingʼ malo, kendo enosik kama entie, chakre dhoranga Benjamin kidhi e Dhorangach Mokwongo nyaka e Dhorangach manie kona; kendo koa e ohinga mar Hananel ma gin kuonde biyo mzabibu mar ruoth.
11 Mʼmenemo mudzakhala anthu; sadzawonongedwanso. Yerusalemu adzakhala pa mtendere.
Ji nodag kanyo; ok nochak okethe kendo. Jerusalem nobed kama ji odakie gi kwe.
12 Mliri umene Yehova adzakanthire nawo mitundu yonse ya anthu imene inkamenyana ndi Yerusalemu ndi uwu: Matupi awo adzawola iwo eni akuyenda, maso awo adzawola ali mʼmalo mwake, ndipo malilime awo adzawola ali mʼkamwa mwawo.
Masira ma Jehova Nyasaye biro goyogo pinje duto mosebedo kakedo gi Jerusalem en ma: Ringregi biro tow ka gichungʼ, wengegi biro tow, kendo lewgi biro tow ei dhogi.
13 Pa tsiku limenelo Yehova adzasokoneza anthu akuluakulu. Munthu aliyense adzagwira dzanja la mnzake, ndi kuyamba kumenyana okhaokha.
Chiengʼno Jehova Nyasaye nogo ji gi kihondko maduongʼ. Ngʼato ka ngʼato nomak wadgi mondo ogorego.
14 Yuda nayenso adzachita nkhondo ku Yerusalemu. Chuma chonse cha anthu a mitundu yozungulira adzachisonkhanitsa pamodzi; golide, siliva ndi zovala zochuluka kwambiri.
Juda bende noked Jerusalem. Mwandu mag pinje duto molworo dalano nochoki, ma gin dhahabu, fedha kod lewni mogundho.
15 Mliri womwewo udzapha akavalo ndi nyulu, ngamira ndi abulu, pamodzi ndi nyama zonse zokhala ku misasako.
Masira machal kamano bende nogo farese, nyithi punde, ngamia, punde, kaachiel gi le duto ma noyudre e kembnigo.
16 Kenaka opulumuka ochokera mwa mitundu yonse ya anthu amene anathira nkhondo Yerusalemu, azidzapita chaka ndi chaka kukapembedza Mfumu Yehova Wamphamvuzonse, ndiponso kukachita Chikondwerero cha Misasa.
Eka joma otony moa e pinje duto mosemonjo Jerusalem nodhi e got zeituni higa ka higa mondo olam Ruoth Nyasaye, ma en Jehova Nyasaye Maratego, kendo mondo gitim Sawo mar Kiche.
17 Ngati mitundu ina ya anthu pa dziko lapansi sidzapita ku Yerusalemu kukapembedza Mfumu Yehova Wamphamvuzonse, idzakhala wopanda mvula.
Kapo ni moko kuom ogendini mag piny otamore dhi Jerusalem mondo olam Ruoth, ma en Jehova Nyasaye Maratego, to koth ok nochwenigi.
18 Ndipo ngati anthu a ku Igupto sadzapita ndi kukakhala nawo kumeneko, adzakhala wopanda mvula. Yehova adzabweretsa pa iwo mliri umene analangira mitundu ina ya anthu imene sinapite ku Chikondwerero cha Misasa.
Ka jo-Misri ok odhi e dalano to koth ok nochwenigi. Jehova Nyasaye nokel kuomgi kit masiche machal gi mago mane oketo kuom oganda mane ok dhi mondo otim Sawo mar Kiche.
19 Chimenechi chidzakhala chilango cha Igupto ndiponso mitundu ina yonse imene sidzapita ku Chikondwerero cha Misasa.
Ma e kum ma ibiro kumogo jo-Misri kod ogendini mamoko ma ok odhi Jerusalem mondo otim Sawo mar Kiche.
20 Pa tsiku limenelo pa maberu a akavalo padzalembedwa mawu oti wopatulikira Yehova, ndipo miphika ya mʼNyumba ya Yehova idzakhala yopatulika ngati mbale za ku guwa.
Chiengʼno okode motwe e ngʼut farese bende nondikie ni mowal ni Jehova Nyasaye kendo agulni mitedogo ei hekalu bende nowal ne tich Jehova Nyasaye mana ka tewni mitiyogo e kendo mar misango.
21 Mʼphika uliwonse ku Yerusalemu ndi ku Yuda udzakhala wopatulikira Yehova Wamphamvuzonse, ndipo onse amene adzabwera kudzapereka nsembe adzatenga miphika ina ndi kuphikiramo. Ndipo nthawi imeneyo simudzakhalanso Akanaani mʼNyumba ya Yehova Wamphamvuzonse.
Agulni duto man Jerusalem kod Juda nobed maler ni Jehova Nyasaye Maratego, kendo ji duto mabiro mondo otim misango nokaw agulnigo moko mi gitedie igi. To chiengʼno jo-Kanaan moro amora ok nobedi e od Jehova Nyasaye Maratego.

< Zekariya 14 >