< Zekariya 13 >
1 “Pa tsiku limenelo nyumba ya Davide adzayitsekulira kasupe wa madzi pamodzi ndi okhala mu Yerusalemu, kuti awachotsere tchimo lawo ndi chodetsa chawo.
En ce jour tout lieu sera ouvert à la maison de David et aux habitants de Jérusalem, pour le départ et la séparation.
2 “Pa tsiku limenelo, ndidzafafaniziratu mayina a mafano mʼdziko, ndipo sadzawakumbukiranso,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Ndidzachotsa mʼdziko aneneri pamodzi ndi mzimu wonyansa.
Et ce jour-là voici ce qui arrivera, dit le Seigneur Dieu des armées: J'effacerai les noms des idoles sur la terre, et il n'y aura plus de ces noms aucun souvenir; et J'exterminerai de la terre les faux prophètes et l'esprit immonde.
3 Ndipo ngati wina aliyense adzafuna kunenera, abambo ndi amayi ake amene anamubereka, adzamuwuza kuti, ‘Uyenera kufa, chifukwa wayankhula bodza mʼdzina la Yehova.’ Pamene anenera, makolo ake omwe adzamubaya.
Et voici ce qui arrivera: si un homme prophétise encore, son père et sa mère qui l'ont engendré lui diront: Tu mourras, parce que tu as dit des mensonges au Nom du Seigneur. Et son père et sa mère qui l'ont engendré l'empêcheront de prophétiser.
4 “Pa tsiku limenelo mneneri aliyense adzachita manyazi chifukwa cha masomphenya ake. Sadzavala chovala chake chaubweya ndi cholinga chonamiza anthu.
Et ce jour-là voici ce qui arrivera: les prophètes menteurs seront confondus, chacun par la vision même pour laquelle il aura prophétisé, et ils se ceindront de cilice de crin, parce qu'ils auront menti.
5 Iye adzati, ‘Sindine mneneri. Ndine mlimi; ndakhala ndi kulima munda kuyambira ubwana wanga.’
Et chacun d'eux dira: Je ne suis point prophète; je suis un homme travaillant la terre, et c'est un homme qui m'a donné le jour, et m'a ainsi élevé depuis ma jeunesse.
6 Ngati wina adzamufunsa, ‘Zilonda zili mʼthupi lakoli ndi chiyani?’ Iye adzayankha kuti, ‘Zilondazi ndinazilandira mʼnyumba ya abwenzi anga.’
Et Je lui dirai: Qu'est-ce que ces plaies que Tu as au milieu des mains? Et Il répondra: Ce sont les plaies que J'ai reçues dans une maison bien-aimée.
7 “Dzambatuka iwe lupanga, ukanthe mʼbusa wanga, ukanthe munthu amene ali pafupi ndi Ine!” akutero Yehova Wamphamvuzonse. Kantha mʼbusa ndipo nkhosa zidzabalalika, ndipo ndidzatambalitsa dzanja langa kuwononga zazingʼono.
Glaive, lève-toi contre Mes pasteurs et contre l'homme qui habite Ma ville, dit le Seigneur tout-puissant; frappez le berger, enlevez les brebis, et J'étendrai Ma main sur les petits.
8 Mʼdziko monse, akutero Yehova Wamphamvuzonse, “zigawo ziwiri mwa zigawo zitatu za anthu zidzakanthidwa ndi kuwonongeka; koma chigawo chimodzi chidzatsala mʼdzikomo.
Et voici ce qui arrivera sur toute la terre, dit le Seigneur: J'en exterminerai deux parts, elles périront; et la troisième part sera épargnée.
9 Chigawo chachitatuchi ndidzachiyika pa moto; ndidzawayeretsa monga momwe amayeretsera siliva ndi kuwayesa monga momwe amayesera golide. Adzayitana pa dzina langa ndipo Ine ndidzawayankha; Ine ndidzanena kuti, ‘Awa ndi anthu anga,’ ndipo iwo adzanena kuti, ‘Yehova ndiye Mulungu wathu.’”
Et Je ferai passer la troisième part dans la flamme, et Je la purifierai au feu, comme on purifie l'argent, et Je l'éprouverai comme on éprouve l'or. Elle invoquera Mon Nom, et Je l'exaucerai; et Je dirai: Voici Mon peuple; et elle dira: Le Seigneur est mon Dieu.