< Zekariya 13 >

1 “Pa tsiku limenelo nyumba ya Davide adzayitsekulira kasupe wa madzi pamodzi ndi okhala mu Yerusalemu, kuti awachotsere tchimo lawo ndi chodetsa chawo.
Paa hin Dag skal en Kilde vælde frem for Davids Hus og Jerusalems Indbyggere mod Synd og Urenhed.
2 “Pa tsiku limenelo, ndidzafafaniziratu mayina a mafano mʼdziko, ndipo sadzawakumbukiranso,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Ndidzachotsa mʼdziko aneneri pamodzi ndi mzimu wonyansa.
Og paa hin Dag, lyder det fra Hærskarers HERRE, udrydder jeg Afgudernes Navne af Landet, saa de ikke mer skal ihukommes; ogsaa Profeterne og Urenhedens Aand driver jeg ud af Landet.
3 Ndipo ngati wina aliyense adzafuna kunenera, abambo ndi amayi ake amene anamubereka, adzamuwuza kuti, ‘Uyenera kufa, chifukwa wayankhula bodza mʼdzina la Yehova.’ Pamene anenera, makolo ake omwe adzamubaya.
Naar nogen da atter profeterer, skal hans egne Forældre, hans Fader og Moder, sige til ham: »Du har forbrudt dit Liv, thi du har talt Løgn i HERRENS Navn.« Og hans egne Forældre, hans Fader og Moder, skal gennembore ham, naar han profeterer.
4 “Pa tsiku limenelo mneneri aliyense adzachita manyazi chifukwa cha masomphenya ake. Sadzavala chovala chake chaubweya ndi cholinga chonamiza anthu.
Paa hin Dag skal hver en Profet skamme sig over sine Syner, naar han profeterer, og han skal ikke klæde sig i laadden Kappe for at føre Folk bag Lyset,
5 Iye adzati, ‘Sindine mneneri. Ndine mlimi; ndakhala ndi kulima munda kuyambira ubwana wanga.’
men sige: »Jeg er ingen Profet; jeg er Bonde og har dyrket Jord fra min Ungdom.«
6 Ngati wina adzamufunsa, ‘Zilonda zili mʼthupi lakoli ndi chiyani?’ Iye adzayankha kuti, ‘Zilondazi ndinazilandira mʼnyumba ya abwenzi anga.’
Og spørger man ham: »Hvad er det for Saar paa dit Bryst?« skal han sige: »Dem fik jeg i mine Boleres Hus.«
7 “Dzambatuka iwe lupanga, ukanthe mʼbusa wanga, ukanthe munthu amene ali pafupi ndi Ine!” akutero Yehova Wamphamvuzonse. Kantha mʼbusa ndipo nkhosa zidzabalalika, ndipo ndidzatambalitsa dzanja langa kuwononga zazingʼono.
Frem, Sværd, imod min Hyrde, mod Manden, som staar mig nær, saa lyder det fra Hærskarers HERRE. Hyrden vil jeg slaa, saa Faarehjorden spredes; mod Drengene løfter jeg Haanden.
8 Mʼdziko monse, akutero Yehova Wamphamvuzonse, “zigawo ziwiri mwa zigawo zitatu za anthu zidzakanthidwa ndi kuwonongeka; koma chigawo chimodzi chidzatsala mʼdzikomo.
Og i hele Landet lyder det fra HERREN, skal to Tredjedele udryddes og udaande, men een Tredjedel skal levnes.
9 Chigawo chachitatuchi ndidzachiyika pa moto; ndidzawayeretsa monga momwe amayeretsera siliva ndi kuwayesa monga momwe amayesera golide. Adzayitana pa dzina langa ndipo Ine ndidzawayankha; Ine ndidzanena kuti, ‘Awa ndi anthu anga,’ ndipo iwo adzanena kuti, ‘Yehova ndiye Mulungu wathu.’”
Og denne Tredjedel fører jeg i Ild og renser den, som man renser Sølv, prøver den, som man prøver Guld. Den skal paakalde mit Navn, og jeg svarer; jeg siger: »Den er mit Folk.« Og den skal sige: »HERREN er min Gud.«

< Zekariya 13 >