< Zekariya 12 >
1 Uthenga wa Yehova kwa Israeli. Yehova, amene amayala mlengalenga, amene amayika maziko a dziko lapansi, ndiponso amene amalenga mzimu wokhala mwa munthu, akunena kuti,
Malheur accablant de la parole du Seigneur sur Israël. Le Seigneur qui a étendu le ciel, et fondé la terre, et formé l’esprit de l’homme en lui, dit:
2 “Taonani, ndidzasandutsa Yerusalemu kukhala chakumwa choledzeretsa chimene chidzasokoneza mitundu yonse ya anthu yomuzungulira. Yuda adzazingidwa pamodzinso ndi Yerusalemu.
Voici que moi je ferai de Jérusalem une porte d’enivrement pour tous les peuples d’alentour; mais Juda même sera pendant le siège contre Jérusalem.
3 Pa tsiku limenelo, pamene mitundu yonse ya anthu a dziko lapansi idzasonkhana kulimbana naye, ndidzasandutsa Yerusalemu thanthwe losatheka kusunthidwa ndi mitundu yonse ya anthu. Onse oyesa kumusuntha adzadzipweteka.
Et il arrivera qu’en ce jour-là je ferai de Jérusalem une pierre de poids pour tous les peuples; tous ceux qui la soulèveront seront meurtris et déchirés; et tous les royaumes de la terre s’assembleront contre elle.
4 Pa tsiku limenelo kavalo aliyense ndidzamuchititsa mantha kuti asokonezeke, ndipo wokwerapo wake ndidzamuchititsa misala,” akutero Yehova. “Ndidzayangʼanira nyumba ya Yuda koma ndidzachititsa khungu akavalo onse a anthu a mitundu ina.
En ce jour-là, dit le Seigneur, je frapperai de stupeur tous les chevaux, et ceux qui les montent de démence; et sur la maison de Juda j’ouvrirai mes yeux: tous les chevaux des peuples, je les frapperai de cécité.
5 Pamenepo atsogoleri a Yuda adzayankhula mʼmitima mwawo kuti, ‘Anthu a ku Yerusalemu ndi amphamvu, chifukwa Yehova Wamphamvuzonse ndiye Mulungu wawo.’
Et les chefs de Juda diront en leur cœur: Que les habitants de Jérusalem trouvent un appui pour moi dans le Seigneur des armées, leur Dieu.
6 “Pa tsiku limenelo ndidzasandutsa atsogoleri a Yuda kukhala ngati mbawula yotentha pakati pa nkhuni, ngati sakali yoyaka pa mitolo ya tirigu. Adzatentha mitundu yonse ya anthu yowazungulira, kumanja ndi kumanzere, koma Yerusalemu sadzasuntha pa malo ake.
En ce jour-là, je ferai des chefs de Juda comme un foyer de feu sous du bois, comme une torche de feu dans la paille; et ils dévoreront à droite et à gauche les peuples d’alentour, et Jérusalem sera de nouveau habitée en son propre lieu, à Jérusalem.
7 “Yehova adzapulumutsa malo okhala Yuda poyamba, kuti ulemu wa nyumba ya Davide ndi wa anthu okhala mu Yerusalemu usapambane ulemu wa Yuda.
Et le Seigneur sauvera les tabernacles de Juda comme au commencement; afin que la maison de David ne se glorifie point fastueusement, et que la gloire des habitants de Jérusalem ne s’élève pas contre Juda,
8 Pa tsiku limenelo Yehova adzatchinjiriza onse okhala mu Yerusalemu, kotero kuti anthu ofowoka kwambiri pakati pawo adzakhala ngati Davide, ndipo nyumba ya Davide idzakhala ngati Mulungu, ngati mngelo wa Yehova wowatsogolera.
En ce jour-là, le Seigneur protégera les habitants de Jérusalem, et celui qui d’entre eux tombera en ce jour-là sera comme David, et la maison de David comme une maison à Dieu, comme un ange du Seigneur en leur présence.
9 Pa tsiku limenelo ndidzawononga mitundu yonse yofuna kuthira nkhondo Yerusalemu.
Et il arrivera qu’en ce jour-là, j’aurai soin de briser toutes les nations qui viennent contre Jérusalem.
10 “Ndipo pa nyumba ya Davide ndi pa anthu okhala mu Yerusalemu ndidzakhuthulirapo mzimu wachisomo ndi wopemphera. Iwo adzandiyangʼana Ine, amene anamubaya, ndipo adzamulirira kwambiri monga momwe munthu amalirira mwana wake mmodzi yekhayo, ndiponso adzamva chisoni kwambiri monga momwe amachitira ndi mwana woyamba kubadwa.
Et je répandrai sur la maison de David et sur les habitants de Jérusalem l’esprit de grâce et de prières; et ils regarderont vers moi, qu’ils ont percé; et ils pleureront amèrement celui qu’ils ont percé, comme ils pleureraient leur fils unique, et ils s’affligeront à son sujet, comme on a coutume de s’affliger à la mort du premier-né.
11 Pa tsiku limenelo mudzakhala kulira kwakukulu mu Yerusalemu, monga kulira kwa ku Hadadi-Rimoni ku chigwa cha Megido.
En ce jour-là, il y aura un grand pleur dans Jérusalem, comme le pleur d’Adadremmon dans la plaine de Mageddon.
12 Dziko lidzalira kwambiri, fuko lililonse pa lokha, akazi awo pa okhanso: fuko la Davide pamodzi ndi akazi awo, fuko la Natani pamodzi ndi akazi awo,
La terre pleurera, familles et familles à part; les familles de la maison de David à part, et leurs femmes à part;
13 nyumba ya Levi pamodzi ndi akazi awo, fuko la Simei pamodzi ndi akazi awo,
Les familles de la maison de Nathan à part, et leurs femmes à part; les familles de la maison de Lévi à part, et leurs femmes à part; les familles de Séméi à part, et leurs femmes à part.
14 ndiponso mafuko onse pamodzi ndi akazi awo.
Toutes les autres familles, familles et familles à part, et leurs femmes à part.